< Job 31 >
1 J'avais fait un pacte avec mes yeux… Comment les eussé-je arrêtés sur une vierge?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 Et quel sort d'en haut Dieu m'eût-il envoyé, et quel lot le Tout-puissant, des lieux suprêmes?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 La ruine n'est-elle pas pour le criminel, et le malheur pour ceux qui font le mal?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Ne découvre-t-Il pas mes voies, et ne compte-t-Il pas tous mes pas?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 Ai-je eu commerce avec le mensonge, et mon pied fut-il prompt à supplanter?
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 Que Dieu me pèse à la juste balance, et Il reconnaîtra mon innocence!
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 Mes pas ont-ils dévié de la voie, et mon cœur suivit-il l'attrait de mes yeux? Une seule tache est-elle empreinte sur ma main?
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Alors, que je sème, et qu'un autre moissonne, et que mes rejetons soient extirpés!
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 Mon cœur pour une femme s'est-il laissé séduire? ai-je été aux aguets à la porte de mon prochain?
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Alors, que ma femme tourne la meule pour un autre, et que d'autres abusent d'elle!
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 Car c'est là un crime, un forfait que les juges doivent punir;
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 oui, c'est un feu qui consume, à détruire, et aurait dans sa racine ruiné tout mon avoir.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 Ai-je méprisé les droits de mon esclave, et de ma servante, quand ils n'étaient pas d'accord avec moi?
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 Mais que ferais-je, si Dieu se levait? et, s'il me châtiait, que lui répliquerais-je?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Dans le sein maternel, Celui qui me forma, ne le forma-t-Il pas aussi? et ne nous prépara-t-Il pas dans le sein d'une mère?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 Ai-je rebuté le vœu du pauvre, et fait languir les yeux de la veuve?
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 Ai-je mangé mon pain seul, et l'orphelin n'y eut-il point de part?
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 Non, dès ma jeunesse, j'élevai l'un en père, et dès ma naissance je fus le guide de l'autre.
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 Ai-je pu voir l'indigent non vêtu, et le pauvre non couvert?
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 Leurs reins ne me bénissaient-ils pas, et la toison de mes agneaux ne les réchauffait-elle pas?
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 Ma main a-t-elle menacé l'orphelin, parce que je me voyais soutenu à la Porte?
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 Alors, que mon épaule se détache de ma nuque, et que mon bras brisé sorte de son emboîture!
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Mais les vengeances de Dieu sont ma terreur, et devant Sa majesté je deviens impuissant.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 Ai-je pris l'or pour mon appui, et ai-je dit au métal: En toi je me confie?
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 Me suis-je applaudi de la grandeur de mes biens, et des grands gains obtenus par mes mains?
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 Ai-je regardé la lumière, quand elle resplendit, et la lune, quand magnifique elle s'avance?
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 Et mon cœur en secret s'est-il laissé séduire, jusqu'à confier à ma main les baisers de ma bouche?
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 Cela aussi serait un crime que les juges doivent punir, parce que j'aurais menti au Dieu suprême.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 Étais-je joyeux de la ruine de mon ennemi, transporté de le voir atteint par les revers?
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Mais je ne permettais pas à ma langue de pécher en demandant sa mort dans une imprécation.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 Les gens de ma tente ne disaient-ils pas: Montrez-nous qui ne fut pas rassasié à sa table?
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 L'étranger ne passait pas la nuit dehors, et j'ouvrais ma porte au voyageur.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 A l'exemple des hommes ai-je dissimulé mes fautes, enfouissant dans mon sein mes égarements,
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 parce que je redoutais le peuple assemblé, et que le mépris des tribus me faisait peur à m'ôter la parole, et à m'empêcher de passer ma porte?
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Ah! s'il voulait m'écouter et me dire: Voici ma signature! Si le Tout-puissant voulait répliquer! si j'avais le grief écrit par ma partie!
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Oui, je le porterais sur mon épaule, je le ceindrais comme un diadème,
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 j'avouerais chacun de mes pas, comme un prince je L'aborderais. –
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 Mon champ réclame-t-il contre moi, et ses sillons en même temps portent-ils plainte?
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 En ai-je mangé le produit, sans l'avoir payé, et ai-je arraché des soupirs à son maître?
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Alors, que la ronce germe au lieu du froment, et l'herbe gourmande à la place de l'orge! Fin des discours de Job.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.