< Exode 31 >
1 Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
2 Voici, j’ai appelé nommément Béséléel, fils d’Uri, fils de Hur de la tribu de Juda,
“Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
3 Et je l’ai rempli de l’esprit de Dieu, de sagesse, d’intelligence et de science pour toute sorte d’ouvrage,
Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
4 Pour inventer tout ce qui peut se faire par l’art avec l’or, l’argent et l’airain,
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
5 Avec du marbre, des pierres précieuses et divers bois.
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
6 Et je lui ai donné pour compagnon Ooliab, fils d’Achisamech de la tribu de Dan. Et dans le cœur de tout ouvrier habile j’ai mis de la sagesse, afin qu’ils fassent tout ce que je t’ai ordonné:
Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
7 Le tabernacle d’alliance, l’arche de témoignage, le propitiatoire qui est dessus, et tous les vases du tabernacle;
Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
8 La table et ses vases, le chandelier très pur avec ses vases, et les autels du parfum à brûler,
tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
9 Et de l’holocauste et tous leurs vases, le bassin avec sa base;
guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
10 Les vêtements saints du ministère pour Aaron, le grand-prêtre et ses fils, afin qu’ils s’acquittent de leur office dans les choses sacrées;
ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
11 L’huile de l’onction, le parfum à brûler composé d’aromates pour le sanctuaire: ainsi, ils feront tout ce que je t’ai ordonné.
ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
12 Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
13 Parle aux enfants d’Israël, et tu leur diras: Ayez soin de garder mon sabbat, parce qu’il est un signe entre moi et vous en vos générations, afin que vous sachiez que c’est moi, le Seigneur, qui vous sanctifie.
“Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
14 Gardez mon sabbat, car il est saint pour vous: celui qui le profanera mourra de mort; celui qui travaillera en ce jour-là, son âme périra du milieu de son peuple.
“Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
15 Pendant six jours vous travaillerez, au septième jour c’est un sabbat, repos saint pour le Seigneur, quiconque travaillera en ce jour-là, mourra.
Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
16 Que les enfants d’Israël gardent le sabbat, et qu’ils le célèbrent en leurs générations. C’est un pacte éternel
Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
17 Entre moi et les enfants d’Israël et un signe perpétuel; car c’est en six jours que le Seigneur a fait le ciel et la terre, et au septième il a cessé son œuvre.
Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
18 Or, le Seigneur ayant achevé les discours de cette sorte sur la montagne de Sinaï, donna à Moïse les deux tables de pierre du témoignage, écrites du doigt de Dieu.
Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.