< Exode 38 >

1 Il fit encore l’autel de l’holocauste de bois de sétim, de cinq coudées en carré, et de trois en hauteur.
Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
2 Les cornes de l’autel sortaient des quatre angles, et il le couvrit de lames d’airain.
Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
3 Et pour les usages de l’autel il prépara les divers vases d’airain, les chaudières, les pincettes, les fourchettes, les crocs et les brasiers.
Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 Il fit aussi la grille de l’autel d’airain, en forme de rets, et au-dessous, le foyer au milieu de l’autel,
Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
5 Quatre anneaux ayant été jetés en fonte pour les quatre sommités de la grille, afin d’y passer les leviers pour porter l’autel.
Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
6 Il fit ces leviers eux-mêmes de bois de sétim, et il les couvrit de lames d’airain,
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
7 Et il les passa dans les anneaux qui saillaient sur les côtés de l’autel. Mais l’autel lui-même n’était pas massif, mais creux, composé d’ais et vide au dedans.
Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
8 Il fit de plus le bassin d’airain avec sa base, des miroirs des femmes qui veillaient à la porte du tabernacle.
Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
9 Il fit encore le parvis, au côté austral duquel étaient les rideaux de fin lin retors, de cent coudées.
Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 Vingt colonnes d’airain avec leurs soubassements; les chapiteaux des colonnes et tous les ornements du travail étaient d’argent.
Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 Egalement du côté septentrional les colonnes, les soubassements et les chapiteaux des colonnes étaient de la même mesure, du même travail et du même métal.
Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 Mais au côté qui regarde l’occident, les rideaux étaient de cinquante coudées, les dix colonnes avec leurs soubassements étaient d’airain, et les chapiteaux des colonnes et tous les ornements de ce travail, d’argent.
Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
13 Or, contre l’orient il disposa des rideaux de cinquante coudées,
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
14 Sur lesquelles un côté ayant trois colonnes avec ses soubassements prenait quinze coudées,
Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
15 Et l’autre côté (puisque c’est entre l’un et l’autre qu’il fit l’entrée du tabernacle) prenait également quinze coudées par les rideaux, par trois colonnes et autant de soubassements.
polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Tous les rideaux du parvis avaient été tissus de fin lin retors.
Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
17 Les soubassements des colonnes étaient d’airain, et leurs chapiteaux avec tous leurs ornements, d’argent; mais les colonnes elles-mêmes du parvis, il les revêtit d’argent.
Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
18 Et à l’entrée du parvis, il fit en ouvrage de brodeur un rideau d’hyacinthe, de pourpre, d’écarlate et de fin lin retors lequel avait la hauteur était de cinq coudées, selon la mesure que tous les rideaux du parvis avaient.
Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
19 Mais il y avait quatre colonnes à l’entrée avec leurs soubassements d’airain; et leurs chapiteaux et leurs ornements étaient d’argent.
pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
20 Il fit aussi autour du tabernacle et du parvis les pieux d’airain.
Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
21 Telles sont les parties du tabernacle du témoignage, qui furent énumérées par Tordre de Moïse pour les cérémonies des Lévites par l’entremise d’Ithamar fils d’Aaron, le prêtre,
Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
22 Et que Béséléel, fils d’Uri, fils de Hur, de la tribu de Juda, le Seigneur l’ordonnant par Moïse avait achevé,
Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
23 Après s’être adjoint Ooliab, fils d’Achisamech de la tribu de Dan, qui était aussi lui-même ouvrier habile en bois, tisseur en diverses couleurs, et brodeur en hyacinthe, en pourpre, en écarlate et en fin lin.
pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
24 Tout l’or qui fut dépensé pour le travail du sanctuaire et qui fut offert en dons, fut de vingt-neuf talents et de sept cent trente sicles, selon la mesure du sanctuaire.
Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
25 Or ces offrandes furent faites par ceux qui entrèrent dans le dénombrement, depuis vingt ans et au-dessus, au nombre de six cent trois mille et cinq cent cinquante portant les armes.
Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
26 Il y eut de plus cent talents d’argent, dont furent fondus les soubassements du sanctuaire et l’entrée où le voile était suspendu.
Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
27 Cent soubassements furent faits avec cent talents, un talent supputé pour chaque soubassement.
Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
28 Mais avec les mille sept cent et soixante-quinze sicles il fit les chapiteaux des colonnes, qu’il revêtit aussi d’argent.
Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
29 On offrit encore deux mille et soixante-dix talents d’airain, et de plus quatre cents sicles,
Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
30 Dont furent fondus les soubassements à l’entrée du tabernacle de témoignage, l’autel d’airain avec sa grille, tous les vases qui appartiennent à son usage,
Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
31 Les soubassements du parvis, tant autour qu’à son entrée, et les pieux du tabernacle et du parvis tout autour.
matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

< Exode 38 >