< Psaumes 3 >
1 Cantique de David, quand il fuyait devant Absalon, son fils. O Éternel, que mes ennemis sont nombreux! en nombre ils se lèvent contre moi!
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 Leur foule dit de moi: « Il n'est par-devers Dieu point de salut pour lui. (Pause)
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 Mais tu es, ô Éternel, le bouclier qui me couvre, tu es ma gloire, c'est toi qui tiens ma tête levée.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 De ma voix j'invoque l'Éternel, et Il me répond de sa montagne sainte. (Pause)
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 Je me couche, et je m'endors; je m'éveille, car l'Éternel est mon soutien.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 Je suis sans peur devant des milliers d'hommes contre moi campés de toute part.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Sus! Éternel! sauve-moi, mon Dieu! car tu romps la mâchoire à tous mes ennemis, et tu brises les dents des impies.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 Le salut vient de l'Éternel! Que ta bénédiction soit sur ton peuple! (Pause)
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)