< 2 Samuel 24 >
1 Et la fureur du Seigneur recommença à s’irriter contre Israël, et il excita parmi eux, David, disant: Va, dénombre Israël et Juda.
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 Le roi dit donc à Joab, prince de son armée: Parcours toutes les tribus d’Israël, depuis Dan jusqu’à Bersabée, et dénombrez tout le peuple, afin que j’en sache le nombre.
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 Et Joab répondit au roi: Que le Seigneur votre Dieu multiplie votre peuple encore autant qu’il est maintenant, et que de nouveau, il le centuple en la présence de mon seigneur le roi: mais que veut faire mon seigneur le roi par une chose de cette nature?
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 Mais la parole du roi l’emporta sur les paroles de Joab et des princes de l’armée; et Joab sortit, et les princes des soldats, de la présence du roi, pour dénombrer le peuple d’Israël.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 Et lorsqu’ils eurent passé le Jourdain, ils vinrent à Aroër, à la droite de la ville qui est dans la vallée de Gad,
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 Puis, par Jazer ils passèrent en Galaad, et dans la terre inférieure d’Hodsi; et ils vinrent dans les forêts de Dan. Tournant ensuite près de Sidon,
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 Ils passèrent près des murailles de Tyr, et de toute la terre de l’Hévéen et du Chananéen, et ils vinrent au midi de Juda, à Bersabée.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 Et, toute la terre examinée, ils se trouvèrent, après neuf mois et vingt jours, à Jérusalem.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 Joab donc donna le dénombrement du peuple au roi, et il se trouva d’Israël huit cent mille hommes forts, qui pouvaient tirer l’épée; et de Juda, cinq cent mille combattants.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Mais le cœur de David fut pris de remords, après que le peuple eut été dénombré, et David dit au Seigneur: J’ai beaucoup péché en cette action; mais je vous prie. Seigneur, écartez l’iniquité de votre serviteur, parce que j’ai agi tout à fait en insensé.
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 C’est pourquoi David se leva le matin, et la parole du Seigneur fut adressée à Gad, le prophète et le voyant de David, disant:
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 Va, et parle à David: Voici ce que dit le Seigneur: L’option de trois choses t’est donnée; choisis celle que tu voudras, afin que je te la fasse.
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 Lors donc que Gad fut venu vers David, il lui annonça, disant: Ou une famine vous viendra sur la terre durant sept ans; ou vous fuirez vos ennemis durant trois mois, et eux vous poursuivront; ou bien une peste sera pendant trois jours dans votre terre. Maintenant donc délibérez, et voyez quelle parole je dois porter en réponse à celui qui m’a envoyé.
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 Et David répondit à Gad: Je suis dans une très grande angoisse, mais il vaut mieux que je tombe dans les mains du Seigneur (car ses miséricordes sont sans nombre), que dans les mains des hommes.
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 Et le Seigneur envoya une peste en Israël, depuis le matin jusqu’au temps marqué; et il mourut d’entre le peuple, depuis Dan jusqu’à Bersabée, soixante dix mille hommes.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 Et, lorsque l’ange du Seigneur eut étendu sa main sur Jérusalem pour la détruire, le Seigneur eut pitié de son affliction, et dit à l’ange qui frappait le peuple: Il suffit, maintenant retiens ta main. Or, l’ange du Seigneur était alors près de l’aire d’Aréuna, le Jébuséen.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 Et David dit au Seigneur, quand il vit l’ange tuant le peuple: C’est moi qui ai péché et qui ai agi iniquement: ceux-ci, qui sont les brebis, qu’ont-ils fait? Que votre main, je vous conjure, se tourne contre moi et contre la maison de mon père.
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 Or, Gad vint vers David en ce jour-là, et lui dit: Montez, et élevez au Seigneur un autel dans l’aire d’Aréuna, le Jébuséen.
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 Et David monta selon la parole de Gad, que lui avait ordonnée le Seigneur.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 Et regardant, Aréuna aperçut le roi et ses serviteurs venir vers lui;
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 Et il sortit et se prosterna devant le roi, le visage incliné vers la terre, et il dit: Quelle raison y a-t-il pour que mon seigneur le roi vienne vers son serviteur? David lui répondit: C’est pour acheter de toi l’aire et bâtir un autel au Seigneur, afin que cesse la tuerie qui ravage le peuple.
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 Et Aréuna dit à David: Que mon seigneur le roi prenne, et qu’il offre comme il lui plaît: vous avez les bœufs pour l’holocauste, le char, et les jougs de bœufs, pour servir de bois.
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Le roi Aréuna donna toutes ces choses au roi; et Aréuna dit au roi: Que le Seigneur votre Dieu reçoive votre vœu.
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 Le roi, lui répondant, dit: Pas du tout comme vous voulez; mais j’achèterai de vous, selon le prix, et je n’offrirai point au Seigneur mon Dieu des holocaustes qui ne me coûtent rien. David donc acheta l’aire et les bœufs cinquante sicles d’argent.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 Et David bâtit là un autel au Seigneur, et il offrit des holocaustes et des sacrifices pacifiques. Et le Seigneur devint propice à la terre, et la plaie fut écartée d’Israël.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.