< 1 Samuel 20 >
1 Or, David s’enfuit de Naïoth, qui est en Ramatha, et étant venu, il dit devant Jonathas: Qu’ai-je fait? quelle est mon iniquité, et quel est mon péché contre ton père, puisqu’il cherche mon âme?
Tsono Davide anathawa ku Nayoti ku Rama ndi kupita kwa Yonatani ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ine ndinachita chiyani? Kodi ndinalakwa chiyani? Kodi abambo ako ndinawalakwira chiyani kuti azifuna kundipha?”
2 Jonathas lui répondit: À Dieu ne plaise! tu ne mourras pas; car mon père ne fait rien de grand ni de petit, s’il ne me l’a fait savoir auparavant. C’est donc la seule parole que mon père m’ait célée? Cela ne sera nullement.
Yonatani anayankha kuti, “Sizitheka! Iwe sufa ayi! Taona abambo anga sachita chinthu chilichonse chachikulu kapena chachingʼono wosandiwuza ine. Tsopano abambo anga angandibisire bwanji zimenezi? Sichoncho ayi.”
3 Et il jura de nouveau à David. Et celui-ci dit: Ton père sait certainement que j’ai trouvé grâce à tes yeux, et il dira: Que Jonathas ne sache point ceci, de peur qu’il ne soit contristé. Bien plus, le Seigneur vit, et ton âme vit! car c’est d’un seul pas (pour ainsi dire) que moi et la mort nous sommes séparés.
Koma Davide analumbira kuti, “Abambo ako akudziwa bwino lomwe kuti iwe umandikonda ndipo iwo amaganiza kuti, Yonatani sayenera kudziwa zimenezi mwina adzamva chisoni kwambiri. Komabe, pali Yehova ndi pali iwe, imfa sinanditalikire.”
4 Et Jonathas répondit à David: Tout ce que me dira ton âme, je le ferai pour toi.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Chilichonse chimene iwe ukufuna kuti ndichite, ndidzakuchitira.”
5 David dit alors à Jonathas: Voici que les calendes sont demain, et moi d’après l’usage, j’ai coutume de m’asseoir auprès du roi pour manger; laisse-moi donc aller me cacher dans la campagne jusqu’au soir du troisième jour.
Ndipo Davide anati, “Taona mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano, ndipo ine ndiyenera kukadya ndi mfumu. Koma undilole ndipite ndikabisale mʼmunda mpaka mkuja madzulo.
6 Si, regardant, ton père me demande, tu lui répondras: David m’a demandé d’aller promptement à Bethléhem, sa ville; parce que là les victimes solennelles sont présentées pour tous ceux de sa tribu.
Ngati abambo ako akafunsa za ine, ukawawuze kuti, ‘Davide anandiwumiriza kuti ndimulole apite msanga kwawo ku Betelehemu, chifukwa akupereka nsembe yapachaka ya banja lonse.’
7 S’il dit: Bien, la paix sera faite avec ton serviteur; mais s’il s’irrite, sache que sa malice est à son comble.
Akanena kuti, ‘Wachita bwino,’ ndiye kuti zinthu zindiyendera bwino ine mtumiki wako. Koma ngati akapsa mtima, ndiye udziwe kuti iwo atsimikiza zondichita zoyipa.
8 Fais donc miséricorde à ton serviteur, puisque tu m’as fait faire, à moi, ton serviteur, l’alliance du Seigneur avec toi; mais s’il est quelque iniquité en moi, tue-moi toi-même, et ne m’introduis point auprès de ton père.
Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”
9 Et Jonathas dit: Loin de toi une pareille chose; car il ne peut pas se faire, que je sache d’une manière certaine que la malice de mon père contre toi est à son comble, et que je ne t’en informe point.
Yonatani anati, “Sizitheka! Ndikanadziwa kuti abambo anga atsimikiza kuti akuchite choyipa, kodi sindikanakuwuza?”
