< Amos 5 >
1 Ecoutez cette parole, chant lugubre que j’entonne sur vous: La maison d’Israël est tombée, elle ne se relèvera plus.
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 La vierge d’Israël a été jetée par terre, et il n’y a personne qui la rétablisse.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 Parce que voici ce que dit le Seigneur Dieu: Dans la ville de laquelle sortaient mille hommes, il en restera cent; et dans celle de laquelle sortaient cent, il en restera dix, dans la maison d’Israël.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 Parce que voici ce que dit le Seigneur à la maison d’Israël: Cherchez-moi et vous vivrez.
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 Et ne cherchez point Béthel, et n’allez point à Galgala, et vous ne passerez point à Bersabée, parce que Galgala sera emmenée captive, et Béthel sera réduite à rien.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Cherchez le Seigneur, et vivez; de peur que la maison de Joseph ne s’embrase comme un feu; et le feu la dévorera, et il n’y aura personne qui éteigne Béthel.
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 C’est vous qui changez en absinthe le jugement, et qui abandonnez la justice sur la terre.
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 Cherchez qui a fait Arcturus et Orion, qui convertit les ténèbres en lumière du matin, et qui change le jour en nuit, qui appelle les eaux de la mer et la répand sur la face de la terre; le Seigneur est son nom.
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Il sourit en amenant la ruine sur le fort, et il porte le ravage sur le puissant.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Ils ont eu en haine celui qui les reprenait à la porte; celui qui parlait à bon droit, ils l’ont abominé.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 C’est pourquoi, parce que vous dépouilliez le pauvre, que vous lui enleviez un butin précieux, vous bâtirez des maisons en pierre de taille, et vous n’y habiterez pas; vous planterez des vignes délicieuses, et vous n’en boirez pas le vin.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 Parce que j’ai connu vos nombreux crimes, et vos graves péchés; ennemis du juste, vous recevez des présents, et vous déprimez les pauvres à la porte.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 C’est pour cela que l’homme prudent en ce temps-là se tiendra en silence, parce que le temps est mauvais.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Cherchez le bien et non le mal, afin que vous viviez, et le Seigneur Dieu des armées sera avec vous, comme vous avez dit.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Haïssez le mal, et aimez le bien, et établissez à la porte de la ville le jugement; peut-être que le Seigneur Dieu des armées aura pitié des restes de Joseph.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 À cause de ceci, voici ce que dit le Seigneur Dieu des armées, le dominateur: Sur toutes les places publiques, lamentations, et dans tous les lieux qui sont hors de la ville, on dira: Malheur! malheur! et on appellera le laboureur au deuil, et aux lamentations ceux qui savent se lamenter.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Et dans toutes les vignes il y aura des lamentations, parce que je passerai au milieu de toi, dit le Seigneur.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Malheur à ceux qui désirent le jour du Seigneur! pourquoi le désirer pour vous? Ce jour du Seigneur sera pour vous ténèbres et non lumière.
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Comme si un homme fuit à la face du lion, et qu’il rencontre l’ours; et qu’il entre dans la maison, et appuie de sa main sur la muraille, et que le serpent le morde.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Est-ce que le jour du Seigneur ne sera pas ténèbres et non lumière; obscurité et non splendeur?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Je hais, et j’ai rejeté vos fêtes; je ne respirerai pas l’odeur de vos assemblées.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Que si vous m’offrez des holocaustes et des présents, je ne les recevrai pas; et les grasses victimes qui accompagneront vos vœux, je ne les regarderai pas.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Eloigne de moi le tumulte de tes cantiques; et les airs de ta lyre, je ne les écouterai pas.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Et le jugement se découvrira comme l’eau, et la justice comme un torrent violent.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Est-ce que vous m’avez offert des hosties et des sacrifices dans le désert pendant quarante ans, maison d’Israël?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Et vous avez porté le tabernacle de votre Moloch, et l’image de vos idoles, l’étoile de votre dieu, que vous vous êtes fait.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Aussi je vous ferai émigrer au-delà de Damas, dit le Seigneur; car le Dieu des armées est son nom.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.