< 1 Rois 21 >
1 Or après ces événements, en ce même temps, Naboth, le Jezrahélite, avait une vigne qui était dans Jezrahel, près du palais d’Achab, roi de Samarie.
Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
2 Achab parla à Naboth, disant: Donne-moi ta vigne, afin que je me fasse un jardin potager, parce qu’elle est voisine, et je te donnerai en sa place une vigne meilleure, ou, si ta juges plus commode pour toi, le prix en argent, selon ce qu’elle vaut.
Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
3 Naboth lui répondit: Que le Seigneur me soit propice, pour que je ne vous donne point l’héritage de mes pères!
Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
4 Achab vint donc en sa maison, indigné et frémissant, à cause de la parole que lui avait répondue Naboth, le Jezrahélite, disant: Je ne vous donnerai point l’héritage de mes pères. Et, se jetant sur son lit, il tourna sa face vers la muraille, et ne mangea point du pain.
Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
5 Mais Jézabel, sa femme, entra auprès de lui, et lui dit: Qu’est-ce que cela? Pourquoi votre âme est-elle contristée? et pourquoi ne mangez-vous point du pain?
Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
6 Il lui répondit: J’ai parlé à Naboth, le Jezrahélite, et je lui ai dit: Donne-moi ta vigne, en acceptant de l’argent, ou si cela te plaît, je te donnerai une vigne meilleure en sa place. Et lui m’a répondu: Je ne vous donnerai point ma vigne.
Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
7 Jézabel, sa femme, lui dit donc: Vous avez une grande autorité et vous gouvernez bien le royaume d’Israël. Levez-vous et mangez du pain, et ayez l’esprit calme; c’est moi qui vous donnerai la vigne de Naboth, le Jezrahélite.
Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
8 C’est pourquoi elle écrivit des lettres au nom d’Achab, et les scella de l’anneau du roi, et elle les envoya aux anciens et aux grands qui étaient dans la ville de Naboth, et habitaient avec lui.
Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
9 Or le sens de ces lettres était celui-ci: Publiez un jeûne, et faites asseoir Naboth entre les premiers du peuple,
Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
10 Et subornez contre lui deux hommes, fils de Bélial, et qu’ils disent ce faux témoignage: Il a blasphémé Dieu et le roi; ensuite menez-le hors de la ville, lapidez-le, et qu’ainsi il meure.
Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
11 Ses concitoyens donc, les anciens et les grands qui habitaient avec lui dans la ville, firent comme leur avait ordonné Jézabel, et comme il était écrit dans la lettre qu’elle leur avait envoyée:
Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
12 Ils publièrent un jeûne, et firent asseoir Naboth entre les premiers du peuple.
Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
13 Et deux hommes, fils du diable, ayant été amenés, ils les firent asseoir en face de lui; mais ceux-ci, comme hommes diaboliques, rendirent contre lui ce témoignage devant la multitude: Naboth a blasphémé Dieu et le roi. C’est pourquoi on l’amena hors de la ville, et on le lapida.
Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
14 Et ils envoyèrent à Jézabel, disant: Naboth a été lapidé, et il est mort.
Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
15 Or il arriva que, lorsque Jézabel eut appris que Naboth avait été lapidé et qu’il était mort, elle dit à Achab: Levez-vous, et prenez possession de la vigne de Naboth, le Jezrahélite, qui n’a pas voulu se rendre à votre désir, ni vous la donner en acceptant de l’argent; car Naboth ne vit plus, mais il est mort.
Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
16 Lorsque Achab eut appris cela, c’est-à-dire que Naboth était mort, il se leva, et il descendait dans la vigne de Naboth, le Jezrahélite, pour en prendre possession.
Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
17 La parole du Seigneur fut donc adressée à Elle, le Thesbite, disant:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
18 Lève-toi, et descends à la rencontre d’Achab, roi d’Israël, qui est dans Samarie: car voilà qu’il descend dans la vigne de Naboth pour en prendre possession.
“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
19 Et tu lui parleras, disant: Voici ce que dit le Seigneur: Tu as tué, et de plus tu as pris possession. Et après cela, tu ajouteras: Voici ce que dit le Seigneur: En ce même lieu dans lequel les chiens ont léché le sang de Naboth, ils lécheront aussi ton sang.
Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
20 Et Achab dit à Elie: Est-ce que tu m’as trouvé ton ennemi? Elie lui répondit: Je vous ai trouvé tel, parce que vous vous êtes vendu pour faire le mal en la présence du Seigneur.
Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
21 Voilà que j’amènerai des maux sur toi; je moissonnerai ta postérité, et je tuerai d’Achab celui qui urine contre une muraille, celui qui est renfermé, et celui qui est le dernier dans Israël.
Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
22 Et je rendrai ta maison comme la maison de Jéroboam, fils de Nabath, et comme la maison de Baasa, fils d’Ahia, parce que tu as agi de manière à provoquer mon courroux, et que tu as fait pécher Israël.
Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
23 Mais le Seigneur a parlé aussi de Jézabel, disant: Les chiens mangeront Jézabel dans la campagne de Jezrahel.
“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
24 Si Achab meurt dans la ville, les chiens mangeront sa chair; et s’il meurt dans la campagne, les oiseaux du ciel le mangeront.
“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
25 Ainsi, il n’y eut point un autre semblable à Achab, qui se vendit pour faire le mal en la présence du Seigneur; car Jézabel, sa femme, l’excita,
(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
26 Et il devint tellement abominable, qu’il suivait les idoles qu’avaient faites les Amorrhéens, que le Seigneur extermina à la face des enfants d’Israël.
Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
27 C’est pourquoi, lorsque Achab eut entendu ces paroles, il déchira ses vêtements, couvrit sa chair d’un cilice, jeûna et dormit avec le sac, et marcha la tête baissée.
Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
28 Et la parole du Seigneur fut adressée à Elie, le Thesbite, disant:
Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
29 N’as-tu pas vu Achab humilié devant moi? Puis donc qu’il s’est humilié à cause de moi, je n’amènerai pas le malheur en ses jours, mais pendant les jours de son fils, je porterai le malheur dans sa maison.
“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”