< Ézéchiel 27 >
1 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Toi donc, fils d’un homme, fais entendre sur Tyr des lamentations;
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 Et tu diras à Tyr, qui habite à l’entrée de la mer, au siège du commerce des peuples pour des îles nombreuses: Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Ô Tyr, tu as dit, je suis d’une parfaite beauté,
Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 Et située au milieu de la mer.: Tes voisins qui t’ont bâtie ont mis le comble à ta beauté,
Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 C’est avec les sapins du Sanir qu’ils t’ont construite ainsi que tous tes étages qui plongent dans la mer; ils ont pris un cèdre du Liban pour te faire un mât.
Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
6 Ils ont poli des chênes de Basan pour tes rames; et ils ont fait tes bancs avec l’ivoire des Indes, et les prétorioles avec le bois des îles d’Italie.
Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Le byssus varié d’Egypte a été tissu en forme de voile pour être mis sur ton mât; l’hyacinthe et la pourpre des îles d’Elisa sont devenues ta couverture.
Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
8 Les habitants de Sidon et d’Arad ont été tes rameurs; tes sages, ô Tyr, sont devenus tes pilotes.
Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 Les vieillards de Gébal et ses hommes habiles ont eu des nautoniers pour le service de tout ton équipage; tous les vaisseaux de la mer et leurs nautoniers ont été engagés dans ton commerce.
Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 Les Perses, et les Lydiens, et les Lybiens étaient dans ton armée, tes hommes de guerre; ils ont suspendu chez toi la cuirasse et le bouclier pour ton ornement.
“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 Les fils d’Arad, et ton armée, étaient sur tes murs tout autour; et aussi les Pygmées qui étaient sur tes tours ont suspendu leurs carquois à tes murs tout autour; ils ont mis eux-mêmes le comble à ta beauté.
Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 Les Carthaginois qui négociaient avec toi par l’abondance de toutes les richesses, ont rempli tes foires d’argent, de fer, d’étain, et de plomb.
“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 La Grèce, Thubal et Mosoch étaient tes courtiers; ils ont amené des esclaves et des vases d’airain à ton peuple.
“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 De la maison de Thogorma on amenait des chevaux, des cavaliers et des mulets à ton marché.
“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 Les fils de Dédan ont négocié avec toi; beaucoup d’îles ont négocié par tes mains; elles t’ont donné des dents d’ivoire et de l’ébène en échange de tes marchandises.
“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 Le Syrien qui négociait avec toi à cause de la multitude de tes ouvrages, a exposé dans ton marché des pierreries et de la pourpre, et des vêtements de tricot, et du byssus, et de la soie, et du chodchod.
“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 Juda et la terre d’Israël étaient aussi tes courtiers; ils ont exposé dans tes foires du froment de première qualité, du baume, du miel, de l’huile et de la résine.
“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 Damas, qui négociait avec toi, te donnait pour la multitude de tes ouvrages une multitude de différentes richesses, du vin généreux, des laines de la couleur la plus belle.
“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
19 Dan, et la Grèce et Mosel dans tes foires ont exposé du fer travaillé; il y avait du stacté et de la canne dans ton commerce.
Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 Dédan était ton courtier pour les tapis à s’asseoir.
“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 L’Arabie et tous les princes de Cédar ont négocié par tes mains; avec des agneaux, et des béliers, et des boucs, ils sont venus vers toi étant en commerce avec toi.
“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 Les marchands de Saba et de Réema eux-mêmes ont négocié avec toi en toutes sortes d’excellents aromates, en pierres précieuses, et en or qu’ils ont exposé dans ton marché.
“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 Haran, et Chené, et Eden ont négocié avec toi; Saba, Assur et Chelmad t’ont vendu leurs marchandises.
“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 Eux aussi trafiquaient avec toi de bien des manières pour des balles d’hyacinthe, de tissus de diverses couleurs et de trésors précieux qui étaient enveloppés et attachés avec des cordes; ils avaient encore des cèdres dans leurs trafics avec toi.
Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 Les vaisseaux de la mer étaient tes princes dans ton commerce; tu as été comblée de richesses et extrêmement glorifiée au milieu de la mer.
“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Tes rameurs t’ont conduite sur les grandes eaux; mais le vent du midi t’a brisée au fond de la mer.
Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
27 Tes richesses, et tes trésors, et ton nombreux équipage, tes nautoniers, tes pilotes qui avaient en garde les objets à ton usage et commandaient à tes gens; et aussi tous les hommes de guerre qui étaient en toi, avec toute la multitude qui se trouve au milieu de toi, tomberont au fond de la mer au jour de ta ruine.
Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
28 Au bruit de la clameur de tes pilotes, les flots seront troublés;
Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 Et ils descendront de leurs vaisseaux, tous ceux qui tenaient la rame; les nautoniers et tous les pilotes de la mer se tiendront sur la terre.
Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 Ils se lamenteront sur toi à haute voix, et pousseront des cris amers; et ils jetteront de la poussière sur leurs têtes et se couvriront de cendre.
Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 Et ils raseront à cause de toi leur chevelure et se ceindront de cilices; et ils te pleureront dans l’amertume de l’âme d’un pleur très amer.
Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
32 Et ils entonneront sur toi un chant lugubre, et se désoleront à ton sujet, disant: Quelle ville est comme Tyr, et quelle ville est devenue muette au milieu de la mer?
Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
33 Toi qui, en faisant sortir tes marchandises de la mer, as comblé de biens des peuples nombreux, qui, par la multitude de tes richesses et de tes peuples, as enrichi des rois de la terre;
Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
34 Maintenant tu as été brisée par la mer; tes richesses et toute la multitude qui était au milieu de toi sont tombées au profond des eaux.
Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
35 Tous les habitants des îles seront frappés de stupeur sur loi; et tous leurs rois battus par cette tempête ont changé de visage.
Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
36 Les marchands de tous les peuples ont sifflé sur toi: tu as été réduite au néant, et tu ne seras plus à jamais.
Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”