< 2 Chroniques 20 >

1 Après cela les enfants de Moab et les enfants d’Ammon, et avec eux des Ammonites, s’assemblèrent contre Josaphat pour combattre contre lui.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Et des messagers vinrent et l’annoncèrent à Josaphat, disant: Une grande multitude vient contre vous des lieux qui sont au-delà de la mer et de la Syrie, et voilà qu’ils s’arrêtent à Asasonthamar, qui est Engaddi.
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 Or, Josaphat, saisi de crainte, s’appliqua entièrement à prier le Seigneur, et publia un jeûne dans tout Juda.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 Et Juda s’assembla pour prier le Seigneur, et même tous sortirent de leurs villes pour l’implorer,
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Et lorsque Josaphat se fut levé au milieu de Juda et de Jérusalem dans la maison du Seigneur, devant le parvis nouveau,
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 Il dit: Seigneur Dieu de nos pères, c’est vous qui êtes Dieu dans le ciel, et qui dominez sur tous les royaumes des nations: dans votre main sont la force et la puissance, et personne ne peut vous résister.
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 N’est-ce pas vous, notre Dieu, qui avez tué tous les habitants de cette terre devant votre peuple Israël, et qui l’avez donnée à la postérité d’Abraham, votre ami pour toujours?
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Et ils y ont habité, et ils y ont construit un sanctuaire à votre nom, disant:
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 S’il fond sur nous des maux, un glaive de jugement, une peste, et une famine, nous nous tiendrons en votre présence devant cette maison, dans laquelle a été invoqué votre nom, et nous crierons vers vous dans nos tribulations, et vous nous exaucerez, et vous nous sauverez.
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 Maintenant donc, voilà que les enfants d’Ammon et de Moab, et les habitants de la montagne de Séir, au milieu desquels vous ne permîtes pas à Israël de passer lorsqu’ils sortaient d’Égypte; mais ils se détournèrent d’eux, et ils ne les tuèrent pas.
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 Voilà que ces peuples agissent tout autrement, et ils s’efforcent de nous chasser de la possession que vous nous avez donnée.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Ô notre Dieu, ne les jugerez-vous pas? Certes, nous n’avons pas une assez grande force pour que nous puissions résister à cette multitude qui vient fondre sur nous. Mais, comme nous ignorons ce que nous devons faire, il ne nous reste qu’à diriger nos yeux vers vous.
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Or tout Juda était debout devant le Seigneur, avec leurs petits enfants, leurs femmes et leurs autres enfants.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 Là était aussi Jahaziel, fils de Zacharie, fils de Banaïas, fils de Jéhiel, fils de Mathanias, Lévite de la famille d’Asaph; et l’Esprit de Dieu descendit sur lui au milieu de la multitude;
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Et il dit: Ecoutez, vous tous, Juda, et vous qui habitez Jérusalem, et vous aussi, roi Josaphat: Voici ce que vous dit le Seigneur: Ne craignez point, et ne redoutez point cette multitude; car ce n’est pas votre combat, mais celui de Dieu.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Demain vous descendrez contre eux; car ils doivent monter par le coteau du nom de Sis, et vous les trouverez à l’extrémité du torrent qui est contre le désert de Jéruel.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Ce ne sera pas vous qui combattrez; mais seulement soyez résolus, et vous verrez le secours du Seigneur sur vous, ô Juda et Jérusalem: ne craignez point et ne vous effrayez point; demain vous marcherez contre eux, et le Seigneur sera avec vous.
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 Josaphat donc, et Juda, et tous les habitants de Jérusalem, tombèrent inclinés vers la terre devant le Seigneur, et l’adorèrent.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 Et les Lévites d’entre les enfants de Caath et d’entre les enfants de Coré louaient le Seigneur Dieu d’Israël avec une voix forte et élevée.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Et lorsqu’au matin ils se furent levés, ils sortirent par le désert de Thécué; et, lorsqu’ils étaient en marche, Josaphat, debout au milieu d’eux, dit: Ecoutez-moi, hommes de Juda, et vous tous, habitants de Jérusalem: mettez votre confiance dans le Seigneur votre Dieu, et vous serez en sûreté; croyez à ses prophètes, et toutes choses seront prospères.
