< Lévitique 11 >
1 Et l'Éternel parla à Moïse et Aaron et leur dit:
Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
2 Parlez aux enfants d'Israël en ces termes: Voici les animaux que vous pouvez manger parmi toutes les bêtes qui sont sur la terre.
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
3 Tout animal ayant le pied fourché et la corne fendue de part en part et qui rumine, vous servira d'aliment;
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
4 parmi ceux qui ruminent et ont le pied fourché, voici seulement ceux dont vous vous abstiendrez, le chameau, car il rumine, mais n'a pas la corne fendue de part en part; vous le tiendrez pour impur;
“‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
5 et la gerboise, car elle rumine, mais n'a pas de corne fendue de part en part; vous la tiendrez pour impure;
Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
6 et le lièvre, car il rumine, mais n'a pas de corne fendue de part en part; vous le tiendrez pour impur;
Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
7 et le porc, car il a bien le pied fourché et une corne fendue de part en part, mais il ne rumine pas; vous le tiendrez pour impur.
Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
8 Vous ne mangerez pas de leur chair, ni ne toucherez leurs corps morts; vous les tiendrez pour impurs.
Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
9 Parmi les animaux qui sont dans les eaux, ceux que vous pouvez manger sont tous ceux qui portent nageoires et écailles dans les eaux, les mers, les rivières, ils vous serviront d'aliments;
“‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 mais tous ceux qui ne portent pas nageoires et écailles dans les mers et les rivières parmi tous ceux qui fourmillent dans les eaux et les êtres qui vivent dans les eaux, seront pour vous une souillure.
Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
11 Ils seront pour vous une souillure; vous ne mangerez point de leur chair, vous regarderez leur corps mort comme immonde.
Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
12 Tout ce qui dans les eaux ne porte pas nageoires et écailles sera pour vous immonde.
Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
13 Et parmi les oiseaux voici ceux que vous regarderez comme immondes, qui ne se mangeront pas, qui seront pour vous une souillure, l'aigle et l'orfraie et l'aigle de mer,
“‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
14 et le faucon et l'espèce de l'émerillon,
nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
15 toutes les espèces de corbeaux,
akhungubwi a mitundu yonse,
16 et l'autruche femelle et l'autruche mâle et la mouette, et l'espèce du vautour
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
17 et le hibou et le pélican sauteur et l'ibis,
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
18 et le cygne et le pélican et le percnoptère
tsekwe, vuwo, dembo,
19 et la cigogne et l'espèce du perroquet et la huppe et la chauve-souris.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
20 Vous regarderez comme immonde tout insecte ailé marchant sur quatre pieds.
“‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
21 Les seuls insectes ailés marchant sur quatre pieds qui vous serviront d'aliments sont ceux qui ont les pieds surmontés de jambes pour sauter sur la terre.
Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
22 Ceux de cette famille que vous mangerez, sont l'espèce de l'arbeh, l'espèce du solam, et l'espèce du hargal, et l'espèce du hagab.
Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
23 Mais tous les autres insectes ailés à quatre pieds seront immondes pour vous; ils vous rendront impurs,
Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
24 quiconque aura touché leurs corps morts, sera jusqu'au soir en état d'impureté,
“‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
25 et quiconque aura porté de leurs corps morts, lavera ses habits et sera jusqu'au soir en état d'impureté.
Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
26 Vous tiendrez pour immonde tout animal qui a le pied fourché, mais n'a pas une corne fendue de part en part et ne rumine pas; quiconque le touchera sera en état d'impureté.
“‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
27 Et tout ce qui marche sur ses pattes et tous les animaux qui marchent sur quatre pieds, vous les tiendrez pour immondes,
Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
28 et quiconque touchera leurs corps morts sera jusqu'au soir en état d'impureté. Et celui qui portera leurs corps morts, lavera ses habits et sera jusqu'au soir en état d'impureté; vous les regarderez comme immondes.
Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
29 Et parmi les menus animaux qui frétillent sur la terre, vous tiendrez pour impurs les taupes, les souris et les lézards selon leur espèce,
“‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
30 et l'Anaka et le Coch, et la Letaa et le colimaçon et le caméléon.
gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
31 Tenez-les pour impurs parmi tous ceux qui frétillent; quiconque les touchera morts, sera jusqu'au soir en état d'impureté.
Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
32 Et tout objet sur lequel tombera un de ces animaux morts sera souillé, meuble quelconque de bois, ou vêtements, ou cuir, ou sac, tout ustensile servant à un usage quelconque; il sera mis dans l'eau et restera souillé jusqu'au soir, après quoi il se retrouvera pur.
Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
33 Et tout vase de terre dans lequel il en tombera sera souillé avec tout son contenu, et vous briserez le vase.
Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
34 Et tout comestible sur lequel il tombera de cette eau sera souillé, et toute liqueur à boire contenue dans ce vase sera souillée.
Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
35 Et tout objet sur lequel il tombera quelque chose de leurs corps morts, sera souillé, fourneau et foyer seront mis en pièces, comme souillés, et vous devez les regarder comme immondes.
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
36 Les sources, les citernes et les réservoirs d'eau seuls n'en contracteront point de souillure. Mais quiconque touchera leur corps mort, tombera en état d'impureté.
Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
37 S'il tombe quelque chose de leur corps mort sur une semence quelconque qui doit être semée, elle ne cessera pas d'être pure;
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
38 mais si l'on a humecté cette semence et qu'il y tombe quelque chose de leurs corps morts, tenez-la pour souillée.
Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
39 Et si l'un des animaux qui vous servent d'aliment, périt, celui qui touchera son corps mort sera jusqu'au soir en état d'impureté.
“‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
40 Et celui qui mangera de son corps mort lavera ses habits et sera jusqu'au soir en état d'impureté; et celui qui portera son corps mort lavera ses habits et sera jusqu'au soir en état d'impureté.
Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
41 Et tout reptile rampant sur la terre sera pour vous un animal immonde dont vous ne ferez pas un aliment.
“‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
42 En fait de reptiles rampant sur la terre, tous ceux qui se traînent sur le ventre et tous ceux qui marchent sur quatre pieds ou plus, quel qu'en soit le nombre, ne vous serviront point d'aliment: ce sont des souillures.
Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
43 Ne souillez vos personnes par aucun reptile qui se traîne, et ne vous exposez pas à leur contact immonde pour tomber par là dans l'état d'impureté.
Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
44 Car je suis l'Éternel, votre Dieu, et vous devez vous sanctifier et être saints, car je suis Saint, et éviter de souiller vos personnes par aucun des reptiles qui se traînent sur la terre.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
45 Car je suis l'Éternel qui vous ai retirés du pays d'Egypte, pour être votre Dieu: Soyez donc saints, car je suis Saint.
Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
46 Telle est la loi qui parmi les bestiaux et les oiseaux et tous les êtres vivants qui se meuvent dans les eaux, et tous les êtres vivants qui rampent sur la terre,
“‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
47 vous apprendra à discerner ce qui est pur ou impur, l'animal qui se mange et celui qui ne se mange pas.
Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”