< 2 Samuel 10 >
1 Or, il arriva après cela que le roi des enfants d’Ammon mourut, et Hanon, son fils, régna en sa place.
Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Et David dit: Je ferai miséricorde à Hanon, fils de Naas, comme son père m’a fait miséricorde. David envoya donc, le consolant par ses serviteurs de la mort de son père. Mais lorsque les serviteurs de David furent venus dans la terre des enfants d’Ammon,
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
3 Les princes des enfants d’Ammon dirent à Hanon leur seigneur: Pensez-vous que ce soit pour l’honneur de votre père, que David vous ait envoyé des consolateurs, et que ce ne soit pas pour s’enquérir de la ville, l’explorer et la détruire, que David a envoyé ses serviteurs vers vous?
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 C’est pourquoi Hanon prit les serviteurs de David, rasa la moitié de leur barbe, coupa la moitié de leurs vêtements jusqu’au haut des cuisses, et les renvoya.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
5 Lorsque cela eut été annoncé à David, il envoya au-devant d’eux; car ces hommes étaient très honteusement confus, et David leur manda: Demeurez à Jéricho jusqu’à ce que votre barbe croisse, et alors revenez.
Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Mais les enfants d’Ammon, voyant qu’ils avaient fait injure à David, envoyèrent prendre à leur solde des Syriens de Rohob, et des Syriens de Soba, vingt mille hommes de pied, mille du roi de Maacha, et douze mille d’Istob.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
7 Ce qu’ayant appris David, il envoya Joab et toute l’armée de ses guerriers.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
8 Les enfants d’Ammon sortirent donc, et rangèrent leur armée en bataille devant l’entrée même de la porte, mais les Syriens de Soba et de Rohob, d’Istob et de Maacha, étaient séparément dans la plaine.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
9 Joab donc, voyant que la bataille était préparée contre lui et par devant et par derrière, prit de toute l’élite d’Israël, et rangea son armée en bataille contre les Syriens;
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
10 Mais le reste du peuple, il le confia à Abisaï son frère, qui le rangea en bataille contre les enfants d’Ammon.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
11 Et Joab dit: Si les Syriens prévalent contre moi, tu me seras en aide; mais si les enfants d’Ammon prévalent contre toi, je te secourrai.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
12 Sois homme courageux, et combattons pour notre peuple, et la cité de notre Dieu: mais le Seigneur fera ce qui est bon à ses yeux.
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
13 C’est pourquoi Joab et le peuple qui était avec lui engagèrent le combat contre les Syriens, qui aussitôt s’enfuirent devant lui.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
14 Mais les enfants d’Ammon voyant que les Syriens avaient fui, s’enfuirent aussi eux-mêmes devant Abisaï, et ils entrèrent dans la ville; et Joab s’en retourna après la défaite des enfants d’Ammon, et vint à Jérusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
15 Les Syriens donc, voyant qu’ils avaient succombé devant Israël, s’assemblèrent tous.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
16 Et Adarézer envoya pour faire venir les Syriens, qui étaient au-delà du fleuve, et il amena leur armée; or, Sobach, maître de la milice d’Adarézer, était leur prince.
Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
17 Lorsque cela eut été annoncé à David, il réunit tout Israël, passa le Jourdain, et vint à Hélam; et les Syriens rangèrent leur armée en bataille contre David, et combattirent contre lui.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
18 Et les Syriens s’enfuirent devant Israël, et David tua des Syriens sept cents hommes qui étaient sur les chariots, et quarante mille cavaliers; et il frappa Sobach, prince de la milice, lequel mourut sur-le-champ.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
19 Or, tous les rois qui étaient venus au secours d’Adarézer, voyant qu’ils étaient vaincus par Israël, furent épouvantés, et cinquante-huit mille hommes s’enfuirent devant Israël. Et ils firent la paix avec Israël, et ils les servirent; et les Syriens craignirent de donner encore secours aux enfants d’Ammon.
Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.