< Isaïe 4 >
1 Et sept femmes viendront en ce jour saisir un même homme, et lui diront: « Nous voulons manger notre pain et nous vêtir de nos habits; seulement, que nous portions ton nom! fais cesser notre opprobre! »
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 En ce jour-là, le Germe de l'Éternel sera l'ornement et la gloire, et le fruit de la terre sera l'orgueil et la parure des restes échappés d'Israël.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 Et quiconque sera laissé en Sion et survivra dans Jérusalem, portera le nom de Saint, quiconque sera inscrit au livre des vivants en Jérusalem;
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 quand le Seigneur aura lavé les ordures des filles de Sion, et fait disparaître le sang de Jérusalem de son sein, par l'Esprit de jugement et par l'Esprit d'extermination.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 Et sur toute l'étendue de la montagne de Sion, et sur ses lieux d'assemblées, l'Éternel établira pendant le jour un nuage et une fumée, et de nuit l'éclat d'un feu allumé; car toute magnificence est mise à couvert;
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 et il y aura un abri pour donner de l'ombrage pendant le jour contre la chaleur, et pour être un refuge et une retraite contre l'orage et la pluie.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.