< Actes 20 >
1 Après que le tumulte eut cessé, Paul ayant appelé les disciples, et leur ayant fait une exhortation, leur dit adieu, et partit pour aller en Macédoine.
Litatha phokoso, Paulo anayitanitsa ophunzira ndipo atawalimbikitsa anawatsanzika ndipo ananyamuka kupita ku Makedoniya.
2 Lorsqu’il eut parcouru ces contrées et fait beaucoup d’exhortations, il vint en Grèce;
Iye anayendera madera a kumeneko, nalimbitsa mtima anthu, ndipo pomaliza pake anapita ku Grisi.
3 Où, après avoir séjourné trois mois, il résolut de s’en retourner par la Macédoine, les Juifs lui ayant dressé une embuscade sur le chemin qu’il devait prendre pour se rendre par mer en Syrie.
Kumeneko anakhala miyezi itatu. Popeza kuti Ayuda anakonza zomuchita chiwembu pamene amati azinyamuka kupita ku Siriya pa sitima ya pamadzi, iye anaganiza zobwereranso kudzera ku Makedoniya.
4 Sopater, fils de Pyrrhus, de Bérée, l’accompagna, de même qu’Aristarque et Second, Thessaloniciens; Gaïus, de Derbe, et Timothée; Tychique et Trophime, tous deux d’Asie.
Iye anapita pamodzi ndi Sopatro mwana wa Puro wa ku Bereya, Aristariko ndi Sekundo a ku Tesalonika, Gayo wa ku Derbe ndi Timoteyo, ndipo a ku Asiya anali Tukiko ndi Trofimo.
5 Ceux-ci étant allés devant, nous attendirent à Troas;
Anthu amenewa anatsogola ndipo anakatidikira ku Trowa.
6 Pour nous, après les jours des azymes, nous nous embarquâmes à Philippes, et en cinq jours nous les rejoignîmes à Troas, où nous demeurâmes sept jours.
Koma ife tinayenda pa sitima ya pamadzi kuchokera ku Filipi chitatha Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Patapita masiku asanu tinakumana nawo enawo ku Trowa, ndipo tinakhala kumeneko masiku asanu ndi awiri.
7 Le premier jour de la semaine, les disciples étant assemblés pour rompre le pain. Paul, qui devait partir le lendemain, les entretenait, et il prolongea son discours jusqu’au milieu de la nuit.
Pa tsiku loyamba la Sabata, tinasonkhana kuti tidye mgonero. Paulo analalikira kwa anthu chifukwa anaganiza zoti achoke tsiku linalo, ndipo analalika mpaka pakati pa usiku.
8 Or il y avait beaucoup de lampes dans le cénacle où nous étions rassemblés.
Munali nyale zambiri mʼchipinda chammwamba mʼmene tinasonkhanamo.
9 Et un jeune homme, du nom d’Eutyque, qui était assis sur la fenêtre, était enseveli dans un profond sommeil, car Paul par lait depuis longtemps, et en traîné par le sommeil, tomba du troisième étage en bas, et fut relevé mort.
Pa chipinda chachitatu chammwamba cha nyumbayo, pa zenera, panakhala mnyamata wina dzina lake Utiko, amene ankasinza pomwe Paulo amayankhulabe. Atagona tulo, iye anagwa pansi kuchokera pa chipinda chammwamba ndipo anamutola atafa.
10 Paul étant descendu où il était, s’étendit sur lui, et, l’ayant embrassé, dit: Ne vous troublez point, car son âme est en lui.
Paulo anatsika, nadziponya pa mnyamatayo, namukumbatira. Paulo anati, “Musadandaule, ali moyo!”
11 Puis étant remonté et ayant rompu le pain et mangé, il leur parla encore beaucoup jusqu’au jour, et il partit ainsi.
Kenaka Paulo anakweranso, mʼchipinda muja nanyema buledi nadya. Atayankhula mpaka kucha, anachoka.
12 Or on ramena le jeune homme vivant, et ils en furent grandement consolés.
Anthu anatenga mnyamatayo kupita kwawo ali moyo ndipo anatonthozedwa mtima kwambiri.
13 Pour nous, montant sur le vaisseau, nous naviguâmes vers Asson, où nous devions reprendre Paul; car il l’avait ainsi disposé, devant lui-même aller par terre.
