< Psaumes 125 >

1 Cantique graduel. Ceux qui se confient dans l'Éternel, sont comme la montagne de Sion, elle est inébranlable et stable éternellement.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 Des montagnes entourent Jérusalem: ainsi l'Éternel entoure son peuple dès maintenant à jamais.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Car le sceptre de l'impie ne restera pas sur le lot des justes, afin que les justes ne portent pas leurs mains au mal.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Éternel, fais du bien aux hommes de bien, et à ceux qui sont droits en leurs cœurs!
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 Pour ceux qui dévient et prennent des voies tortueuses, que l'Éternel les perde avec les artisans du crime! Paix soit à Israël!
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.

< Psaumes 125 >