< 1 Thessaloniciens 1 >
1 Paul, Silvain et Timothée, à l’Eglise des Thessaloniciens, en Dieu le Père, et le Seigneur Jésus-Christ.
Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu.
2 Grâce à vous et paix. Nous rendons continuellement grâces à Dieu pour vous tous, faisant sans cesse mémoire de vous dans nos prières,
Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu.
3 Nous souvenant devant notre Dieu et Père des œuvres de votre foi, des travaux de votre charité, et de la constance de votre espérance en Notre Seigneur Jésus-Christ,
Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
4 Sachant, mes frères chéris de Dieu, quelle a été votre élection,
Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani,
5 Et que notre Evangile ne vous a pas été annoncé en paroles seulement, mais avec des miracles, avec l’Esprit-Saint et une grande plénitude de ses dons; car vous savez quels nous avons été parmi vous pour votre bien.
chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni.
6 Et vous, vous êtes devenus les imitateurs de nous et du Seigneur, recevant la parole au milieu de beaucoup de tribulations avec la joie de l’Esprit-Saint;
Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera.
7 En sorte que vous êtes devenus un modèle pour tous les croyants dans la Macédoine et dans l’Achaïe.
Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya.
8 Car par vous la parole du Seigneur s’est répandue, non seulement dans la Macédoine et dans l’Achaïe, mais la foi que vous avez en Dieu a même pénétré en tout lieu, de sorte que nous n’avons nullement besoin d’en rien dire;
Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu,
9 Puisqu’eux-mêmes racontent quelle entrée nous avons faite chez vous, et comment vous vous êtes convertis des idoles à Dieu, pour servir le Dieu vivant et véritable,
pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona.
10 Et attendre du ciel son Fils Jésus (qu’il a ressuscité d’entre les morts), qui nous a délivrés de la colère à venir.
Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.