< 2 Chroniques 32 >

1 Après ces choses si fidèlement exécutées, Sennachérib, roi des Assyriens, vint et entra dans Juda; il assiégea les villes fortifiées, voulant les prendre.
Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
2 Lorsqu’Ezéchias eut vu cela, savoir que Sennachérib était venu, et que tout l’effort de la guerre était tourné contre Jérusalem,
Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
3 Il tint conseil avec les princes et les hommes les plus braves, pour boucher les sources des fontaines qui étaient hors de la ville: l’avis de tous l’ayant décidé,
iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
4 Il assembla une très grande multitude, et il boucha toutes les sources, et le ruisseau qui coulait au milieu du pays, disant: C’est de peur que les rois des Assyriens ne viennent, et ne trouvent une abondance d’eau.
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
5 Il bâtit aussi avec grand soin tout le mur qui avait été ruiné, et il construisit les tours au dessus, et en dehors de l’autre mur; il restaura Mello dans la cité de David, et il fit des armes de tout genre et des boucliers;
Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
6 Et il établit ensuite des chefs de combattants dans l’armée; puis il les convoqua sur la place de la porte de la cité, et il parla à leur cœur, disant:
Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
7 Agissez courageusement, et fortifiez-vous: ne craignez point, et ne redoutez point le roi des Assyriens, ni toute cette multitude qui est avec lui; car il y a un plus grand nombre avec nous qu’avec lui.
“Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
8 Car avec lui est un bras de chair; avec nous le Seigneur notre Dieu, qui est notre aide et combat pour nous. Et le peuple fut fortifié par ces paroles d’Ezéchias, roi de Juda.
Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
9 Après que ces choses se furent passées, Sennachérib, roi des Assyriens, envoya ses serviteurs à Jérusalem (car lui-même assiégeait Lachis avec toute son armée) vers Ezéchias, roi de Juda, et vers tout le peuple qui était dans la ville, disant:
Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
10 Voici ce que dit Sennachérib, roi des Assyriens: En qui avez-vous confiance, pour demeurer ainsi assiégés dans Jérusalem?
“Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
11 Est-ce qu’Ézéchias ne vous trompe pas pour vous livrer à la mort par la faim et la soif, vous assurant que le Seigneur votre Dieu vous délivrera de la main du roi des Assyriens?
Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
12 N’est-ce pas cet Ezéchias qui a détruit ses hauts lieux et ses autels, et qui a ordonné à Juda et à Jérusalem, disant: C’est devant un seul autel que vous adorerez, et c’est sur cet autel que vous brûlerez de l’encens?
Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
13 Est-ce que vous ignorez ce que j’ai fait, moi et mes pères, à tous les peuples de la terre? Est-ce que les dieux des nations et de toute la terre ont été assez forts pour délivrer leur pays de ma main?
“Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
14 Quel est celui de tous les dieux des nations que mes pères ont ravagées, qui ait pu délivrer son peuple de ma main, pour que même votre Dieu puisse vous délivrer de ma main?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
15 Qu’Ézéchias ne vous trompe donc point, et que par une vaine persuasion il ne vous joue point: ne le croyez pas. Car si aucun dieu de toutes les nations et de tous les royaumes n’a pu délivrer son peuple de ma main ni de celle de mes pères, conséquemment même votre Dieu ne pourra pas vous délivrer de ma main.
Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
16 Mais les serviteurs de Sennachérib dirent encore beaucoup d’autres choses contre le Seigneur Dieu et contre Ezéchias, son serviteur.
Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
17 Il écrivit aussi des lettres pleines de blasphèmes contre le Seigneur Dieu d’Israël, et il dit contre lui: Comme les dieux des autres nations n’ont pu délivrer leur peuple de ma main, ainsi même le Dieu d’Ezéchias ne pourra pas délivrer son peuple de cette main.
Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
18 De plus, d’une voix forte et en langue judaïque, il criait contre le peuple qui était sur les murs de Jérusalem, pour l’épouvanter et prendre la ville.
Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
19 Ainsi il parla contre le Dieu de Jérusalem comme contre les dieux des peuples de la terre, ouvrages des mains des hommes.
Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
20 Le roi Ezéchias donc, et Isaïe, le prophète, fils d’Amos, prièrent en opposition à ce blasphème, et poussèrent des cris jusqu’au ciel.
Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
21 Et le Seigneur envoya un ange qui frappa tout homme vigoureux, guerrier et le prince de l’armée du roi des Assyriens; et Sennachérib retourna avec ignominie en son pays. Or, lorsqu’il fut entré dans la maison de son dieu, ses fils, qui étaient sortis de ses entrailles, le tuèrent par le glaive.
Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
22 Le Seigneur sauva ainsi Ezéchias et les habitants de Jérusalem de la main de Sennachérib, roi des Assyriens, et de la main de tous, et il leur donna le repos alentour.
Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
23 Beaucoup même portaient des hosties et des sacrifices au Seigneur à Jérusalem, et des présents à Ezéchias, roi de Juda, qui a été exalté après cela devant toutes les nations.
Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
24 En ces jours-là, Ezéchias fut malade jusqu’à la mort, et il pria le Seigneur, et le Seigneur l’exauça, et il lui en donna un signe.
Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
25 Mais Ezéchias ne rendit pas à Dieu selon les biens qu’il avait reçus, parce que son cœur s’éleva, et la colère du Seigneur s’alluma contre lui, contre Juda et contre Jérusalem.
Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
26 Mais ensuite il s’humilia autant lui-même que les habitants de Jérusalem, de ce que son cœur s’était exalté: et c’est pourquoi la colère du Seigneur ne vint point sur eux dans les jours d’Ezéchias.
Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
27 Or Ezéchias fut riche et très illustre; il s’amassa beaucoup de trésors d’argent, d’or, de pierres précieuses, d’aromates, d’armes de tout genre, et de vases de grand prix.
Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
28 Il avait aussi des magasins de blé, devin et d’huile, des écuries pour toute sorte de gros bétail, et des parcs pour des troupeaux.
Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
29 Et il bâtit des villes pour lui; car il avait des troupeaux de brebis et de gros bétail innombrables, parce que le Seigneur lui avait donné des biens en très grande abondance.
Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
30 C’est ce même Ezéchias qui boucha la fontaine supérieure des eaux de Gihon, et les détourna sous terre vers l’occident de la ville de David; en toutes ses œuvres il fit heureusement ce qu’il voulut.
Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
31 Cependant dans le message des princes de Babylone qui avaient été envoyés vers lui pour s’informer du prodige qui était arrivé sur la terre. Dieu l’abandonna pour le tenter et pour faire connaître tout ce qui était en son cœur.
Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
32 Mais le reste des actions d’Ezéchias et de ses miséricordes est écrit dans la vision d’Isaïe, le prophète, fils d’Amos, et dans le Livre des rois de Juda et d’Israël.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
33 Ezéchias dormit avec ses pères, et on l’ensevelit au dessus du sépulcre des fils de David: tout Juda célébra ses funérailles, et tous les habitants de Jérusalem; et Manassé son fils régna en sa place.
Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chroniques 32 >