< Actes 15 >

1 Et quelques-uns, qui étaient descendus de Judée, enseignaient aux frères: Si vous n’êtes circoncis suivant le rit de Moïse, vous ne pouvez être sauvés.
Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
2 Paul et Barnabé s’étant donc fortement élevés contre eux, il fut résolu que Paul et Barnabé, et quelques-uns d’entre les autres, iraient à Jérusalem vers les apôtres et les prêtres pour cette question.
Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
3 Ceux-ci donc, accompagnés par l’Eglise, traversèrent la Phénicie et la Samarie, racontant la conversion des gentils; et ils causaient ainsi à tous les frères une grande joie.
Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
4 Arrivés à Jérusalem, ils furent reçus par l’Eglise, par les apôtres et les anciens, auxquels ils racontèrent combien Dieu avait fait de grandes choses avec eux.
Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
5 Mais que quelques-uns de la secte des pharisiens, qui avaient embrassé la foi, s’étaient levés, disant qu’il fallait qu’ils fussent circoncis, et qu’on leur ordonnât de garder la loi de Moïse.
Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
6 Les apôtres et les prêtres s’assemblèrent donc pour examiner cette question.
Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
7 Mais après une grande discussion, Pierre, se levant, leur dit: Hommes, mes frères, vous savez qu’en des jours déjà anciens. Dieu m’a choisi parmi vous afin que les gentils entendissent par ma bouche la parole de l’Evangile, et qu’ils crussent.
Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
8 Et Dieu, qui connaît les cœurs, leur a rendu témoignage, leur donnant l’Esprit-Saint, comme à nous;
Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
9 Et il n’a fait entre nous et eux aucune différence, purifiant leurs cœurs par la foi.
Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
10 Maintenant donc, pourquoi tentez-vous Dieu, imposant aux disciples un joug que ni nos pères ni nous n’avons pu porter?
Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
11 Mais c’est par la grâce de Jésus-Christ que nous croyons être sauvés, comme eux aussi.
Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
12 Alors toute l’assemblée se tut; et ils écoutaient Barnabé et Paul racontant combien de miracles et de prodiges Dieu avait faits par eux parmi les gentils.
Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
13 Et après qu’ils se furent tus, Jacques répondit, disant: Hommes, mes frères, écoutez-moi:
Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
14 Simon a raconté comment Dieu, dès le principe, a visité les gentils, afin de choisir parmi eux un peuple pour son nom.
Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
15 Et les paroles des prophètes s’accordent avec lui, ainsi qu’il est écrit:
Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
16 Après cela je reviendrai, et je rebâtirai le tabernacle de David, qui est tombé; je réparerai ses ruines et je le relèverai;
“‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
17 Afin que le reste des hommes cherchent le Seigneur, et aussi toutes les nations sur lesquelles mon nom a été invoqué, dit le Seigneur, qui fait ces choses.
kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
18 De toute éternité, Dieu connaît son œuvre. (aiōn g165)
zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn g165)
19 C’est pourquoi moi, je juge qu’on ne doit pas inquiéter ceux d’entre les gentils qui se convertissent à Dieu,
“Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
20 Mais leur écrire qu’ils s’abstiennent des souillures des idoles, de la fornication, des animaux étouffés, et du sang.
Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
21 Quant à Moïse, depuis les temps anciens, il a, en chaque ville, des hommes qui le prêchent dans les synagogues, où on le lit tous les jours de sabbat.
Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
22 Alors il plut aux apôtres et aux anciens, avec toute l’Eglise, de choisir quelques-uns d’entre eux, et de les envoyer, avec Paul et Barnabé, à Antioche: Jude, qui est surnommé Barsabas, et Silas, qui étaient des principaux entre les frères,
Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
23 Ecrivant par eux: Les APOTRES et les prêtres, frères, aux frères d’entre les gentils, qui sont à Antioche, et en Syrie et en Cilicie, salut.
kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
24 Comme nous avons appris que quelques-uns sortant d’au milieu de nous vous ont troublés par leurs discours, en bouleversant vos âmes, quoique nous ne leur eussions donné aucun ordre,
Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
25 Il a plu à nous tous de choisir des personnes et de les envoyer vers vous avec nos très chers Barnabé et Paul,
Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
26 Hommes qui ont exposé leur vie pour le nom de notre Seigneur Jésus-Christ.
anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
27 Nous avons donc envoyé Jude et Silas, qui vous rapporteront les mêmes choses de vive voix.
Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
28 Car il a semblé bon à l’Esprit-Saint et à nous, de ne vous imposer aucun autre fardeau que ces choses-ci, qui sont nécessaires:
Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
29 Que vous vous absteniez de ce qui a été sacrifié aux idoles, du sang, des animaux étouffés, et de la fornication; en vous en abstenant, vous agirez bien. Adieu.
Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
30 Ces envoyés donc se rendirent à Antioche, et, les fidèles rassemblés, ils remirent la lettre.
Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
31 Quand ils l’eurent lue, ils éprouvèrent beaucoup de joie et de consolation.
Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
32 Et comme Jude et Silas étaient eux-mêmes prophètes, ils consolèrent les frères et les fortifièrent par de nombreux discours.
Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
33 Et, après avoir passé là quelque temps, ils furent renvoyés en paix par les frères à ceux qui les avaient envoyés.
Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
34 Cependant il parut bon à Silas de rester là, et Jude seul retourna à Jérusalem.
Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
35 Or Paul et Barnabé demeurèrent aussi à Antioche, enseignant et annonçant avec plusieurs autres la parole de Dieu.
Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
36 Mais quelques jours après Paul dit à Barnabé: Retournons visiter nos frères dans toutes les villes où nous avons prêché la parole du Seigneur, pour voir comment ils sont.
Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
37 Or Barnabé voulait prendre avec lui Jean, qui est surnommé Marc.
Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
38 Mais Paul lui représentait que celui qui les avait quittés en Pamphylie et n’était point allé avec eux pour cette œuvre, ne devait pas être repris.
Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
39 De là il y eut division entre eux, de sorte qu’ils se séparèrent l’un de l’autre. Barnabé ayant donc pris Marc, s’embarqua pour Chypre.
Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
40 Et Paul ayant choisi Silas, partit, commis à la grâce de Dieu par les frères.
Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
41 Or il parcourait la Syrie et la Cilicie, confirmant les Eglises, et leur ordonnant de garder les préceptes des apôtres et des prêtres.
Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.

< Actes 15 >