< Colossiens 2 >

1 Car je veux que vous sachiez quelle sollicitude j’ai pour vous, pour ceux qui sont à Laodicée, et pour tous ceux qui n’ont pas vu ma face dans la chair;
Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso.
2 Afin que leurs cœurs soient consolés, et qu’ils soient instruits eux-mêmes dans la charité, pour parvenir à toutes les richesses d’une parfaite intelligence, et à la connaissance du mystère de Dieu le Père et du Christ Jésus,
Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu.
3 En qui tous les trésors de la sagesse et de la science sont cachés.
Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso.
4 Je dis ceci afin que nul ne vous trompe par la sublimité des discours.
Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake.
5 Car, quoique absent de corps, je suis cependant avec vous en esprit, me réjouissant en voyant l’ordre qui est parmi vous, et la solidité de votre foi dans le Christ.
Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.
6 Comme donc vous avez reçu Jésus-Christ, le Seigneur, marchez selon lui,
Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo.
7 Enracinés en lui, édifiés sur lui, vous affermissant dans la foi, telle qu’elle vous a été enseignée, et lui rendant en abondance des actions de grâces.
Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.
8 Prenez garde que personne ne vous séduise par la philosophie, par des raisonnements vains et trompeurs, selon la tradition des hommes, selon les éléments du monde, et non selon le Christ;
Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.
9 Car en lui toute la plénitude de la divinité habite corporellement;
Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu.
10 Et vous êtes remplis en lui, qui est le chef de toute principauté et de toute puissance;
Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse.
11 Et c’est en lui que vous avez été circoncis d’une circoncision non faite de main d’homme par le dépouillement de votre corps de chair, mais de la circoncision du Christ;
Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija.
12 Ayant été ensevelis avec lui dans le baptême, dans lequel vous avez été aussi ressuscités par la foi en la puissance de Dieu qui l’a ressuscité d’entre les morts.
Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.
13 Et vous, lorsque vous étiez morts dans vos péchés et dans l’incirconcision de votre chair, il vous a fait revivre avec lui, vous remettant tous vos péchés;
Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse.
14 Effaçant la cédule du décret porté contre nous, qui nous était contraire, et qu’il a abolie, en l’attachant à la croix;
Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda.
15 Et dépouillant les principautés et les puissances, il les a menées captives avec une noble fierté, triomphant d’elles hautement en lui-même.
Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.
16 Que personne donc ne vous juge sur le manger ou sur le boire, ou à cause des jours de fête, ou des néoménies, ou des sabbats;
Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata.
17 Choses qui ne sont que l’ombre des futures, tandis que le Christ en est le corps.
Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu.
18 Que personne ne vous séduise, affectant l’humilité et le culte des anges, s’ingérant dans ce qu’il n’a point vu; vainement enflé des pensées de sa chair,
Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu.
19 Et ne tenant point à la tête par laquelle tout le corps, servi et relié au moyen des jointures et des ligaments, croît de l’accroissement de Dieu.
Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.
20 Si donc vous êtes morts avec le Christ aux éléments de ce monde, pourquoi décidez-vous encore comme si vous viviez dans le monde?
Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa:
21 Ne mangez pas, ne goûtez pas, ne touchez pas,
“Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?”
22 Toutes choses qui périssent par l’usage même, et n’existent qu’en vertu des préceptes et des ordonnances des hommes,
Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe.
23 Lesquelles ont cependant une apparence de raison dans un culte exagéré et une humilité affectée, dans la mortification du corps, et un certain mépris pour le rassasiement de la chair.
Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.

< Colossiens 2 >