10 Et David répondit à Jonathas: Qui m’informera, si par hasard ton père répond durement à mon sujet?
Davide anafunsa kuti, “Adzandiwuza ndani ngati abambo ako akuyankhe mwaukali?”
11 Et Jonathas dit à David: Viens, et sortons dehors dans la campagne. Et lorsqu’ils furent sortis tous deux dans la campagne,
Yonatani anawuza Davide kuti, “Tiyeni tikayende ku mundako.” Ndipo anapita onse awiri.
12 Jonathas dit à David: Seigneur Dieu d’Israël, si je découvre le dessein de mon père demain, ou après-demain, et qu’il y ait quelque chose de bon pour David, et que je n’envoie aussitôt vers toi, et que je ne t’en donne point connaissance,
Kenaka Yonatani anawuza Davide kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akhale mboni! Ine ndikadzafunsa abambo anga nthawi yonga ino mmawa kapena mkuja, ndipo ndikadzapeza kuti akukufunira zabwino, ine ndidzatuma mawu kuti udziwe.
13 Que le Seigneur fasse ceci à Jonathas, et qu’il ajoute cela. Mais si la malice de mon père persévère contre toi, j’ouvrirai ton oreille, et je te laisserai partir, afin que tu ailles en paix, et que le Seigneur soit avec toi, comme il a été avec mon père.
Koma ngati abambo anga atsimikiza kukuchita choyipa, Yehova andilange ine Yonatani, ndipotu kwambiri ngati sindidzakudziwitsa ndi kukulola kuti upite mu mtendere. Yehova akhale nawe monga anakhalira ndi abambo anga.
14 Et si je vis, tu useras envers moi de la miséricorde du Seigneur; mais si je meurs,
Ndikakhalabe ndi moyo udzandionetse kukoma mtima monga kwa Yehova nthawi yonse ya moyo wanga, kuti ine ndisaphedwe.
15 Tu ne retireras point à jamais ta miséricorde de ma maison, quand le Seigneur aura exterminé de la terre les ennemis de David jusqu’au dernier. Que le Seigneur enlève Jonathas de sa maison, et qu’il tire vengeance, des ennemis de David.
Ndipo usadzaleke kuchitira chifundo banja langa. Pamene Yehova adzawatha adani onse a Davide pa dziko lapansi.”
16 Jonathas fit donc alliance avec la maison de David, et le Seigneur tira vengeance des ennemis de David.
“Dzina la ine Yonatani lisadzafafanizidwe nawo pamodzi. Yehova alange adani onse a Davide.”
17 Et Jonathas renouvela ses serments à David, parce qu’il l’aimait; car il l’aimait comme son âme.
Kenaka Yonatani anamulumbiritsanso Davide kuti asaleke kumukonda, pakuti ankamukonda monga ankadzikondera yekha.
18 Et Jonathas lui dit: Demain sont les calendes, et on s’enquerra de toi;
Kenaka Yonatani anawuzanso Davide kuti, “Mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Zidzadziwika kuti iwe palibe chifukwa mpando wako udzakhala wopanda munthu.
19 Car on s’enquerra de ta place jusqu’après demain. Tu descendras donc, te hâtant, et tu viendras dans le lieu où tu dois être cachée au jour auquel il est permis de travailler, et tu te tiendras près de la pierre dont le nom est Ezel.
Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.
20 Et moi je décocherai trois flèches près de la pierre, et je les lancerai, comme m’exerçant à atteindre le but.
Ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, ngati ndikulasa chinthu.
21 J’enverrai aussi mon serviteur, lui disant: Va, et apporte-moi les flèches.
Ndipo ndidzatuma mnyamata ndi kuti, ‘Pita ukatole miviyo!’ Ngati ndidzanena kwa iye kuti, ‘Taona, mivi ili mbali yakuno, kayitole,’ iwe ukatuluke, pakuti ndikulumbira, pali Yehova Wamoyo, ndiye kuti zako zili bwino, palibe choopsa chilichonse.