Ife tinatsogola kukakwera sitima ya pa madzi kupita ku Aso, kumene tinayembekeza kukatenga Paulo. Iye anakonza motero chifukwa amayenda wapansi.
14 Lors donc qu’il nous eut rejoints à Asson, nous le reprîmes, et nous vînmes à Mitylène.
Pamene anakumana nafe ku Aso tinamutenga ndipo tinapita ku Mitilene.
15 Et de là, naviguant, nous arrivâmes le jour suivant devant Chio; le lendemain nous abordâmes à Samos, et le jour d’après nous vînmes à Milet;
Mmawa mwake tinachoka kumeneko pa sitima ya pamadzi ndipo tinafika pafupi ndi Kiyo. Tsiku linalo tinawolokera ku Samo, ndipo tsiku linanso tinafika ku Mileto.
16 Car Paul s’était proposé de passer Ephèse sans y prendre terre, de peur d’éprouver quelque retard en Asie. Car il se hâtait, afin d’être, s’il lui eût été possible, le jour de la Pentecôte à Jérusalem.
Paulo anali atatsimikiza kuti alambalale Efeso kuopa kutaya nthawi ku Asiya, pakuti ankafulumira kuti akafike ku Yerusalemu kuti ngati nʼkotheka kuti tsiku la Pentekosite akakhale ali ku Yerusalemu.
17 Or, de Milet envoyant à Ephèse, il appela les anciens de l’Eglise.
Paulo ali ku Mileto, anatumiza mawu ku Efeso kuyitana akulu ampingo.
18 Et lorsqu’ils furent venus près de lui, et qu’ils étaient assemblés, il leur dit: Vous savez comment, dès le premier jour où je suis entré en Asie, j’ai été en tout temps avec vous,
Iwo atafika, Paulo anati, “Inu mukudziwa mmene ndinakhalira nanu nthawi yonse imene ndinali nanu kuyambira tsiku loyamba limene ndinafika ku Asiya.
19 Servant le Seigneur en toute humilité, au milieu des larmes et des épreuves qui me sont survenues par les trames des Juifs;
Ndinatumikira Ambuye modzichepetsa kwambiri ndiponso ndi misozi, ngakhale ndinayesedwa kwambiri ndi ziwembu za Ayuda.
20 Comment je ne vous ai soustrait aucune des choses utiles, et que rien ne m’a empêché de vous les annoncer, et de vous les enseigner publiquement et dans les maisons,
Inu mukudziwa kuti, sindinakubisireni kanthu kalikonse kopindulitsa koma ndinakuphunzitsani poyera komanso nyumba ndi nyumba.
21 Prêchant aux Juifs et aux gentils la pénitence envers Dieu, et la foi en Notre Seigneur Jésus-Christ.
Ine ndinawuza Ayuda komanso Agriki kuti ayenera kutembenukira kwa Mulungu polapa ndikuti akhulupirire Ambuye athu Yesu.
22 Et maintenant voilà que, lié par l’Esprit, je m’en vais à Jérusalem, ignorant ce qui doit m’y arriver:
“Ndipo tsopano, mokakamizidwa ndi Mzimu, ndikupita ku Yerusalemu, sindikudziwa zimene zikandichitikire kumeneko.”
23 Si ce n’est que, dans toutes les villes, l’Esprit-Saint m’atteste que des chaînes et des tribulations m’attendent à Jérusalem.
Chimene ndikudziwa ndi chakuti Mzimu Woyera wandichenjeza mu mzinda uliwonse kuti ndende ndi mavuto zikundidikira.
24 Mais je ne crains rien de ces choses, et je ne regarde pas ma vie comme plus précieuse que moi, pourvu que j’accomplisse ma course et le ministère que j’ai reçu du Seigneur Jésus, de rendre témoignage à l’Evangile de la grâce de Dieu.
Koma sindilabadira konse za moyo wanga ngati kuti ndi wa mtengo wapatali kwa ine, malingana ndikatsirize ntchito yanga ndi utumiki umene Ambuye Yesu anandipatsa, ntchito yochitira umboni Uthenga Wabwino wachisomo cha Mulungu.
