< Psaumes 144 >
1 De David. Béni soit l'Éternel, qui est mon rocher: Il exerce mes mains au combat. Et mes doigts à la bataille!
Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
2 Il est mon bienfaiteur et ma forteresse, Ma haute retraite et mon libérateur, Mon bouclier et mon refuge. Celui qui range mon peuple sous ma loi!
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
3 Éternel, qu'est-ce que l'homme, Pour que tu prennes soin de lui, Et le fils de l'homme, pour que tu en tiennes compte?
Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
4 L'homme est semblable à un souffle; Ses jours sont comme l'ombre qui passe.
Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
5 Éternel, abaisse tes cieux et descends; Touche les montagnes, et qu'elles soient couvertes de fumée!
Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
6 Fais briller l'éclair, et disperse mes ennemis: Lance tes flèches, et mets-les en déroute!
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
7 Étends tes mains d'en haut; Délivre-moi, et retire-moi des grandes eaux, De la main des fils de l'étranger,
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
8 Dont la bouche profère le mensonge, Dont la main droite est une main trompeuse.
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
9 Dieu, je chanterai à ta gloire un cantique nouveau. Je te célébrerai sur la lyre à dix cordes,
Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 Toi qui donnes la délivrance aux rois, Qui sauves David, ton serviteur, de l'épée meurtrière.
kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
11 Délivre-moi, et arrache-moi au joug des fils de l'étranger, Dont la bouche ne profère que le mensonge. Dont la main droite est une main trompeuse!
Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
12 Que nos fils, dans leur jeune âge. Croissent comme des plants vigoureux. Que nos filles soient comme des colonnes sculptées. Qui ornent les angles d'un palais!
Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 Que nos celliers soient pleins, Regorgeant de toutes sortes de biens. Que nos brebis se multiplient par milliers, par dix milliers. Dans nos campagnes!
Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
14 Que nos génisses soient fécondes! Qu'il n'y ait ni brèches dans nos murs, ni attaque, Ni cris d'alarme dans nos places.
Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
15 Heureux le peuple dont tel est le partage! Heureux le peuple dont l'Éternel est le Dieu!
Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.