< Exode 24 >

1 Dieu dit aussi à Moïse: Monte vers le Seigneur, toi et Aaron, Nadab et Abiu, et les soixante dix anciens d’Israël, et vous adorerez de loin.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali.
2 Et Moïse seul montera vers le Seigneur, et eux ne s’approcheront pas, et le peuple ne montera pas avec lui.
Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”
3 Moïse vint donc et raconta au peuple toutes les paroles du Seigneur et ses ordonnances, et tout le peuple répondit d’une seule voix: Nous accomplirons toutes les paroles que le Seigneur a dites.
Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.”
4 Or Moïse écrivit tous les discours du Seigneur, et le matin, se levant, il bâtit un autel au pied de la montagne et douze monuments selon les douze tribus d’Israël.
Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena. Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
5 Et il envoya les jeunes gens d’entre les enfants d’Israël, et ils offrirent des holocaustes, et ils immolèrent des victimes pacifiques au Seigneur, des veaux.
Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano.
6 C’est pourquoi Moïse prit la moitié du sang et la mit dans des coupes; mais la partie qui restait, il la répandit sur l’autel.
Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe.
7 Prenant ensuite le livre de l’alliance, il lut, le peuple écoutant, lequel dit: Tout ce que le Seigneur a dit, nous le ferons, et nous serons obéissants.
Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”
8 Or Moïse ayant pris le sang, le répandit sur le peuple, et dit: Voici le sang de l’alliance que le Seigneur a faite avec vous selon toutes ces paroles.
Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”
9 Alors montèrent, Moïse et Aaron, Nadab et Abiu, et les soixante-dix anciens d’israël;
Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri,
10 Et ils virent le Dieu d’Israël, et sous ses pieds comme un ouvrage de pierre de saphir, et comme le ciel, lorsqu’il est serein.
ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo.
11 Et Dieu ne lança pas sa main sur ceux des enfants d’Israël qui s’étaient retirés au loin; et ils virent Dieu, puis ils mangèrent et ils burent.
Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.
12 Or le Seigneur dit à Moïse: Monte vers moi sur la montagne, et sois là: je te donnerai les tables de pierre, et la loi et les commandements que j’ai écrits, afin que tu les enseignes.
Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”
13 Moïse et Josué son serviteur se levèrent; et Moïse montant sur la montagne de Dieu,
Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.
14 Dit aux anciens; Attendez ici jusqu’à ce que nous retournions à vous. Vous avez Aaron et Hur avec vous; s’il naît quelque question, vous leur en ferez le rapport.
Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”
15 Et lorsque Moïse fut monté, la nuée couvrit la montagne.
Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo.
16 Et la gloire du Seigneur reposa sur Sinaï, le couvrant de la nuée pendant six jours; mais au septième jour il appela Moïse du milieu de l’obscurité.
Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo.
17 Or l’aspect de la gloire du Seigneur était comme un feu ardent sur le sommet de la montagne, en la présence des enfants d’Israël.
Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo.
18 Et Moïse étant entré au milieu de la nuée, monta sur la montagne, et il fut là quarante jours et quarante nuits.
Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.

< Exode 24 >