22 Si je dis à mon serviteur: Voici que les flèches sont en deçà de toi, prends-les; viens toi-même à moi, parce que la paix est avec toi, et il n’y a rien de mal; le Seigneur vit! Mais si je parle ainsi à mon serviteur: Voici que les flèches sont au-delà de toi; va en paix, parce que le Seigneur te laisse aller.
Koma ndikadzati, ‘Taona mivi ili patsogolo pako,’ iwe udzachoke chifukwa Yehova ndiye walola kuti uchokepo.
23 Quant à la parole que nous avons dite, moi et toi, que le Seigneur soit entre moi et toi pour toujours.
Tsono zimene tapanganazi Yehova ndiye mboni pakati pa iwe ndi ine mpaka muyaya.”
24 David donc se cacha dans la campagne, et vinrent les calendes, et le roi s’assit pour manger du pain.
Choncho Davide anakabisala mʼmunda ndipo nthawi ya chikondwerero cha mwezi watsopano itakwana mfumu Sauli anadzakhala pansi kuti adye.
25 Et lorsque le roi se fut assis (selon la coutume) sur son siège près de la muraille, Jonathas se leva; Abner s’assit à côté de Saül, et la place de David parut vide.
Iye anakhala pa malo ake a nthawi zonse pafupi ndi khoma moyangʼanana ndi Yonatani, ndipo Abineri anakhala moyandikana ndi Sauli, koma pa malo a Davide panalibe munthu.
26 Et Saül ne dit rien en ce jour-là; car il pensait que peut-être il était arrivé à David de n’être pas pur, et de n’avoir pas été purifié.
Sauli sananene chilichonse tsiku limenelo pakuti ankaganiza kuti “Chilipo chimene chachitika ndi Davide. Mwina mwake ngosayenera za chipembedzo.”
27 Et lorsque fut venu le second jour après les calendes, la place de David parut encore vide. Et Saül demanda à Jonathas, son fils: Pourquoi le fils d’Isaï n’est-il point venu, ni hier, ni aujourd’hui, pour manger?
Koma pa tsiku lachiwiri la chikondwerero cha mwezi watsopano pamalo pa Davide panalibenso munthu. Kenaka Sauli anafunsa Yonatani kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwana wa Yese sanabwere kudzadya, dzulo ngakhale lero?”
28 Et Jonathas répondit à Saül: Il m’a demandé instamment d’aller à Bethléhem,
Yonatani anayankha kuti, “Davide anandiwumiriza kuti ndimulole kuti apite ku Betelehemu.
29 Et il a dit: Laissez-moi aller, parce qu’il y a un sacrifice solennel en ma cité, un de mes frères m’a appelé; maintenant donc, si j’ai trouvé grâce à vos yeux, j’irai aussitôt, et je verrai mes frères. C’est pour cette raison qu’il n’est pas venu à la table du roi.
Anati, ‘Undilole ndipite, chifukwa banja lathu likupereka nsembe mu mzindamo ndipo mʼbale wanga wandiwumiriza kuti ndikakhale nawo. Ngati wandikomera mtima, chonde ndilole ndipite ndikaone abale anga.’ Nʼchifukwa chake sanabwere kudzadya ndi mfumu.”
30 Or, Saül irrité contre Jonathas, lui dit: Fils d’une femme qui ravit volontiers un homme, est-ce que j’ignore que tu aimes le fils d’Isaï, à ta confusion, et à la confusion de ton ignominieuse mère?
Sauli anamupsera mtima Yonatani ndipo namuwuza kuti, “Iwe mwana wobadwa mwa mkazi wamakhalidwe oyipa ndi wowukira! Kodi ukuyesa kuti ine sindikudziwa kuti umagwirizana ndi mwana wa Yese, amene akufuna kukuchititsa manyazi iwe ndi amayi ako?
31 Car durant tous les jours que le fils d’Isaï vivra sur la terre, tu ne seras pas affermi, ni toi, ni ton royaume. C’est pourquoi, envoie dès maintenant, et amène-le-moi, parce que c’est un fils de mort.
