< Ézéchiel 13 >
1 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
2 Adresse tes prédictions aux prophètes d’Israël qui prophétisent, et tu diras à ceux qui prophétisent d’après leur cœur: Ecoutez la parole du Seigneur.
“Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
3 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Malheur aux prophètes insensés qui suivent leur esprit, et ne voient rien.
Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
4 Tes prophètes, Israël, étaient comme des renards dans les déserts.;
Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
5 Vous n’êtes pas montés à la rencontre de l’ennemi, vous n’avez pas opposé un mur pour la maison d’Israël, afin de tenir ferme dans le combat au jour du Seigneur.
Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
6 Ils voient des choses vaines, et ils prophétisent le mensonge, disant: Le Seigneur dit, lorsque le Seigneur ne les a pas envoyés; et ils persistent à maintenir leur discours.
Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
7 Est-ce que vous n’avez pas vu une vision vaine, et annoncé une prédiction mensongère? et vous dites: Le Seigneur dit, lorsque moi je n’ai pas parlé.
Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
8 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu: Parce que vous avez dit des choses vaines, et que vous avez vu le mensonge; c’est pourquoi, voici que moi je suis contre vous, dit le Seigneur Dieu.
“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
9 Et ma main sera sur les prophètes qui voient des choses vaines, et qui prédisent le mensonge; ils ne seront pas dans le conseil de mon peuple, et ils ne seront point écrits dans le livre de la maison d’Israël, et ils n’entreront pas dans la terre d’Israël, et vous saurez que je suis le Seigneur Dieu;
Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
10 Parce qu’ils ont trompé mon peuple, disant: Paix, et il n’y a point de paix; et lui bâtissait une muraille; mais eux l’enduisaient de boue, sans paille.
“Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
11 Dis à ceux qui enduisent sans mélange, que la muraille tombera; car viendra une pluie inondante, et je lancerai des pierres énormes qui tomberont d’en haut, et un vent de tempête qui la renversera.
choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
12 Si toutefois la muraille tombe, ne vous dira-t-on pas: Où est l’enduit dont vous l’avez enduite?
Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
13 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu: Je ferai éclater un vent de tempêtes dans mon indignation, et une pluie inondante se répandra dans ma fureur, et dans ma colère des pierres énormes consumeront tout.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
14 Et je détruirai la muraille que vous avez enduite sans mélange; et je l’égalerai à la terre, et ses fondements seront mis à nu; et elle tombera; et celui qui l’avait enduite sera consumé au milieu d’elle; et vous saurez que moi je suis le Seigneur.
Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
15 Et j’assouvirai mon indignation contre la muraille, et contre ceux qui l’enduisent sans mélange, et je vous dirai: La muraille n’est plus, et ceux qui l’ont enduite ne sont plus.
Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
16 Ils ne sont plus, les prophètes d’Israël qui prophétisent à Jérusalem, et qui voient pour elle une vision de paix; et il n’y a point de paix, dit le Seigneur Dieu.
Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
17 Et toi, fils d’un homme, tourne ta face contre les filles de ton peuple qui prophétisent d’après leur cœur, et fais des prédictions contre elles,
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
18 Et dis: Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Malheur à celles qui cousent des coussinets pour tous les coudes, et qui font des oreillers sous la tête des personnes de tout âge, afin de s’emparer des âmes; et lorsqu’elles s’emparaient des âmes de mon peuple, elles les vivifiaient.
Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
19 Elles me déshonoraient auprès de mon peuple pour un peu d’orge et un morceau de pain, afin de tuer les âmes qui n’étaient pas mortes, et de vivifier les âmes qui ne vivaient pas, mentant à mon peuple, qui croit aux mensonges.
Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
20 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu: Voici que moi je suis contre vos coussinets avec lesquels vous prenez des âmes au vol, je les déchirerai de dessus vos bras, et je laisserai aller les âmes que vous avez prises, ces âmes pour qu’elles s’envolent.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
21 Et je déchirerai vos oreillers; et je délivrerai mon peuple de votre main, et ils ne seront plus en vos mains comme une proie; et vous saurez que je suis le Seigneur,
Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
22 Parce que vous avez affligé en mentant le cœur du juste, que moi je n’ai pas contristé; et parce que vous avez fortifié les mains de l’impie, afin qu’il ne revînt point de sa voie mauvaise, et qu’il ne trouvât point la vie;
Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
23 À cause de cela, vous ne verrez plus de choses vaines, et vous ne ferez plus de prédictions, et j’arracherai mon peuple de votre main, et vous saurez que je suis le Seigneur.
choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”