< Deutéronome 29 >

1 Voici les paroles de l’alliance que le Seigneur ordonna à Moïse de faire avec les enfants d’Israël dans la terre de Moab, outre l’autre alliance qu’il fit avec eux à Horeb.
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 Moïse donc appela tout Israël et leur dit: Vous, vous avez vu tout ce qu’a fait le Seigneur devant vous dans la terre d’Egypte, à Pharaon, à tous ses serviteurs et à toute sa terre,
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 Les grandes épreuves qu’ont vues vos yeux, ces signes et ces prodiges considérables,
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 Et le Seigneur ne vous a pas donné jusqu’au présent jour un cœur intelligent, des yeux voyants et des oreilles qui peuvent entendre.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 Il vous a conduits durant quarante ans à travers le désert: vos vêtements ne se sont pas usés, et la chaussure de vos pieds n’a pas été détruite de vétusté.
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 Vous n’avez pas mangé de pain, vous n’avez pas bu de vin et de cervoise, afin que vous sussiez que c’est moi qui suis le Seigneur votre Dieu.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 Et vous êtes venu en ce lieu, et Séhon, roi d’Hésébon, est sorti, ainsi que Og, roi de Basan, venant au-devant de nous pour le combat. Et nous les avons battus,
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 Et nous avons pris leur terre, et nous l’avons remise, pour la posséder, à Ruben, à Gad et à la demi-tribu de Manassé.
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 Gardez donc les paroles de cette alliance, et accomplissez-les, afin que vous compreniez tout ce que vous faites.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 Vous êtes tous aujourd’hui devant le Seigneur votre Dieu, vos princes, vos tribus, les anciens et les docteurs, tout le peuple d’Israël,
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 Vos enfants et vos femmes, et l’étranger qui demeure avec vous dans le camp, excepté ceux qui coupent le bois, et ceux qui portent l’eau,
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 Afin que tu entres dans l’alliance du Seigneur ton Dieu, et dans le serment que te fait aujourd’hui le Seigneur ton Dieu,
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 Afin qu’il se suscite en toi un peuple, et que lui-même soit ton Dieu, comme il t’a dit, et comme il a juré à tes pères, Abraham, Isaac et Jacob.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 Et ce n’est pas pour vous seuls que moi, je fais cette alliance et je confirme ces serments,
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 Mais c’est pour tous ceux qui sont présents, et pour tous ceux qui sont absents.
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 Car vous, vous savez de quelle manière nous avons habité dans la terre d’Egypte, et de quelle manière nous avons passé au milieu des nations, et qu’en les traversant,
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 Vous avez vu leurs abominations et leurs ordures, c’est-à-dire leurs idoles, du bois, de la pierre, de l’argent et de l’or, qu’ils adoraient.
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 Que s’il y avait parmi vous un homme ou une femme, une famille ou une tribu dont le cœur est aujourd’hui détourné du Seigneur notre Dieu, en sorte qu’il aille et qu’il serve les nations, et qui soit parmi vous une racine produisant du fiel et de l’amertume;
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 Et que quand il aura entendu les paroles de ce serment, il se flatte en lui-même, disant: La paix sera avec moi, et je marcherai dans la perversité de mon cœur: alors que la racine bien abreuvée consume celle qui a soif,
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 Et que le Seigneur ne lui pardonne point; mais que sa fureur et son zèle contre cet homme jettent la fumée la plus épaisse; que toutes les malédictions qui sont écrites dans ce livre s’arrêtent sur lui; que le Seigneur efface son nom de dessous le ciel.
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 Et qu’il l’extermine pour jamais de toutes les tribus d’israël, selon les malédictions, qui sont contenues dans le livre de cette loi et de l’alliance.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 Et la génération suivante et les enfants qui naîtront successivement, et les étrangers qui seront venus de loin, voyant les plaies de cette terre et les infirmités dont l’aura affligée le Seigneur,
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 En la brûlant par le soufre et par l’ardeur du sel, de sorte qu’elle ne soit plus semée, et qu’elle ne pousse plus aucune verdure, à l’exemple de la ruine de Sodome et de Gomorrhe, d’Adama et de Séboïm, que le Seigneur renversa dans sa colère et sa fureur,
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 Et toutes les nations diront: Pourquoi le Seigneur a-t-il fait ainsi à cette terre? qu’est-ce que cette immense colère de sa fureur?
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 Et on leur répondra: Parce qu’ils ont abandonné l’alliance du Seigneur, qu’il a faite avec leurs pères, quand il les a retirés de la terre d’Egypte;
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 Et qu’ils ont servi des dieux étrangers, qu’ils les ont adorés, des dieux qu’ils ne connaissaient pas et auxquels ils n’appartenaient pas;
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 C’est pour cela que la fureur du Seigneur s’est irritée contre cette terre, afin qu’il amenât sur elle toutes les malédictions qui sont écrites dans ce livre;
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 Et il les a chassés de leur terre dans sa colère, dans sa fureur et dans sa plus grande indignation, et il les a jetés dans une terre étrangère, comme il est entièrement prouvé aujourd’hui.
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 Les choses cachées sont au Seigneur notre Dieu, celles qui sont manifestes, à nous et à nos enfants à jamais, afin que nous accomplissions toutes les paroles de cette loi.
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.

< Deutéronome 29 >