< 2 Samuel 20 >
1 Il arriva aussi que là était un homme de Bélial, du nom de Séba, fils de Bochri, homme de Jémini, et il sonna de la trompette, et dit: Nous n’avons point de part avec David, ni d’héritage avec le fils d’Isaï; retourne en tes tabernacles, ô Israël.
Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
2 Et tout Israël se sépara de David, et suivit Séba, fils de Bochri; mais les hommes de Juda restèrent près de leur roi, depuis le Jourdain jusqu’à Jérusalem.
Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.
3 Et lorsque le roi fut venu en sa maison à Jérusalem, il prit les dix femmes qu’il avait laissées pour garder la maison, les donna en garde, leur fournissant les aliments; et il ne s’approcha plus d’elles: mais elles étaient enfermées jusqu’au jour de leur mort, vivant en veuves.
Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.
4 Or, le roi dit à Amasa: Appelle près de moi tous les hommes de Juda pour le troisième jour, et toi, sois présent.
Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”
5 Amasa donc s’en alla pour appeler Juda, et il tarda au-delà de l’ordre que lui avait donné le roi.
Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.
6 Or David dit à Abisaï: Maintenant Séba, fils de Bochri, nous affligera plus qu’Absalom: prends donc les serviteurs de ton seigneur, et poursuis-le, de peur qu’il ne trouve des villes fortifiées, et qu’il ne nous échappe.
Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.”
7 Les hommes de Joab sortirent donc avec lui, les Céréthiens aussi et les Phélétiens; et tous les hommes vigoureux sortirent de Jérusalem pour poursuivre Séba, fils de Bochri.
Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
8 Et lorsqu’ils furent près de la grande pierre qui est à Gabaon, Amasa, venant, les rencontra. Or, Joab était vêtu d’une tunique étroite, selon la mesure de son habit, et par-dessus ceint d’un glaive pendant à ses côtés dans son fourreau, et fait de manière qu’il pouvait par un léger mouvement sortir et frapper.
Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.
9 C’est pourquoi Joab dit à Amasa: Salut, mon frère. Et de sa main droite, il prit le menton d’Amasa, comme pour le baiser.
Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona.
10 Or Amasa ne prit point garde au glaive qu’avait Joab, qui le frappa dans le côté, et répandit ses entrailles sur la terre; et il ne le frappa point d’un second coup, et Amasa mourut. Ensuite Joab et Abisaï son frère poursuivirent Séba, fils de Bochri.
Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
11 Cependant quelques hommes des compagnons de Joab, s’étant arrêtés près du cadavre d’Amasa, dirent: Voilà celui qui a voulu être de la suite de David à la place de Joab.
Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!”
12 Et Amasa, couvert de sang, gisait au milieu de la voie. Mais un certain homme vit que tout le peuple s’arrêtait pour le voir; il poussa Amasa de la voie dans le champ, et le couvrit d’un vêtement, afin que les passants ne s’arrêtassent pas à cause de lui.
Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu.
13 Amasa donc ôté de la voie, tout homme passait, suivant Joab, pour poursuivre Séba, fils de Bochri.
Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
14 Mais celui-ci avait passé à travers toutes les tribus d’Israël, à Abéla et à Bethmaacha; et tous les hommes choisis s’étaient assemblés auprès de lui.
Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye.
15 C’est pourquoi Joab et les siens vinrent, et l’assiégèrent à Abéla et à Bethmaacha; et ils environnèrent la ville de fortifications, et la ville fut investie: or, toute la multitude qui était avec Joab s’efforçait de détruire les murs.
Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse,
16 Et une femme sage de la ville s’écria: Ecoutez, écoutez; dites à Joab: Approche-toi d’ici, et je te parlerai.
mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.”
17 Lorsque Joab se fut approché d’elle, elle lui dit: C’est toi qui es Joab? Et celui-ci répondit: Moi. Elle lui parla ainsi: Ecoute les paroles de ta servante. Joab répondit: J’écoute.
Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?” Iye anayankha kuti, “Ndine.” Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.” Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”
18 Et elle de nouveau: Ce mot, dit-elle, se disait dans un ancien proverbe: Ceux qui interrogent, qu’ils interrogent à Abéla; et c’est ainsi qu’ils arrivaient au but.
Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo.
19 N’est-ce pas moi qui réponds la vérité en Israël, et toi, tu demandes à bouleverser une cité, et à détruire une mère en Israël? Pourquoi renverses-tu l’héritage du Seigneur?
Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”
20 Et répondant, Joab dit: Loin de moi, loin de moi cela! je ne renverse, ni ne démolis.
Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.
21 La chose n’est pas ainsi; mais un homme de la montagne d’Ephraïm, Séba, fils de Bochri par son surnom, a levé sa main contre le roi David: livrez-le seul, et nous nous retirerons de la ville. Et la femme dit à Joab: Voilà que sa tête te sera envoyée par-dessus le mur.
Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.” Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”
22 Elle s’avança donc vers tout le peuple, et parla sagement; et ayant coupé la tête de Séba, fils de Bochri, ils la jetèrent à Joab. Et celui-ci sonna de la trompette, et ils se retirèrent de la ville, chacun en ses tabernacles; mais Joab retourna à Jérusalem près du roi.
Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.
23 Joab donc fut chef de toute l’armée d’Israël, mais Banaïas, fils de Joïada, des Céréthiens et des Phéléthiens,
Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti.
24 Et Aduram, des tributs; et Josaphat, fils d’Ahilud, tenait les registres.
Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika,
25 Siva était scribe, et Sadoc et Abiathar, prêtres.
Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe
26 Mais Ira, le Jaïrite, était prêtre de David.
ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.