25 Et maintenant voilà que je sais que vous ne verrez plus mon visage, vous tous au milieu desquels j’ai passé, annonçant le royaume de Dieu.
“Tsopano ndikudziwa kuti inu nonse amene ndinakuyenderani ndi kumakulalikirani ufumu wa Mulungu simudzaonanso nkhope yanga.
26 C’est pourquoi je vous prends à témoins aujourd’hui que je suis pur du sang de vous tous.
Chifukwa chake, ine ndikukuwuzani lero kuti ndilibe mlandu ndi munthu aliyense.
27 Car je ne me suis point refusé à vous annoncer tous les desseins de Dieu.
Pakuti sindinakubisireni pokulalikirani chifuniro chonse cha Mulungu.
28 Soyez donc attentifs et à vous et à tout le troupeau sur lequel Dieu vous a établis évêques, pour gouverner l’Eglise de Dieu, qu’il a acquise par son sang.
Mudziyangʼanire nokha ndiponso muyangʼanire gulu lankhosa limene Mzimu Woyera anakuyikani kuti mukhale oyangʼanira ake. Khalani abusa a mpingo wa Mulungu umene Iye anawugula ndi magazi ake.
29 Car moi je sais qu’après mon départ s’introduiront parmi vous des loups ravissants, qui n’épargneront point le troupeau;
Ndikudziwa kuti ndikachoka ine, padzafika mimbulu yolusa pakati panu imene sidzalekerera gulu lankhosalo.
30 Et que, d’au milieu de vous-mêmes, s’élèveront des hommes qui enseigneront des choses perverses, afin d’attirer les disciples après eux.
Ngakhale pakati pa inu nokha padzapezeka anthu oyankhula zonama ndi cholinga chofuna kukhala ndi ophunzira kuti awatsate.
31 C’est pourquoi, veillez, retenant en votre mémoire que pendant trois ans je n’ai cessé d’avertir avec larmes chacun de vous.
Tsono inu, samalani! Kumbukirani kuti kwa zaka zitatu, usana ndi usiku ndiponso ndi misozi sindinaleke kuchenjeza aliyense wa inu.
32 Et maintenant, je vous recommande à Dieu et à la parole de sa grâce, à celui qui est puissant pour édifier, et pour donner un héritage parmi tous les sanctifiés.
“Tsopano ine ndikukuperekani kwa Mulungu ndiponso kwa mawu a chisomo chake, amene ali ndi mphamvu zokulitsa inu ndi kukupatsani chuma pakati pa onse amene anayeretsedwa.
33 Je n’ai convoité ni l’or, ni l’argent, ni le vêtement de personne, comme
Ine sindinasirire siliva kapena golide kapena zovala za munthu aliyense.
34 Vous le savez vous-mêmes; parce que, à l’égard des choses dont moi et ceux qui sont avec moi avions besoin, ces mains y ont pourvu.
Inu nomwe mukudziwa kuti manja angawa ananditumikira kuti tipeze zimene ine ndi anzanga tinkazifuna.
35 Je vous ai montré en tout que c’est en travaillant ainsi qu’il faut soutenir les faibles, et se souvenir de la parole du Seigneur Jésus; car c’est lui-même qui a dit: Il est plus heureux de donner que de recevoir.
Pa zonse zimene ndinachita, ndinakuonetsani kuti pogwira ntchito molimbika motere tiyenera kuthandiza ofowoka, pokumbukira mawu a Ambuye Yesu akuti, ‘Kupereka kumadalitsa kuposa kulandira.’”
36 Lorsqu’il eut dit ces choses, il se mit à genoux, et pria avec eux tous.
Atanena zimenezi, anagwada pansi pamodzi ndi ena onse, napemphera.
37 Et il y eut un grand pleur parmi eux tous, et se jetant au cou de Paul, ils le baisaient,
Onse analira pamene amamukumbatira ndi kupsompsona.
38 Affligés surtout de la parole qu’il avait dite, qu’ils ne devaient plus revoir son visage. Et ils le conduisirent jusqu’au vaisseau.
Chimene chinamvetsa chisoni kwambiri ndi mawu ake akuti sadzaonanso nkhope yake. Kenaka iwo anamuperekeza ku sitima yapamadzi.