< Genèse 9 >

1 Alors Dieu bénit Noé et ses fils, et leur dit: Soyez féconds et vous multipliez et remplissez la terre.
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
2 Et soyez craints et redoutés de tous les animaux de la terre et de tous les oiseaux des cieux, de tout ce qui rampe sur le sol et de tous les poissons de la mer: ils sont mis dans vos mains.
Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
3 Tout ce qui se meut ayant vie, vous servira d'aliment; aussi bien que la verdure des plantes, je vous donne tout.
Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
4 Ce n'est que la chair dans son âme, son sang, que vous ne mangerez point.
“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
5 Et c'est votre sang seul qu'en faveur de votre vie je redemanderai; je le redemanderai à tous les animaux, et je redemanderai la vie de l'homme à l'homme, à son frère, quel qu'il soit.
Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
6 Quiconque versera le sang de l'homme, par l'homme son sang sera versé, car Dieu a fait l'homme à son image.
“Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
7 Pour vous, soyez féconds et vous multipliez, et pullulez sur la terre et vous y multipliez.
Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
8 Et Dieu dit à Noé et à ses fils avec lui:
Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
9 Pour moi, voici, j'érige mon alliance avec vous et avec votre race après vous,
“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
10 et avec tous les êtres vivants qui sont à vos côtés, oiseaux, bétail et toute bête de la terre qui est à vos côtés, tous ceux qui sont sortis de l'arche avec vous, de tous les animaux de la terre.
pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
11 J'érige donc mon alliance avec vous à cet effet que dorénavant toute chair ne sera point exterminée par les eaux du déluge et que dorénavant il n'y aura plus de déluge pour détruire la terre.
Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
12 Et Dieu dit: Voici le signe de l'alliance que j'institue entre moi et vous et tous les êtres vivants qui sont à vos côtés, pour la suite des âges à jamais:
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
13 je place mon arc dans la nuée pour qu'il devienne un signe d'alliance entre moi et la terre.
Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
14 Et lorsque je ferai surgir les nuées sur la terre, et que mon arc apparaîtra dans la nuée,
Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
15 alors je me rappellerai l'alliance qui existe entre moi et vous et tous les êtres vivant en toute chair, et [qui stipule] que les eaux ne deviendront plus un déluge pour détruire toute chair.
ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
16 Et l'arc étant dans la nuée, je le regarderai pour me rappeler l'alliance éternelle qui existe entre Dieu et tout être vivant en toute chair qui se trouve sur la terre.
Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
17 Et Dieu dit à Noé: Tel est le signe de l'alliance que j'érige entre moi et toute chair qui se trouve sur la terre.
Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
18 Et les fils de Noé qui sortirent de l'arche étaient Sem, Cham et Japheth; or Cham était le père de Canaan.
Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
19 Ce sont là les trois fils de Noé, et c'est d'eux qu'est issue la population répandue sur toute la terre.
Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
20 Et Noé commença à être agriculteur et il planta de la vigne.
Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
21 Et il but du vin, et il se trouva ivre et il se découvrit au milieu de sa tente.
Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
22 Et Cham, père de Canaan, vit la nudité de son père, et le redit à ses deux frères dehors.
Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
23 Alors Sem et Japheth prirent le manteau et le mirent les deux sur leurs épaules, et marchèrent à reculons et couvrirent la nudité de leur père; mais leur visage était tourné, et ils ne virent point la nudité de leur père.
Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
24 Et lorsque Noé se réveilla de son ivresse, il apprit ce que lui avait fait son fils cadet;
Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
25 alors il dit: Maudit soit Canaan, Serviteur des serviteurs qu'il soit pour ses frères!
anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
26 Puis il dit: Béni soit l'Éternel, Dieu de Sem, et que Canaan soit son serviteur!
Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
27 Que Dieu donne de l'extension à Japheth, et qu'il habite dans les tentes de Sem, et que Canaan devienne leur serviteur!
Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
28 Et après le déluge Noé vécut trois cent cinquante ans;
Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
29 et la totalité des jours de Noé fut neuf cent cinquante ans, puis il mourut.
Anamwalira ali ndi zaka 950.

< Genèse 9 >