< Marc 6 >
1 Jésus, étant parti de là, vint dans son pays, et ses disciples le suivirent.
Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
2 Quand le sabbat fut venu, il se mit à enseigner dans la synagogue; et la multitude qui l'écoutait était dans l'étonnement et disait: D'où cela lui vient-il? Quelle est cette sagesse qui lui est donnée, et comment de tels miracles se font-ils par ses mains?
Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
3 N'est-ce pas le charpentier, le fils de Marie, le frère de Jacques, de Joses, de Jude et de Simon? Ses soeurs ne sont-elles pas ici parmi nous? Et il était pour eux une occasion de chute.
Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
4 Mais Jésus leur dit: Un prophète n'est méprisé que dans son pays, dans sa parenté et dans sa maison.
Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
5 Il ne put faire là aucun miracle, si ce n'est qu'il guérit un petit nombre de malades en leur imposant les mains;
Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
6 et il s'étonna de leur incrédulité. C'est ainsi qu'il parcourait, en enseignant, les villages des environs.
Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
7 Alors il appela les Douze, et il commença à les envoyer deux à deux, en leur donnant pouvoir sur les esprits impurs.
Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
8 Il leur ordonna de ne rien prendre pour la route, sauf un bâton; de n'avoir ni pain, ni sac, ni monnaie dans leur ceinture;
Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
9 de ne prendre pour chaussures que des sandales, et de ne pas emporter deux tuniques.
Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
10 Il leur disait: En quelque maison que vous entriez, demeurez-y jusqu'à ce que vous partiez.
Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
11 Et si, dans quelque endroit, on ne veut ni vous recevoir ni vous écouter, sortez de là, et secouez la poussière attachée à vos pieds, en témoignage contre les habitants.
Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
12 Étant donc partis, ils prêchèrent la repentance.
Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
13 Ils chassaient beaucoup de démons, ils oignaient d'huile beaucoup de malades, et ils les guérissaient.
Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
14 Or, le roi Hérode entendit parler de Jésus, — dont le nom était devenu célèbre. — Et il disait: Ce Jean qui baptisait est ressuscité des morts; et c'est pour cela qu'il s'opère des miracles par son moyen.
Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
15 D'autres disaient: C'est Élie; et d'autres disaient: C'est un prophète, pareil à l'un des anciens prophètes.
Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
16 Mais Hérode, l'ayant appris, disait: C'est ce Jean que j'ai fait décapiter: il est ressuscité!
Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
17 En effet, ce même Hérode avait envoyé prendre Jean; il l'avait fait enchaîner et mettre en prison, à cause d'Hérodias, femme de Philippe, son frère, parce qu'il l'avait épousée,
Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
18 et que Jean lui avait dit: Il ne t'est pas permis d'avoir la femme de ton frère.
Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
19 Aussi Hérodias était-elle remplie de haine contre Jean, et elle désirait le faire mourir. Mais elle ne le pouvait pas;
Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
20 car Hérode craignait Jean, sachant que c'était un homme juste et saint. Il veillait sur lui; il était souvent troublé après l'avoir entendu, et il l'écoutait volontiers.
chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
21 Mais il se présenta un jour favorable: Hérode donna un festin, pour l'anniversaire de sa naissance, aux grands de sa cour, à ses officiers et aux principaux de la Galilée.
Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
22 La fille même d'Hérodias, étant entrée, dansa, et elle plut à Hérode et à ses convives. Le roi dit à la jeune fille: Demande-moi ce que tu veux, et je te le donnerai.
Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
23 Il lui fit aussi ce serment: Tout ce que tu demanderas, je te le donnerai, quand ce serait la moitié de mon royaume!
Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
24 Étant sortie, elle dit à sa mère: Que demanderai-je? Celle-ci lui répondit: La tête de Jean-Baptiste.
Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
25 Aussitôt elle s'empressa de rentrer chez le roi, et elle lui fit sa demande, en disant: Je veux qu'à l'instant même, tu me donnes, sur un plat, la tête de Jean-Baptiste.
Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
26 Le roi en fut fort attristé; mais, à cause de ses serments et des convives, il ne voulut pas lui opposer un refus.
Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
27 Il envoya aussitôt l'un de ses gardes, avec l'ordre d'apporter la tête de Jean. Cet homme alla décapiter Jean dans la prison;
Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
28 il apporta la tête sur un plat, la donna à la jeune fille, et la jeune fille la donna à sa mère.
nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
29 Les disciples de Jean l'ayant appris, vinrent et emportèrent son corps; et ils le mirent dans un tombeau.
Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
30 Les apôtres se rassemblèrent auprès de Jésus, et ils lui racontèrent tout ce qu'ils avaient fait et enseigné.
Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
31 Il leur dit: Venez à l'écart, dans un lieu désert, et prenez un peu de repos. En effet, allait et venait tant de monde, qu'ils n'avaient pas même le temps de manger.
Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
32 Ils partirent donc dans la barque pour se retirer à l'écart, dans un lieu désert.
Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
33 Mais plusieurs les virent s'éloigner et les reconnurent; de toutes les villes le peuple accourut à pied là où ils se rendaient, et il y arriva avant eux.
Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
34 Alors Jésus, étant sorti de la barque, vit une grande multitude, et il fut ému de compassion pour eux, parce qu'ils étaient comme des brebis qui n'ont point de berger; puis il se mit à leur enseigner beaucoup de choses.
Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 Comme l'heure était déjà avancée, ses disciples s'approchèrent de lui et lui dirent: Ce lieu est désert, et l'heure est déjà avancée;
Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
36 renvoie-les, afin qu'ils aillent dans les campagnes et les villages des environs, pour s'acheter de quoi manger.
Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 Il leur répondit: Donnez-leur vous-mêmes à manger. Ils lui dirent! Irons-nous acheter pour deux cents deniers de pain, afin de leur donner à manger?
Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 Il leur répondit: Combien avez-vous de pains? Allez et voyez. Ils s'en assurèrent et lui dirent: Cinq pains et deux poissons.
Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 Alors il leur commanda de les faire tous asseoir, par groupes, sur l'herbe verte.
Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
40 Et ils s'assirent par rangées, par centaines et par cinquantaines.
Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
41 Jésus prit les cinq pains et les deux poissons; et, levant les yeux au ciel, il rendit grâces, rompit les pains et les donna à ses disciples pour les offrir à la foule; il leur partagea aussi les deux poissons.
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
42 Tous mangèrent et furent rassasiés;
Onse anadya ndipo anakhuta,
43 et on emporta douze paniers pleins de morceaux de pain, avec ce qui restait des poissons.
ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
44 Or, ceux qui avaient mangé étaient au nombre de cinq mille hommes.
Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
45 Aussitôt après, Jésus obligea ses disciples à entrer dans la barque et à passer avant lui sur l'autre rive, vers Beth-saïda, pendant qu'il renverrait le peuple.
Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
46 Après l'avoir renvoyé, il s'en alla sur la montagne pour prier.
Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
47 Quand le soir fut venu, la barque était au milieu de la mer, et Jésus était seul à terre.
Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
48 Et il vit qu'ils avaient beaucoup de peine à ramer, parce que le vent leur était contraire. Vers la quatrième veille de la nuit, il vint à eux, marchant sur la mer; et il voulait les devancer.
Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
49 Quand ils le virent marcher sur la mer, ils crurent que c'était un fantôme, et ils jetèrent des cris;
koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
50 car tous l'avaient vu, et ils en étaient troublés. Mais aussitôt il leur parla et leur dit: Rassurez-vous c'est moi, n'ayez point de peur!
pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
51 Alors il monta auprès d'eux dans la barque, et le vent s'apaisa. Ils furent encore plus saisis d'étonnement;
Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
52 Car ils n'avaient pas compris le miracle des pains, parce que leur cœur était endurci.
popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
53 Quand ils eurent traversé la mer, ils vinrent au pays de Génézareth, et ils abordèrent.
Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
54 Dès qu'ils furent sortis de la barque, les gens reconnurent Jésus:
Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
55 ils parcoururent toute la contrée, et ils se mirent à apporter sur leurs lits ceux qui étaient malades, partout où ils entendaient dire que Jésus se trouvait.
Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
56 Et dans tous les endroits où il arrivait, villages, villes ou campagnes, on mettait les malades sur les places publiques, et on le priait de leur permettre de toucher au moins le bord de son vêtement; et tous ceux qui le touchaient étaient guéris.
Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.