< 1 Rois 16 >
1 Or la parole du Seigneur fut adressée à Jéhu, fils d’Hanani, contre Baasa, disant:
Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
2 Quand je t’ai élevé de la poussière, et je t’ai établi chef sur mon peuple Israël, toi au contraire, tu as marché dans la voie de Jéroboam, et tu as fait pécher mon peuple Israël, pour m’irriter par leurs péchés:
“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
3 Voilà que moi, je moissonnerai la postérité de Baasa et la postérité de sa maison, et je ferai de ta maison ce que j’ai fait de la maison de Jéroboam, fils de Nabath.
Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
4 Celui de la race de Baasa qui mourra dans la ville, les chiens le mangeront, et celui qui mourra dans la campagne, les oiseaux du ciel le mangeront.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
5 Mais le reste des actions de Baasa, et tout ce qu’il fit, et ses combats, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois d’Israël?
Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
6 Baasa dormit donc avec ses pères, et il fut enseveli à Thersa; et Ela son fils régna en sa place.
Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
7 Mais lorsque par l’entremise de Jéhu le prophète, fils d’Hanani, la parole du Seigneur eut été adressée contre Baasa, contre sa maison, et contre tout le mal qu’il avait fait devant le Seigneur, pour l’irriter par les œuvres de ses mains, afin que sa maison devînt comme la maison de Jéroboam, Baasa pour ce motif même le tua, c’est-à-dire, Jéhu, fils d’Hanani le prophète,
Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
8 La vingt-sixième année d’Asa, roi de Juda, Ela, fils de Baasa, régna sur Israël à Thersa pendant deux ans;
Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
9 Car son serviteur Zambri, chef de la moitié de sa cavalerie, se révolta contre lui; or Ela était à Thersa buvant et ivre, dans la maison d’Arsa, gouverneur de Thersa.
Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
10 Zambri donc se jetant sur lui, le frappa et le tua la vingt-septième année d’Asa, roi de Juda, et il régna en sa place.
Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
11 Et lorsqu’il fut roi et qu’il fut assis sur son trône, il tua toute la maison de Baasa, et il ne laissa d’elle aucun urinant contre une muraille, ni ses proches, ni ses amis.
Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
12 Ainsi Zambri détruisit toute la maison de Baasa, selon la parole que le Seigneur avait dite à Baasa par l’entremise de Jéhu le prophète,
Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
13 À cause de tous les péchés de Baasa et des péchés d’Ela son fils, qui avaient péché et fait pécher tout Israël, provoquant le Seigneur Dieu d’Israël par leurs vanités.
chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
14 Mais le reste des actions d’Ela, et tout ce qu’il fit, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois d’Israël?
Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
15 La vingt-septième année d’Asa, roi de Juda, Zambri régna pendant sept jours à Thersa: or l’armée d’Israël assiégeait Gebbethon, ville des Philistins.
Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
16 Et lorsqu’il eut appris que Zambri s’était révolté et avait tué le roi, tout Israël se donna pour roi Amri, qui était prince de la milice d’Israël, et en ce jour-là dans le camp.
Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
17 Amri monta donc, et tout Israël avec lui, de Gebbethon, et ils assiégeaient Thersa.
Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
18 Or Zambri, voyant que la ville allait être prise d’assaut, entra dans le palais et se brûla avec la maison royale: et il mourut
Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
19 Dans ses péchés qu’il avait commis, faisant le mal devant le Seigneur, et marchant dans la voie de Jéroboam et dans le péché par lequel il avait fait pécher Israël.
chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
20 Mais le reste des actions de Zambri, de ses embûches et de sa tyrannie, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois d’Israël?
Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
21 Alors le peuple d’Israël fut divisé en deux parties: la moitié du peuple suivait Thebni, fils de Gineth, pour l’établir roi, et l’autre moitié. Amri.
Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
22 Mais le peuple qui était avec Amri l’emporta sur le peuple qui était avec Thebni, fils de Gineth; or Thebni mourut, et Amri régna.
Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
23 Depuis la trente-unième année d’Asa, roi de Juda, Amri régna sur Israël pendant douze ans: à Thersa, il régna six ans.
Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
24 Et il acheta la montagne de Samarie à Somer, pour deux talents d’argent; et il la bâtit, et il appela la ville qu’il avait construite Samarie, du nom de Somer, le maître de la montagne.
Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
25 Mais Amri fit le mal en la présence du Seigneur, et il agit méchamment, plus que tous ceux qui furent avant lui.
Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
26 Et il marcha dans toute la voie de Jéroboam, fils de Nabath, et dans ses péchés par lesquels il avait fait pécher Israël, pour irriter le Seigneur Dieu d’Israël par ses vanités.
Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
27 Mais le reste des actions d’Amri et les combats qu’il donna, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois d’Israël?
Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
28 Et Amri dormit avec ses pères et fut enseveli à Samarie, et Achab, son fils, régna en sa place.
Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Mais Achab, fils d’Amri, régna sur Israël la trente-huitième année d’Asa, roi de Juda. Et Achab, fils d’Amri, régna sur Israël à Samarie pendant vingt-deux ans.
Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
30 Et Achab, fils d’Amri, fit le mal en la présence du Seigneur plus que tous ceux qui furent avant lui.
Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
31 Et il ne lui suffit pas de marcher dans les péchés de Jéroboam, fils de Nabath; de plus, il prit pour femme Jézabel, fille d’Ethbaal, roi des Sidoniens, et il alla, et servit Baal et l’adora.
Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
32 Et il éleva un autel à Baal dans le temple de Baal qu’il avait bâti à Samarie,
Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
33 Et il planta le bois sacré; et Achab ajouta à son œuvre en irritant le Seigneur Dieu d’Israël plus que tous les rois d’Israël qui furent avant lui.
Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
34 Pendant ses jours, Hiel, de Béthel, bâtit Jéricho: il en jeta les fondements sur Abiram, son premier-né, et il en posa les portes sur Ségub, son dernier fils, selon la parole que le Seigneur avait dite par l’entremise de Josué, fils de Nun.
Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.