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Et il donna ses avis au peuple, et il établit les chantres du Seigneur pour le louer dans leurs diverses bandes, marcher devant l’armée, et d’une voix unanime dire: Rendez gloire au Seigneur, parce que sa miséricorde est éternelle.
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Et lorsqu’ils eurent commencé à chanter ainsi des louanges, le Seigneur tourna tous les desseins des ennemis contre eux-mêmes, c’est-à-dire des enfants d’Ammon et de Moab, et des habitants de la montagne de Séir qui étaient sortis pour combattre contre Juda; et ils furent battus.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Car les fils d’Ammon et de Moab se levèrent contre les habitants de la montagne de Séir, pour les massacrer et les exterminer; et lorsqu’ils eurent achevé, s’étant aussi tournés contre eux-mêmes, ils tombèrent sous leurs coups mutuels.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Or, lorsque Juda fut venu à l’échauguette qui regarde le désert, il vit de loin tout le pays dans une grande étendue plein de cadavres, et qu’il ne restait personne qui eût pu échapper à la mort.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Josaphat vint donc, et tout le peuple avec lui, pour enlever les dépouilles des morts, et ils trouvèrent, parmi les cadavres, des meubles divers, des vêtements aussi et des vases très précieux, et ils les pillèrent; en sorte qu’ils ne purent tout emporter, ni enlever durant trois jours les dépouilles, à cause de la quantité du butin.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 Or, le quatrième jour, ils s’assemblèrent dans la vallée de la Bénédiction; car, parce qu’ils y avaient béni le Seigneur, ils appelèrent ce lieu vallée de Bénédiction, jusqu’au présent jour.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Ensuite tout homme de Juda, et tous les habitants de Jérusalem, et Josaphat à leur tête, retournèrent à Jérusalem dans une grande allégresse, parce que le Seigneur leur avait donné de la joie au sujet de leurs ennemis.
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 Ils entrèrent donc à Jérusalem dans la maison du Seigneur avec des psaltérions, des harpes et des trompettes.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Mais la terreur du Seigneur fondit sur tous les royaumes des pays voisins, lorsqu’ils eurent appris que le Seigneur avait combattu contre les ennemis d’Israël.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Et le royaume de Josaphat se reposa, et Dieu lui donna la paix alentour.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Josaphat régna donc sur Juda; et il avait trente-cinq ans, lorsqu’il commença à régner: or il régna vingt-cinq ans à Jérusalem; et le nom de sa mère était Azuba, fille de Sélahi.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Et il marcha dans les voies de son père Asa, et il ne s’en détourna point, faisant ce qui était agréable devant le Seigneur.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Cependant il ne détruisit pas les hauts lieux, et le peuple n’avait pas encore dirigé son cœur vers le Seigneur Dieu de ses pères.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Or le reste des actions de Josaphat, des premières et des dernières, est écrit dans l’histoire que Jéhu, fils d’Hanani, a insérée dans les Livres des rois d’Israël.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Après cela, Josaphat, roi de Juda, contracta amitié avec Ochozias, roi d’Israël, dont les œuvres furent très impies.
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 Et il contribua à ce qu’ils fissent des vaisseaux, qui iraient à Tharsis; ils firent donc une flotte à Asiongaber.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 Mais Eliézer, fils de Dodaü de Marésa, prophétisa à Josaphat, disant: Parce que vous avez fait alliance avec Ochozias, le Seigneur Dieu a frappé vos œuvres, et vos vaisseaux ont été brisés, et ils n’ont pu aller à Tharsis.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.

< 2 Chroniques 20 >