< Ézéchiel 21 >

1 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils d’un homme, tourne ton visage vers Jérusalem; fais tomber tes paroles sur les sanctuaires, et prophétise contre la terre d’Israël;
“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
3 Et tu diras à la terre d’Israël: Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Voici que je viens vers toi; et je tirerai le glaive de son fourreau, et je tuerai en toi le juste et l’impie;
Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
4 Mais parce que j’ai tué en toi le juste et l’impie, pour cela même mon glaive sortira de son fourreau contre toute chair, du midi jusqu’à l’aquilon;
Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
5 Afin que toute chair sache que moi le Seigneur j’ai tiré de son fourreau mon irrévocable glaive.
Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
6 Et toi, fils d’un homme, gémis jusqu’au brisement de tes reins, et avec amertume gémis devant eux.
“Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
7 Et lorsqu’ils te diront: Pourquoi gémis-tu? tu diras: À cause de ce que j’ai entendu et qui vient; et tout cœur se fondra, et toutes les mains deviendront défaillantes, et tout esprit sera sans force, et l’eau coulera de tous les genoux; voici que cela vient, et que cela s’accomplira, dit le Seigneur Dieu.
Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
8 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anandiyankhulanso kuti,
9 Fils d’un homme, prophétise, et dis: Voici ce que dit le Seigneur Dieu. Dis: Le glaive, le glaive a été aiguisé et poli.
“Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
10 C’est afin de tuer des victimes qu’il a été aiguisé; c’est afin de briller qu’il a été poli; toi qui abats le sceptre de mon fils, tu as coupé tout arbre par le pied.
Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
11 Et je l’ai donné à polir pour qu’il soit tenu à la main; il a été aiguisé, ce glaive, et il a été poli, afin qu’il soit dans la main de celui qui tue.
“‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
12 Crie et hurle, fils d’un homme, parce qu’il a été fait pour tuer mon peuple, pour tuer tous les chefs d’Israël qui avaient pris la fuite: ils ont été livrés au glaive avec mon peuple; c’est pourquoi frappe sur ta cuisse,
Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
13 Parce qu’il a été éprouvé; et ce sceptre, lorsqu’il l’aura renversé, ne sera plus, dit le Seigneur Dieu.
“‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
14 Toi donc, fils d’un homme, prophétise, frappe des mains, et qu’il soit doublé le glaive, et qu’il soit triplé le glaive des tués; c’est le glaive de la grande tuerie, lequel les frappe de stupeur,
“Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
15 Et fait fondre les cœurs et multiplie les ruines. À toutes leurs portes j’ai jeté l’épouvante du glaive aiguisé et poli pour briller, engaîné pour le carnage.
Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
16 Aiguise-toi, va à droite ou à gauche, partout où tu désires porter ta face.
Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
17 Bien plus, moi-même je frapperai des mains et j’assouvirai mon indignation; c’est moi le Seigneur qui ai parlé.
Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
18 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anandiyankhulanso kuti,
19 Et toi, fils de l’homme, pose-toi deux voies, afin que vienne le glaive du roi de Babylone; toutes deux sortiront d’une seule terre; et c’est de la main qu’il tirera sa conjecture, et à la tête de la voie de la cité qu’il conjecturera.
“Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
20 Tu feras une voie, afin que vienne le glaive à Rabbath des fils d’Ammon, et à Juda contre Jérusalem, ville très fortifiée.
Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
21 Car le roi de Babylone s’est arrêté à la double voie, à la tête des deux chemins, cherchant un augure, mêlant les flèches: il a interrogé les idoles, il a consulté les entrailles,
Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
22 À sa droite le sort est tombé sur Jérusalem, afin qu’il place des béliers, qu’il ouvre sa bouche pour le carnage, qu’il élève la voix avec un hurlement, qu’il place des béliers contre les portes, qu’il forme un rempart et qu’il bâtisse des fortifications.
Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
23 Et il sera à leurs yeux comme consultant vainement un oracle, et imitant le repos des sabbats; mais lui-même se souviendra de leur iniquité, pour prendre Jérusalem.
Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
24 C’est pourquoi voici ce que dit le Seigneur Dieu: Parce que vous vous êtes souvenus de votre iniquité, et que vous avez révélé vos prévarications, et que vos péchés ont paru dans toutes vos pensées; parce que, dis-je, vous vous en êtes souvenus, vous serez saisis par sa main.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
25 Mais toi, profane, chef impie d’Israël, dont le jour marqué d’avance est venu dans le temps de la punition de ton iniquité;
“‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
26 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Ôte la tiare, enlève la couronne; n’est-ce pas cette couronne qui a élevé l’homme et humilié le grand?
Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
27 Je la montrerai iniquité, iniquité, iniquité [mais cela n’arriva pas jusqu’à ce que vînt celui à qui appartient le jugement], et je la lui livrerai.
Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
28 Et toi, fils d’un homme, prophétise et dis: Voici ce que dit le Seigneur Dieu aux fils d’Ammon, et pour leur opprobre: Glaive, glaive, sors du fourreau pour tuer, polis-toi, afin que tu lues et que tu brilles,
“Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
29 Lorsqu’on voit pour toi des choses vaines, et qu’on prédit des mensonges, afin que tu tombes sur le cou des impies blessés à mort, dont le jour marqué d’avance est venu dans le temps de la punition de leur iniquité.
Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
30 Rentre dans ton fourreau, dans le lieu où tu as été créé, dans la terre de ta naissance je te jugerai;
“‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
31 Et je verserai sur toi mon indignation: dans le feu de ma fureur je soufflerai sur toi, et je t’abandonnerai aux mains d’hommes insensés, et qui ont machiné ta perte.
Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
32 Du feu tu seras la pâture, ton sang sera répandu au milieu de la terre, tu seras livré à l’oubli, parce que c’est moi le Seigneur qui ai parlé.
Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”

< Ézéchiel 21 >