< Juges 16 >

1 Et Samson étant allé à Gaza, y vit une courtisane, et il entra chez elle.
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
2 On dit aux Gazites: Samson est arrivé ici! Et ils firent des rondes, et toute la nuit ils le guettèrent à la porte de la ville, et ils ne firent point de bruit de toute la nuit et ils disaient: Attendons l'aube du matin; alors nous le tuerons.
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
3 Et Samson fut couché jusqu'à minuit; et vers minuit il se leva, et il saisit les deux battants de la porte de la ville et les deux jambages, et les arracha avec la barre, et les chargea sur ses épaules et les porta sur le sommet de la montagne qui est vis-à-vis d'Hébron.
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
4 Et il arriva ensuite qu'il aima une femme dans la vallée de Sorek, et elle se nommait Delila.
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
5 Alors les princes des Philistins allèrent chez elle et lui dirent: Flatte-le et observe où gît sa grande force, et par où nous pourrions le maîtriser pour le garrotter et le dompter; et nous, nous te donnerons chacun mille et cent sicles d'argent.
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
6 Alors Delila dit à Samson: Révèle-moi donc où gît ta grande force, et de quoi il faudrait te lier pour te dompter!
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
7 Et Samson lui dit: Qu'on me lie de sept cordes encore humides, non séchées, et je deviens débile et tel qu'un autre homme.
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
8 Alors les princes des Philistins firent porter chez elle sept cordes encore humides, non séchées; et elle l'en garrotta.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
9 Or des gens se tenaient chez elle embusqués dans une chambre. Et elle lui dit: Les Philistins contre toi, Samson! Alors il cassa les cordes comme l'on casse un cordon de chanvre, quand il sent le feu. Et l'on ne connut pas le secret de sa force.
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
10 Alors Delila dit à Samson: Voici, tu m'as abusée, et tu m'as fait un mensonge. A présent indique-moi donc avec quoi il faut te lier.
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
11 Et il lui dit: Qu'on me lie de cordes neuves qui n'aient servi à aucun travail, et je deviens débile et tel qu'un autre homme.
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
12 Alors Delila prit des cordes neuves et l'en lia; puis elle lui dit: Les Philistins contre toi, Samson! Or des gens se tenaient embusqués dans une chambre. Et il dégagea ses bras en cassant les cordes comme un fil.
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
13 Alors Delila dit à Samson: Jusqu'ici tu m'as abusée et tu m'as dit des mensonges! Indique-moi avec quoi il faut te lier. Et il lui dit: Si avec des fils tu tisses en natte les sept tresses de ma tête.
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
14 Et avec un clou elle les fixa [à la paroi] et elle lui dit: Les Philistins contre toi, Samson! Et il se réveilla de son sommeil, et rompit le clou qui fixait la natte, et les fils.
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
15 Alors elle lui dit: Comment peux-tu dire: Je t'aime! tandis que ton cœur n'est pas avec moi? Voici trois fois que tu m'abuses sans me révéler où gît ta grande force.
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
16 Et comme tous les jours elle l'importunait par ses discours et par son insistance, son âme ennuyée à la mort perdit patience;
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17 alors il lui ouvrit tout son cœur et lui dit: Jamais rasoir ne passa sur ma tête, parce que dès le sein de ma mère je suis consacré à Dieu; si j'étais rasé, ma force s'en irait, et je deviendrais débile et tel que tous les hommes.
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
18 Et Delila, voyant qu'il lui avait ouvert tout son cœur, envoya un message aux princes des Philistins pour les mander et leur dire: Cette fois venez, car il m'a ouvert tout son cœur. Et les princes des Philistins arrivèrent chez elle et apportèrent l'argent dans leurs mains.
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
19 Et elle l'endormit sur ses genoux et fit venir un homme, et elle fit raser les sept tresses de sa tête, et commença ainsi à le dompter, et sa force disparut.
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
20 Et elle dit: Les Philistins contre toi, Samson! Et il se réveilla de son sommeil; et il se disait: Je m'en tirerai cette fois comme l'autre fois et je me dégagerai. Or il ne se doutait pas que l'Éternel s'était retiré de lui.
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
21 Alors les Philistins le saisirent et lui crevèrent les yeux, et le menèrent à Gaza, et le lièrent d'une double chaîne d'airain, et il fut réduit à moudre dans la prison.
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
22 Cependant sa chevelure commençait à croître depuis qu'elle avait été rasée.
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
23 Or les princes des Philistins se réunirent pour immoler un grand sacrifice à Dagon, leur dieu, et pour se réjouir. Et ils dirent: Notre Dieu a fait tomber entre nos mains Samson, notre ennemi.
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24 Et quand le peuple le vit, ils louèrent leur dieu; car ils disaient: Notre Dieu a fait tomber entre nos mains notre ennemi, et le dévastateur de notre pays, et le meurtrier d'un grand nombre des nôtres.
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
25 Et comme ils étaient en belle humeur, ils dirent: Faites venir Samson pour nous divertir. Et ils firent venir Samson de la prison, et il fit des bouffonneries devant eux et ils le placèrent entre les colonnes.
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26 Et Samson dit au valet qui lui tenait la main: Laisse-moi tâter les colonnes sur lesquelles pose l'édifice, je voudrais m'y appuyer.
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
27 Or l'édifice était rempli d'hommes et de femmes, et tous les princes des Philistins s'y trouvaient; et sur le toit il y avait environ trois mille hommes et femmes regardant Samson faire des bouffonneries.
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
28 Alors Samson invoqua l'Éternel et dit: Seigneur, Éternel! oh! souviens-toi de moi, et prête-moi force pour cette fois seulement, ô Dieu, afin que je tire des Philistins une vengeance unique pour la perte de mes deux yeux.
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
29 Et Samson fit pencher les deux colonnes médiales sur lesquelles posait l'édifice, en s'y appuyant, à l'une de la main droite, à l'autre de la gauche.
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30 Et Samson dit: Que je périsse avec les Philistins! Et il les renversa avec force, et l'édifice croula sur les princes et sur tout le peuple présent, et les morts qu'il fit mourir lors de sa mort, furent plus nombreux que ceux qu'il avait fait mourir de son vivant.
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
31 Et ses frères avec toute la maison de son père vinrent pour l'enlever; et ils le transportèrent et lui donnèrent la sépulture entre Tsorea et Esthaol dans le tombeau de Manoah, son père. Or il jugea Israël pendant vingt ans.
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

< Juges 16 >