< 2 Timothée 1 >

1 Paul, apôtre de Jésus-Christ par la volonté de Dieu, selon la promesse de vie, qui est dans le Christ Jésus;
Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.
2 À Timothée, son fils bien-aimé, grâce, miséricorde, paix par Dieu le Père et par le Christ Jésus Notre Seigneur.
Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
3 Je rends grâces à Dieu, qu’à l’exemple de mes ancêtres, je sers avec une conscience pure, de ce que, nuit et jour, je fais
Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga.
4 Désirant, au souvenir de tes larmes, te voir, pour être rempli de joie;
Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe.
5 Rappelant en ma mémoire cette foi non feinte, qui est en toi, et qui a été premièrement dans ton aïeule Loïde, et dans ta mère Eunice, et qui, j’en ai la certitude, est aussi en toi.
Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.
6 C’est pourquoi je t’engage à ranimer la grâce de Dieu, qui est en toi par l’imposition de mes mains.
Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja.
7 Car Dieu ne nous a pas donné un esprit de crainte, mais de force, d’amour et de modération.
Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.
8 Ne rougis donc point du témoignage de Noire Seigneur, ni de moi son captif; mais prends part aux travaux de l’Evangile, selon la puissance de Dieu,
Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu.
9 Qui nous a délivrés, et nous a appelés par sa vocation sainte, non selon nos œuvres, mais selon son décret et la grâce qui nous a été donnée dans le Christ Jésus avant le commencement des siècles, (aiōnios g166)
Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
10 Et qui a été manifestée maintenant par l’apparition de notre Sauveur Jésus-Christ qui a détruit la mort, et fait luire la vie et l’incorruptibilité par l’Evangile.
Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe.
11 C’est pourquoi j’ai été établi moi-même prédicateur, apôtre et maître des nations.
Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu.
12 Et c’est pour cela aussi que j’endure ces souffrances; mais je n’en rougis point. Car je sais à qui je me suis confié, et je suis sûr qu’il est puissant pour garder mon dépôt jusqu’à ce jour.
Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.
13 Prends pour modèle les saines paroles que tu as entendues de moi dans la foi et l’amour qui est en Jésus-Christ.
Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu.
14 Conserve le précieux dépôt, par l’Esprit-Saint qui habite eu nous.
Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.
15 Tu sais que tous ceux qui sont en Asie m’ont abandonné; de ce nombre sont Phigelle et Hermogène.
Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.
16 Que le Seigneur répande sa miséricorde sur la maison d’Onésiphore, parce qu’il m’a souvent soulagé, et qui] n’a point rougi de mes chaînes;
Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo.
17 Mais que, lorsqu’il est venu à Rome, il m’a cherché avec beaucoup de soin, et m’a trouvé.
Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza.
18 Que le Seigneur lui donne de trouver miséricorde devant lui en ce jour. Car combien de services ne m’a-t-il pas rendus à Ephèse? Tu le sais parfaitement.
Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

< 2 Timothée 1 >