Mwana wa Yese akakhala ndi moyo pa dziko lapansi lino, iwe sudzakhala mfumu. Tsopano tumiza munthu akamutenge kubwera naye kwa ine, pakuti Davide ayenera kufa basi!”
32 Mais Jonathas répondant à Saül, son père, dit: Pourquoi mourra-t-il? qu’a-t-il fait?
Yonatani anafunsa abambo ake kuti, “Nʼchifukwa chiyani mufuna kuti Davide aphedwe? Iye walakwa chiyani?”
33 Et Saül saisit sa lance pour le frapper. Et Jonathas comprit qu’il avait été arrêté par son père de tuer David.
Apo Sauli anamuponyera mkondo wake kuti amuphe. Tsono Yonatani anadziwa kuti abambo ake atsimikiza mtima kuti aphe Davide.
34 Jonathas donc se leva de table dans une colère de fureur, et il ne mangea pas de pain le second jour des calendes; car il était contristé au sujet de David, parce que son père l’avait outragé.
Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.
35 Et lorsque le matin fut venu, Jonathas vint à la campagne, selon la convention faite avec David, et un petit serviteur avec lui,
Tsono mmawa Yonatani anapita ku munda kumene anapangana ndi Davide. Anali ndi mnyamata wake.
36 Et il dit à son serviteur: Va, et apporte-moi les flèches que je tire. Et lorsque le serviteur eut couru, il tira une autre flèche au-delà du serviteur.
Tsono anawuza mnyamatayo kuti, “Thamanga ukatole muvi umene nditi ndiponye.” Mnyamatayo akuthamanga Yonatani anaponya muvi patsogolo pa mnyamatayo.
37 C’est pourquoi le serviteur vint à l’endroit du trait qu’avait lancé Jonathas; et Jonathas cria derrière le serviteur, et dit: La voilà la flèche, là-bas, au-delà de toi.
Mnyamatayo atafika pamene muvi wa Yonatani unagwera,
38 Et Jonathas cria encore derrière le serviteur, disant: Hâte-toi vite, ne t’arrête point. Or le serviteur de Jonathas recueillit les flèches, et les apporta à son maître;
Yonatani anayitananso mnyamatayo kuti, “Fulumira, pita msanga usayime.” Choncho mnyamatayo anatola muvi uja ndi kubwera nayo kwa mbuye wake.
39 Quant à ce qui se faisait, il l’ignorait entièrement; car Jonathas et David seulement savaient la chose.
(Mnyamatayo sanadziwe chimene chimachitika koma Yonatani ndi Davide ndiwo ankadziwa).
40 Ensuite Jonathas donna ses armes au serviteur, et lui dit: Va, et porte-les à la ville.
Pambuyo pake Yonatani anapereka zida zake za nkhondo kwa mnyamatayo ndipo anati, “Pita, nyamula ubwerere nazo ku mzinda.”
41 Et lorsque le serviteur s’en fut allé, David se leva du lieu, qui regardait le midi, et tombant incliné vers la terre, il se prosterna par trois fois; et, s’embrassant l’un l’autre, ils pleurèrent ensemble, mais David beaucoup plus.
Mnyamatayo anapita. Kenaka Davide anatuluka ku mbali ina ya mulu wa miyala uja, nadzigwetsa pansi ndi kugunditsa nkhope yake pansi katatu. Anapsompsona nayamba kulira onse awiri, koma Davide analira kwambiri.
42 Jonathas donc dit à David: Va en paix; tout ce que nous avons juré tous deux, au nom du Seigneur, disant: Que le Seigneur soit entre moi et toi, et entre ma postérité et ta postérité pour toujours… Et David se leva et s’en alla; mais Jonathas rentra dans la ville.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Pita mu mtendere pakuti ife awiri tinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Yehova ndiye akhale mboni pakati pa iwe ndi ine ndiponso pakati pa zidzukulu zako ndi zidzukulu zanga kwa nthawi yonse.’” Kenaka Davide anachoka, ndipo Yonatani anabwerera ku mzinda kuja.