< Jonas 1 >

1 Et: la parole de l'Éternel fut adressée à Jonas, fils d'Amitthaï, en ces mots:
Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
2 Lève-toi, va à Ninive la grande ville, et prêche-lui, car sa méchanceté est parvenue jusqu'à moi.
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
3 Mais Jonas se leva pour s'enfuir à Tarsis de devant la face de l'Éternel. Et il descendit à Joppe, et il trouva un navire partant pour Tarsis, et il paya son naulage, et s'embarqua pour aller avec eux à Tarsis, loin de la face de l'Éternel.
Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
4 Mais l'Éternel envoya un grand vent sur la mer, et il s'éleva une grande tempête sur la mer, et le navire risquait de naufrager.
Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
5 Alors les mariniers eurent peur, et ils invoquèrent chacun leur dieu, et ils jetèrent l'attirail qui était sur le vaisseau à la mer, pour l'alléger. Mais Jonas était descendu dans l'intérieur du vaisseau, et s'étant couché il s'était endormi
Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
6 Alors le maître du vaisseau s'approcha, de lui et lui dit: Que fais-tu de dormir? lève-toi! invoque ton Dieu! peut-être Dieu se ressouviendra de nous, et nous ne périrons pas.
Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
7 Et ils se dirent l'un à l'autre: Venez et tirons au sort pour connaître lequel nous attire ce malheur! Et ils tirèrent au sort, et le sort désigna Jonas.
Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
8 Alors ils lui dirent: Dis-nous qui nous attire ce malheur? Quelles sont tes affaires et d'où viens-tu? quel est ton pays et de quelle nation es-tu?
Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
9 Et il leur dit: Je suis hébreu, et c'est l'Éternel, le Dieu des Cieux, que j'adore, Celui qui a fait la mer et la terre ferme.
Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
10 Et ces hommes furent saisis d'une grande crainte, et ils lui dirent: Pourquoi as-tu fait cela? Car ces hommes savaient qu'il fuyait de devant la face de l'Éternel, parce qu'il le leur avait avoué.
Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
11 Et ils lui dirent: Que te ferons-nous pour que la mer se calme envers nous? Car la mer devenait toujours plus orageuse.
Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
12 Et il leur dit: Prenez-moi, et jetez-moi à la mer, et la mer se calmera envers vous; car je sais que c'est moi qui vous attire cette grande tempête.
Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
13 Et ces hommes ramèrent pour revenir à terre; mais ils ne pouvaient, car la mer allait s'agitant toujours plus contre eux.
Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
14 Alors ils invoquèrent l'Éternel et dirent: Éternel, oh! ne nous fais pas: périr à cause de l'âme de cet homme, et ne nous charge pas du sang innocent; car tu es l'Éternel; ce que tu trouves bon, tu le fais.
Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
15 Et ils prirent Jonas et le jetèrent à la mer, et la mer cessa d'être furieuse.
Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
16 Et ces hommes furent saisis d'une grande crainte envers l'Éternel, et ils sacrifièrent à l'Éternel des victimes, et ils vouèrent des vœux.
Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
17 Et l'Éternel envoya un grand poisson pour engloutir Jonas, et Jonas fut dans le corps du poisson trois jours et trois nuits.
Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.

< Jonas 1 >