< Jean 7 >

1 Après cela, Jésus se mit à parcourir la Galilée: il ne voulait pas parcourir la Judée, parce que les Juifs cherchaient à le faire mourir.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 La fête des Juifs, appelée fête des Tabernacles, approchait.
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 Et ses frères lui dirent: Pars d'ici, et va en Judée, afin que tes disciples y voient aussi les oeuvres que tu fais.
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 On ne fait rien en secret, quand on cherche à se faire connaître. Puisque tu fais ces choses, manifeste-toi au monde.
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 En effet, ses frères eux-mêmes ne croyaient pas en lui.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 Jésus leur dit: Mon temps n'est pas encore venu; pour vous, le temps est toujours favorable.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 Le monde ne peut vous haïr; mais il me hait, parce que je rends à ce sujet ce témoignage, que ses oeuvres sont mauvaises.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 Vous, montez à cette fête; pour moi je ne monte pas à cette fête, parce que mon temps n'est pas encore accompli.
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 Après leur avoir dit cela, il demeura en Galilée.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 Lorsque ses frères furent montés à la fête, il y monta, lui aussi, mais comme en secret, et non pas publiquement.
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 Les Juifs le cherchaient donc pendant la fête, et ils disaient: Où est-il?
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 Et il y avait dans la foule une grande rumeur à son sujet. Les uns disaient: C'est un homme de bien. Et les autres disaient: Non, certes; il séduit le peuple!
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 Toutefois, personne ne parlait librement de lui, par crainte des Juifs.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 On était déjà au milieu de la fête, lorsque Jésus monta au temple et se mit à enseigner.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 Les Juifs, étonnés, disaient: Comment cet homme connaît-il les Écritures, lui qui n'a pas étudié?
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 Jésus leur répondit: Ma doctrine n'est pas de moi, mais de Celui qui m'a envoyé.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 Si quelqu'un veut faire la volonté de Dieu, il connaîtra si ma doctrine est de Dieu, ou si je parle de mon chef.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 Celui qui parle de son chef cherche sa propre gloire; mais celui qui cherche la gloire de celui qui l'a envoyé, est digne de foi, et il n'y a point d'injustice en lui.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 Moïse ne vous a-t-il pas donné la Loi? Et aucun de vous n'observe la Loi! Pourquoi cherchez-vous à me faire mourir?
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 La foule répondit: Tu es possédé d'un démon; qui donc cherche à te faire mourir?
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 Jésus reprit en disant: J'ai fait une oeuvre, et vous en êtes tous étonnés.
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 Moïse vous a donné la circoncision — qui vient, non de Moïse, lui-même, mais des patriarches, — et vous la pratiquez le jour du sabbat!
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 Si un homme reçoit la circoncision le jour du sabbat, afin que la loi de Moïse ne soit pas violée, pourquoi vous irritez-vous contre moi, parce que j'ai guéri un homme, dans son corps tout entier, le jour du sabbat?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Ne jugez pas sur l'apparence; mais jugez selon la justice.
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Quelques-uns des habitants de Jérusalem disaient: N'est-ce pas là celui qu'on cherche à faire mourir?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 Le voici qui parle librement, et on ne lui dit rien. Les chefs auraient-ils vraiment reconnu qu'il est le Christ?
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 Nous savons pourtant d'où est celui-ci; or, quand le Christ viendra, personne ne saura d'où il est.
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 Alors Jésus, enseignant dans le temple, s'écria: Vous me connaissez, et vous savez d'où je suis. Je ne suis pas venu de moi-même, mais Celui qui m'a envoyé est véritable, et vous ne le connaissez pas.
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 Moi, je le connais; car je viens de lui, et c'est lui qui m'a envoyé.
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 Ils cherchaient donc à l'arrêter; cependant personne ne mit la main sur lui, parce que son heure n'était pas encore venue.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 Parmi le peuple, il y en eut beaucoup qui crurent en Jésus, et ils disaient: Quand le Christ viendra, fera-t-il plus de miracles que n'en fait celui-ci?
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 Les pharisiens entendirent les propos que la foule tenait à son sujet; et, de concert avec eux, les principaux sacrificateurs envoyèrent des agents pour s'emparer de lui.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 Jésus dit alors: Je suis encore avec vous pour un peu de temps; puis, je m'en vais à Celui qui m'a envoyé.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 Vous me chercherez et vous ne me trouverez pas, et là où je suis, vous ne pouvez venir.
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 Les Juifs se dirent entre eux: Où doit-il donc aller, que nous ne le trouverons pas? Doit-il aller vers ceux qui sont dispersés parmi les Grecs et enseigner les Grecs?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 Que signifie ce qu'il a dit: Vous me chercherez, et vous ne me trouverez pas, et là où je suis, vous ne pouvez venir?
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 Le dernier, le grand jour de la fête, Jésus était là, debout, et il s'écria: Si quelqu'un a soif, qu'il vienne à moi, et qu'il boive.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 Celui qui croit en moi, des fleuves d'eau vive, comme l'a dit l'Écriture, couleront de son sein.
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 Il disait cela de l'Esprit que devaient recevoir ceux qui croiraient en lui; car l'Esprit n'avait pas encore été donné, parce que Jésus n'était pas encore glorifié.
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 Plusieurs, parmi la foule, ayant entendu ces paroles, disaient: Celui-ci est véritablement le prophète.
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 D'autres disaient: C'est le Christ. D'autres encore: Le Christ viendra-t-il de la Galilée?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 L'Écriture ne dit-elle pas que c'est de la famille de David et du village de Bethléhem, d'où était David, que le Christ doit sortir?
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 Le peuple était donc divisé à son sujet.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 Et quelques-uns d'entre eux voulaient l'arrêter; mais personne ne mit la main sur lui.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 Les agents retournèrent donc vers les principaux sacrificateurs et les pharisiens; et ceux-ci leur dirent: Pourquoi ne l'avez-vous pas amené?
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 Les agents répondirent: Jamais homme n'a parlé comme cet homme!
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 Les pharisiens leur dirent: Avez-vous été séduits, vous aussi?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Y a-t-il un seul des chefs ou des pharisiens qui ait cru en lui?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 Mais cette populace, qui ne connaît point la Loi, est exécrable!
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 Nicodème — celui qui était venu précédemment trouver Jésus et qui était l'un d'entre eux — leur dit:
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 Notre Loi juge-t-elle un homme sans qu'on l'ait entendu d'abord, et sans qu'on ait pris connaissance de ce qu'il a fait?
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 Ils lui répondirent: Es-tu Galiléen, toi aussi? Informe-toi, et tu verras qu'il ne sort pas de prophète de la Galilée.
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
53 [Chacun se retira dans sa maison.]
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.

< Jean 7 >