< 1 Chroniques 14 >

1 Hiram, roi de Tyr, envoya aussi des messagers à David, et des bois de cèdre, et des maçons, et des charpentiers, pour lui bâtir une maison.
Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu.
2 Et David reconnut que le Seigneur l’avait confirmé roi sur Israël, et qu’il avait élevé son royaume sur son peuple Israël.
Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
3 Il prit encore d’autres femmes à Jérusalem, et il engendra des fils et des filles.
Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
4 Or voici les noms de ceux qui lui naquirent à Jérusalem: Samua et Sobad, Nathan et Salomon,
Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
5 Jébahar, Elisua, et Eliphalet,
Ibihari, Elisua, Elipeleti,
6 Noga aussi, et Napheg et Japhia,
Noga, Nefegi, Yafiya,
7 Elisama, Baaliada et Eliphalet.
Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.
8 Or les Philistins, apprenant que David avait été oint comme roi sur tout Israël, montèrent tous pour le chercher: ce qu’ayant appris David, il sortit au-devant d’eux.
Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo.
9 Cependant les Philistins, venant, se répandirent dans la vallée de Raphaïm.
Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu.
10 Alors David consulta le Seigneur, disant: Monterai-je contre les Philistins, et les livrerez-vous en ma main? Et le Seigneur lui répondit: Monte, et je les livrerai en ta main.
Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”
11 Lors donc que ceux-ci eurent monté à Baalpharasim, David les battit là, et dit: Le Seigneur a dispersé mes ennemis par ma main, comme les eaux se dispersent: et c’est pourquoi ce lieu fut appelé Baalpharasim.
Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu.
12 Et les Philistins laissèrent là leurs dieux, et David commanda qu’ils fussent brûlés.
Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.
13 Les Philistins firent encore une autre fois irruption, et se répandirent dans la vallée.
Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo.
14 Et David consulta Dieu de nouveau; et Dieu lui dit: Ne monte pas après eux, mais éloigne-toi d’eux; et tu viendras contre eux, vis-à-vis des poiriers.
Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
15 Et lorsque tu entendras le bruit de quelqu’un qui marche au haut des poiriers, alors tu sortiras pour la bataille; car Dieu sortira devant toi pour battre le camp des Philistins.
Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
16 David fit donc comme Dieu lui avait ordonné; et il battit le camp des Philistins, depuis Gabaon jusqu’à Gazer.
Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.
17 Ainsi le nom de David se répandit dans toutes les contrées, et le Seigneur inspira la terreur de ce prince à toutes les nations.
Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.

< 1 Chroniques 14 >