< Deutéronome 4 >
1 Maintenant, Israël, écoute les préceptes et les ordonnances que moi je t’enseigne, afin que les pratiquant, tu vives, et que tu possèdes, en y entrant, la terre que le Seigneur Dieu de vos pères va vous donner.
Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
2 Vous n’ajouterez point à la parole que je vous dis, et vous n’en retrancherez point: gardez les commandements du Seigneur votre Dieu que moi, je vous prescris.
Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
3 Vos yeux ont vu tout ce qu’a fait le Seigneur contre Béelphégor, comment il a brisé tous ses adorateurs du milieu de vous.
Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
4 Mais vous qui êtes attachés au Seigneur votre Dieu, vous vivez tous jusqu’au présent jour.
Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
5 Vous savez que je vous ai enseigné les préceptes et les lois, comme m’a commandé le Seigneur mon Dieu: ainsi, vous les pratiquerez dans la terre que vous allez posséder;
Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
6 Vous les observerez et les accomplirez par vos œuvres. Car telles sont votre sagesse et votre intelligence devant les peuples, afin qu’entendant parler de tous ces préceptes, ils disent: Voici un peuple sage et intelligent, une grande nation.
Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
7 Et il n’est point d’autre nation, si grande qu’elle soit, qui ait des dieux s’approchant délie, comme notre Dieu, qui est présent à toutes nos prières.
Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
8 Quelle est, en effet, l’autre nation assez illustre pour qu’elle ait des cérémonies, des ordonnances justes, et toute cette loi que j’exposerai aujourd’hui devant vos yeux?
Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
9 Garde-toi donc toi-même et ton âme soigneusement. N’oublie point les paroles qu’ont vues tes yeux, et qu’elles ne sortent point de ton cœur tous les jours de ta vie. Tu les enseigneras à tes fils et à tes petits-fils,
Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
10 Depuis le jour que tu t’es trouvé devant le Seigneur ton Dieu à Horeb, quand le Seigneur me parla, disant: Assemble auprès de moi le peuple, afin qu’ils entendent mes paroles, et qu’ils apprennent à me craindre tout le temps qu’ils vivront sur la terre, et qu’ils instruisent leurs enfants.
Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
11 Et vous vous approchâtes du pied de la montagne, qui brûlait jusqu’au ciel; et il y avait sur elle des ténèbres, un nuage et une obscurité.
Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
12 Et le Seigneur vous parla du milieu du feu. Vous entendîtes la voix de ses paroles, mais de forme, vous n’en vîtes absolument point.
Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
13 Il vous fit connaître son alliance, qu’il vous ordonna d’accomplir, et les dix paroles qu’il écrivit sur deux tables de pierre.
Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
14 Et à moi, il me commanda, en ce temps-là, de vous enseigner des cérémonies et des ordonnances que vous deviez accomplir dans la terre que vous allez posséder.
Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
15 Gardez donc soigneusement vos âmes. Vous n’avez vu aucune représentation au jour que le Seigneur vous parla à Horeb, du milieu du feu;
Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
16 De peur que, séduits, vous ne vous fassiez quelque représentation taillée au ciseau, ou bien quelque image d’homme ou de femme;
kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
17 Quelque représentation de toutes les bêtes qui sont sur la terre, ou des oiseaux qui volent sous le ciel,
kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
18 Et des reptiles qui se meuvent sur la terre, ou des poissons qui sous la terre demeurent dans les eaux;
Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
19 De peur que, les yeux levés au ciel, tu ne voies le soleil, la lune et tous les astres du ciel, et que, séduit par l’erreur, tu ne les adores, et tu n’offres un culte à des choses que le Seigneur ton Dieu a créées pour servir à toutes les nations qui sont sous le ciel.
Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
20 Pour vous, le Seigneur vous a tirés et ramenés de la fournaise de fer de l’Egypte, pour avoir un peuple héréditaire, comme il est au présent jour.
Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
21 Et le Seigneur s’est irrité contre moi, à cause de vos discours, et il a juré que je ne passerai pas le Jourdain, et que je n’entrerai pas dans la terre excellente qu’il va vous donner.
Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
22 Voici donc que je meurs en ce pays; je ne passerai point le Jourdain; vous, vous le passerez, et vous posséderez cette belle terre.
Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
23 Prends garde d’oublier jamais l’alliance du Seigneur ton Dieu, qu’il a établie avec toi, et de te faire quelque représentation taillée au ciseau des choses dont le Seigneur a défendu d’en faire,
Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
24 Parce que le Seigneur ton Dieu est un feu consumant, un Dieu jaloux.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
25 Si vous engendrez des enfants et des petits-enfants, et que vous demeuriez dans cette terre, et que, séduits, vous fassiez quelque représentation, commettant le mal devant le Seigneur votre Dieu, en sorte que vous le provoquiez au courroux,
Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
26 J’invoque à témoin aujourd’hui le ciel et la terre que bientôt vous serez exterminés de la terre, que, le Jourdain passé, vous allez posséder; vous n’y habiterez pas longtemps, mais le Seigneur vous détruira,
ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
27 Et vous dispersera dans tous les peuples, et vous resterez en petit nombre parmi les nations, chez lesquelles le Seigneur doit vous conduire.
Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
28 Et là vous servirez des dieux qui ont été fabriqués par la main des hommes, du bois et de la pierre, qui ne voient, ni n’entendent, ni ne mangent, ni ne flairent.
Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
29 Mais, lorsque tu chercheras là le Seigneur ton Dieu, tu le trouveras, si cependant c’est de tout ton cœur que tu le cherches, et dans toute l’affliction de ton âme.
Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
30 Après que te seront arrivées toutes les choses qui ont été prédites, tu reviendras, dans le dernier temps, au Seigneur ton Dieu, et tu écouteras sa voix,
Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
31 Parce que c’est un Dieu miséricordieux, le Seigneur ton Dieu; il ne t’abandonnera point, et il ne te détruira pas entièrement, et il n’oubliera pas l’alliance qu’il a jurée à tes pères.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
32 Demande aux jours anciens qui ont été avant toi, depuis le jour que Dieu a créé l’homme sur la terre, depuis une extrémité du ciel jusqu’à l’autre extrémité, s’il a été fait jamais une chose semblable, ou si jamais il a été connu
Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
33 Qu’un peuple ait entendu la voix de Dieu, parlant du milieu du feu, comme tu l’as entendue, en conservant la vie;
Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
34 Si Dieu a entrepris devenir et de prendre pour lui une nation au milieu des nations, par des épreuves, des signes et des prodiges, par la guerre, par une main forte, un bras étendu et d’horribles visions, selon tout ce qu’a fait pour vous le Seigneur votre Dieu dans l’Egypte, tes yeux le voyant,
Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
35 Afin que tu susses que c’est le Seigneur lui-même qui est Dieu, et qu’il n’en est pas d’autre que lui.
Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
36 Du haut du ciel il t’a fait entendre sa voix pour l’instruire, et sur la terre il t’a montré son feu très ardent, et tu as entendu ses paroles qui sortaient du milieu du feu
Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
37 Parce qu’il a aimé tes pères, et qu’il a choisi leur postérité après eux; et il t’a retiré de l’Egypte, te précédant avec sa grande puissance,
Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
38 Pour détruire à ton entrée des nations très grandes et plus fortes que loi, et pour l’introduire, et te donner leur terre en possession, comme tu vois au présent jour.
kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
39 Sache donc aujourd’hui, et pense en ton cœur, que c’est le Seigneur lui-même qui est Dieu dans le ciel en haut, et sur la terre en bas, et qu’il n’en est pas d’autre.
Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
40 Garde ses préceptes et ses commandements, que moi, je te prescris, afin que bien l’arrivé, à toi et à tes fils après toi, et que tu demeures longtemps sur la terre que le Seigneur ton Dieu va te donner.
Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
41 Alors Moïse sépara trois villes au-delà du Jourdain vers la partie orientale,
Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
42 Afin que s’y réfugie celui qui sans le vouloir aura tué son prochain, et qui n’aura pas été son ennemi un ou deux jours auparavant, et qu’il puisse se retirer dans une de ces villes:
kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
43 Bosor dans le désert, qui est située dans la plate campagne de la tribu de Ruben; Ramolli en Galaad, qui est dans la tribu de Gad, et Golan en Basan, qui est dans la tribu de Manassé.
Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
44 Telle est la loi que Moïse exposa devant les enfants d’Israël;
Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
45 Et telles sont les lois, les cérémonies et les ordonnances qu’il annonça aux enfants d’Israël, quand ils furent sortis de l’Egypte,
Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 Au delà du Jourdain dans la vallée, contre le temple de Phogor dans la terre de Séhon, roi de l’Amorrhéen, qui habita à Hésébon, et que battit Moïse. Les enfants d Israël aussi, sortis de l’Egypte,
Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 Possédèrent sa terre, et la terre d’Og, roi de Basan, deux rois des Amorrhéens qui étaient au-delà du Jourdain, vers le levant,
Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
48 Depuis Aroër qui est sur le bord du torrent d’Arnon, jusqu’à la montagne de Sion, qui est appelée aussi Hermon,
Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
49 Toute la plaine au-delà du Jourdain, vers la partie orientale, jusqu’à la mer du désert, et jusqu’au pied de la montagne de Phasga.
ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.