< Ézéchiel 3 >

1 Et il me dit: Fils d’un homme, tout ce que tu trouveras, mange-le, mange ce livre, et va parler aux fils d’Israël.
Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
2 Et j’ouvris ma bouche, et il me fit manger ce livre;
Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
3 Et il me dit: Fils d’un homme, ton ventre mangera; et tes entrailles seront remplies de ce livre que moi je te donne. Et je le mangeai, et il fut dans ma bouche comme un miel doux.
Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
4 Et il me dit: Fils d’un homme, va à la maison d’Israël, et tu leur diras mes paroles.
Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
5 Car ce n’est pas vers un peuple d’un langage profond et d’une langue inconnue, que tu seras envoyé, mais à la maison d’Israël;
Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
6 Ni à des peuples nombreux, d’un langage profond et d’une langue inconnue, et dont tu ne puisses pas entendre les paroles; et si tu étais envoyé vers eux, ils t’écouteraient.
Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
7 Mais la maison d’Israël ne veut pas t’écouter, parce qu’elle ne veut pas m’écouter; car toute la maison d’Israël est d’un front d’airain et d’un cœur dur.
Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
8 Voilà que j’ai rendu ta face plus ferme que leurs faces, et ton front plus dur que leurs fronts.
Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
9 Comme un diamant, comme une pierre, j’ai rendu ta face; ne les crains pas, ne redoute pas leur face, parce que c’est une maison qui m’exaspère.
Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
10 Et il me dit: Fils d’un homme, toutes les paroles que moi je te dis, prends-les dans ton cœur, et écoute-les de tes oreilles;
Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
11 Et va, rejoins la transmigration, les fils de ton peuple; tu leur parleras, et tu leur diras: Voici ce que dit le Seigneur Dieu; pour voir si par hasard ils écouteront et s’ils y manqueront.
Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
12 Et un esprit m’enleva, et j’entendis derrière moi la voix d’une grande commotion: Bénie la gloire du Seigneur de son lieu;
Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
13 Et j’entendis la voix des ailes des animaux, qui les frappaient l’une contre l’autre, et la voix des roues qui suivaient les animaux, et la voix d’une grande commotion.
Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
14 Un esprit donc me souleva et m’emporta; et je m’en allai plein d’amertume dans l’indignation de mon esprit: mais la main du Seigneur était avec moi, me fortifiant.
Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
15 Et je vins à la transmigration, près d’un tas de nouveaux fruits, vers ceux qui habitaient le long du fleuve de Chobar; et je m’assis où ils étaient assis, et je demeurai là sept jours triste au milieu d’eux.
Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
16 Mais lorsque furent passés les sept jours, la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
17 Fils d’un homme, je t’ai établi sentinelle dans la maison d’Israël; tu entendras de ma bouche une parole, et tu la leur annonceras de ma part.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
18 Si, moi disant à l’impie: Tu mourras de mort, tu ne le lui annonces pas, et ne lui parles pas pour qu’il se détourne de sa voie impie, et qu’il vive, l’impie lui-même dans son iniquité mourra; mais je redemanderai son sang à ta main.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
19 Mais si tu l’annonces à l’impie, et qu’il ne se détourne pas de son impiété et de sa voie impie, lui-même, à la vérité, mourra dans son iniquité; mais toi, tu auras délivré ton âme.
Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
20 Mais si le juste abandonne sa justice et commet l’iniquité, je mettrai une pierre d’achoppement devant lui; il mourra lui-même, parce que tu ne le lui as pas annoncé; il mourra dans son péché, et il ne sera pas mémoire de ses œuvres de justice qu’il a faites; mais je te redemanderai son sang.
“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
21 Mais si toi, tu annonces au juste de ne pas pécher, et que lui ne pèche pas; vivant, il vivra, parce que tu lui as annoncé, et toi, tu as délivré ton âme.
Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
22 Et la main du Seigneur fut sur moi, et il me dit: Lève-toi, sors dans la campagne, et là je te parlerai.
Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
23 Et je me levai, et je sortis dans la plaine; et voici que là était la gloire du Seigneur, comme la gloire que je vis près du fleuve de Chobar; et je tombai sur ma face.
Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
24 Et un esprit entra en moi et m’établit sur mes pieds, et le Seigneur me parla et il me dit: Entre, enferme-toi au milieu de ta maison.
Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
25 Et toi, fils d’un homme, voici qu’on met sur toi des chaînes; ils t’en lieront, et tu ne sortiras pas du milieu d’eux.
Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
26 Et je ferai que ta langue s’attachera à ton palais; et tu seras muet, et non plus comme un homme qui réprimande; parce que c’est une maison qui m’exaspère.
Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
27 Mais, lorsque je t’aurai parlé, j’ouvrirai ta bouche et tu leur diras: Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Que celui qui écoute, écoute; que celui qui y manque, y manque; car c’est une maison qui m’exaspère.
Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”

< Ézéchiel 3 >