< Ézéchiel 15 >
1 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
2 Fils d’un homme, que fera-t-on de l’arbre de la vigne entre tous les arbres des bois, qui sont parmi les arbres des forêts?
“Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
3 Est-ce qu’on prendra du bois de la vigne pour faire un ouvrage, ou en façonnera-t-on une cheville pour y suspendre un objet quelconque?
Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
4 Voilà qu’on le met au feu, pour en être la proie; le feu consume les deux extrémités, et le milieu est réduit en cendre brûlante; est-ce qu’il sera utile pour un ouvrage?
Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
5 Et même lorsqu’il était entier, il n’était propre à aucun ouvrage; combien plus, lorsque le feu l’aura dévoré et entièrement brûlé, on n’en fera aucun ouvrage?
Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
6 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu: Comme l’arbre de la vigne parmi les arbres des forêts, que j’ai mis au feu pour le dévorer, ainsi je livrerai les habitants de Jérusalem.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
7 Et je tournerai ma face contre eux; ils sortiront du feu, et le feu les consumera; et vous saurez que je suis le Seigneur, lorsque j’aurai tourné ma face contre eux,
Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
8 Et que j’aurai rendu la terre inaccessible et désolée, parce qu’ils se sont montrés prévaricateurs, dit le Seigneur Dieu.
Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”