< Éphésiens 1 >
1 Paul, apôtre de Jésus-Christ par la volonté de Dieu, aux saints qui sont à Éphèse, aux fidèles en Jésus-Christ.
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu. Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:
2 Que la grâce et la paix vous soient données de la part de Dieu, notre Père, et du Seigneur Jésus-Christ.
Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
3 Béni soit Dieu, le Père de notre Seigneur Jésus-Christ, qui nous a comblés en Christ de toutes sortes de bénédictions spirituelles dans les lieux célestes,
Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu.
4 nous qu'il a élus en lui, avant la création du monde, pour que nous soyons saints et irrépréhensibles devant Dieu,
Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,
5 nous ayant prédestinés, dans son amour, à devenir ses enfants d'adoption par Jésus-Christ, selon le bon plaisir de sa volonté,
Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.
6 à la louange de la grâce magnifique qu'il nous a gratuitement accordée en son Fils bien-aimé!
Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.
7 C'est en lui que nous avons la rédemption par son rang, la rémission des péchés, selon les richesses de sa grâce
Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu
8 que Dieu a répandue abondamment sur nous, avec toute sorte de sagesse et d'intelligence,
chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso,
9 en nous faisant connaître le mystère de sa volonté, suivant le dessein que, dans sa bienveillance, il avait d'avance formé en lui-même, —
Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake.
10 pour en assurer l'exécution, quand les temps seraient accomplis, — de réunir toutes choses en Christ, aussi bien celles qui sont dans les cieux que celles qui sont sur la terre.
Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
11 C'est en lui aussi que nous avons été rendus participants de l'héritage, comme nous y avions été prédestinés, suivant le dessein de Celui qui opère toutes choses conformément à la décision de sa volonté,
Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake,
12 afin que nous servions à célébrer sa gloire, nous qui avons, les premiers, espéré en Christ.
nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake.
13 C'est en lui que vous aussi, après avoir entendu la parole de la vérité, l'Évangile de votre salut, — c'est en lui que vous avez cru et que vous avez été scellés du Saint-Esprit qui avait été promis,
Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza.
14 lequel est un gage de notre héritage, jusqu'à la rédemption de ceux qu'il s'est acquis pour célébrer sa gloire.
Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
15 C'est pourquoi, ayant entendu parler, moi aussi, de votre foi au Seigneur Jésus et de votre charité envers tous les saints,
Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse,
16 je ne cesse de rendre grâces pour vous, faisant mention de vous dans mes prières.
ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.
17 Je prie le Dieu de notre Seigneur Jésus-Christ, le Père de gloire, de vous accorder un esprit de sagesse et de révélation qui vous apprenne à le connaître,
Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
18 et d'illuminer les yeux de votre coeur afin que vous sachiez quelle est l'espérance que fait naître en nous son appel, quelles sont, pour les saints, les richesses de son glorieux héritage,
Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
19 et quelle est, envers nous qui croyons, l'infinie grandeur de sa puissance qui agit par la vertu souveraine de sa force.
Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
20 C'est cette puissance qu'il a déployée dans le Christ, en le ressuscitant des morts et en le faisant asseoir à sa droite dans les lieux célestes,
imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba.
21 au-dessus de tout pouvoir, de toute autorité, de toute puissance, de toute souveraineté, de tout nom qui puisse être nommé, non seulement dans ce siècle, mais aussi dans celui qui est à venir. (aiōn )
Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn )
22 Il a mis toutes choses sous ses pieds, et il l'a donné pour chef suprême à l'Église,
Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo,
23 qui est son corps, la plénitude de Celui qui remplit tout en tous.
umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.