< 2 Samuel 16 >
1 Or, lorsque David eut dépassé un peu le haut de la montagne, parut à sa rencontre Siba, serviteur de Miphiboseth, avec deux ânes, qui étaient chargés de deux cents pains, et de cent grappes de raisins secs, et de cent panerées de figues sèches, et d’une outre de vin.
Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
2 Et le roi dit à Siba: Que veut dire cela? Et Siba répondit: Les ânes sont pour les serviteurs du roi, afin qu’ils y montent; les pains et les figues pour nourrir vos serviteurs; mais le vin, pour boire, si quelqu’un tombe en défaillance dans le désert.
Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
3 Et le roi reprit: Où est le fils de ton seigneur? Et Siba répondit au roi: Il est demeuré à Jérusalem, disant: Aujourd’hui la maison d’Israël me rendra le royaume de mon père.
Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
4 Le roi dit encore à Siba: Tout ce qui était à Miphiboseth est à toi. Et Siba répondit: Je prie, que je trouve grâce devant vous, mon seigneur le roi.
Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
5 Le roi David vint donc jusqu’à Bahurim; et voilà qu’en sortait un homme de la parenté de la maison de Saül, du nom de Séméi, fils de Géra; et sortant, il s’avançait maudissant,
Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
6 Et il jetait des pierres contre David et contre tous les serviteurs du roi David: or, tout le peuple et tous les combattants marchaient à droite et à gauche à côté du roi.
Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
7 Et Séméi parlait ainsi lorsqu’il maudissait le roi: Sors, sors, homme de sang et homme de Bélial.
Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
8 Le Seigneur t’a rendu tout le sang de la maison de Saül, parce que tu t’es emparé du royaume en sa place; et le Seigneur a mis le royaume en la main d’Absalom ton fils; et voilà que t’accablent tes propres maux, parce que tu es un homme de sang.
Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
9 Alors Abisaï, fils de Sarvia, dit au roi: Pourquoi ce chien mort maudit-il mon seigneurie roi? J’irai, et lui couperai la tête.
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
10 Et le roi répondit: Qu’importe à moi et à vous, fils de Sarvia? Laissez-le maudire; car le Seigneur lui a ordonné qu’il maudisse David. Et quel est celui qui osera dire: Pourquoi a-t-il fait ainsi?
Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
11 Et le roi dit à Abisaï et à tous ses serviteurs: Voilà que mon fils, qui est sorti de mes entrailles, cherche mon âme; combien plus maintenant un fils de Jémini! Laissez-le, qu’il maudisse selon l’ordre du Seigneur;
Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
12 Peut-être que le Seigneur regardera mon affliction, et que le Seigneur me rendra quelque bien pour cette malédiction d’aujourd’hui.
Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
13 C’est pourquoi David allait par son chemin et ses gens avec lui; mais Séméi marchait du même côté, sur la crête de la montagne, maudissant, lançant des pierres contre lui, et répandant de la poussière en l’air.
Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
14 Et ainsi le roi vint, et tout le peuple avec lui, accablé de lassitude, et ils reprirent là des forces.
Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
15 Cependant Absalom et tout son peuple entrèrent à Jérusalem, et Achitophel aussi avec lui.
Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
16 Or, lorsque Chusaï, l’Arachite, ami de David, fut venu vers Absalom, il lui dit: Je vous salue, ô roi; je vous salue, ô roi.
Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
17 Et Absalom: Est-ce là, lui dit-il, ta reconnaissance envers ton ami? pourquoi n’es-tu pas allé avec ton ami?
Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
18 Et Chusaï répondit à Absalom: Point du tout, parce que je serai à celui que le Seigneur a élu, ainsi que tout ce peuple, et tous ceux d’Israël, et c’est avec lui que je demeurerai.
Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
19 Mais pour ajouter encore ceci: Qui vais-je servir? N’est-ce pas le fils du roi? Comme j’ai obéi à votre père, ainsi je vous obéirai.
Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
20 Or Absalom dit à Achitophel: Délibérez sur ce que nous devons faire.
Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
21 Et Achitophel dit à Absalom: Approchez-vous des femmes de votre père, qu’il a laissées pour garder la maison, afin que, lorsque tout Israël aura ouï que vous avez déshonoré votre père, leurs mains se fortifient avec vous.
Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
22 Ils dressèrent donc une tente pour Absalom sur la terrasse, et il s’approcha des femmes de son père devant tout Israël.
Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
23 Et les conseils qu’Achitophel donnait en ces jours-là, étaient comme si quelqu’un consultait Dieu. Tel était tout conseil d’Achitophel, et lorsqu’il était avec David, et lorsqu’il était avec Absalom.
Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.