< Ézéchiel 45 >
1 Et quand vous partagerez au sort le pays par héritages, vous prélèverez sur le pays pour l'Éternel une portion qui sera sainte, et qui aura en longueur vingt-cinq mille [perches] et en largeur dix mille; elle sera sainte dans toute son étendue.
“‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
2 De ce nombre il sera pris pour le sanctuaire cinq cents sur cinq cents en carré, et on y ajoutera tout autour un espace libre de cinquante coudées.
Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
3 Et sur cette mesure tu mesureras en longueur vingt-cinq mille et en largeur dix mille, et ce sera le sanctuaire, le lieu très saint.
Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
4 C'est la portion sainte du pays: elle appartiendra aux prêtres, serviteurs du sanctuaire, qui s'approchent pour servir l'Éternel; et ce sera l'emplacement pour leurs maisons, et un sanctuaire pour le sanctuaire.
Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
5 Et vingt-cinq mille [perches] en longueur et dix mille en largeur appartiendront en propriété aux lévites, serviteurs de la maison, avec vingt chambres.
Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
6 Et vous donnerez en propriété à la ville cinq mille en largeur, et vingt-cinq mille en longueur, parallèlement à la portion sainte; cela appartiendra à toute la maison d'Israël.
“‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
7 Et au prince vous donnerez en deçà et en delà de la portion sainte et de la propriété de la ville, le long de la portion sainte et le long de la propriété de la ville, au côté de l'occident vers l'occident, et au côté de l'orient vers l'orient, la longueur d'une portion de tribu, depuis la limite de l'occident jusqu'à la limite de l'orient.
“‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
8 Ce sera son domaine, sa propriété en Israël, afin que mes princes n'oppriment plus mon peuple, mais laissent le pays à la maison d'Israël selon ses tribus.
Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
9 Ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: C'est assez, princes d'Israël! renoncez à la violence et à l'oppression, faites droit et justice, et délivrez mon peuple de vos exactions, dit le Seigneur, l'Éternel.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
10 Ayez une balance juste, un épha juste, et un bath juste.
Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
11 L'épha et le bath seront une seule et même mesure, de sorte que le bath contiendra la dixième partie du homer, et l'épha la dixième partie du homer; la mesure en sera réglée d'après le homer.
Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
12 Et le sicle sera de vingt géras. Vingt sicles, vingt-cinq sicles, quinze sicles formeront chez vous la mine.
Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
13 Voici la part que vous, prélèverez [pour le prince]: la sixième partie de l'épha sur un homer de froment, et la sixième partie de l'épha sur un homer d'orge.
“‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
14 La redevance sur l'huile, sur le bath d'huile, est d'un dixième de bath sur le cor, à dix baths pour un homer, car dix baths font un homer.
Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
15 Et une brebis du troupeau, prise sur deux cents dans les pâturages bien arrosés d'Israël, sera l'offrande, et l'holocauste, et le sacrifice d'actions de grâces, et leur expiation, dit le Seigneur, l'Éternel.
Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Tout le peuple du pays sera tenu à cette offrande envers le prince d'Israël.
Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
17 Et le prince sera chargé des holocaustes, des offrandes et des libations aux fêtes, et aux nouvelles lunes, et aux jours de sabbat, à toutes les solennités de la maison d'Israël: il offrira la victime pour le péché, et l'offrande, et l'holocauste, et le sacrifice d'actions de grâces, pour faire l'expiation en faveur de la maison d'Israël.
Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
18 Ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Au premier mois, le premier jour du mois, tu prendras un jeune taureau sans défaut, afin de faire l'expiation pour le sanctuaire.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
19 Et le sacrificateur prendra du sang de la victime pour le péché, et en mettra aux jambages de la maison, et aux quatre angles de la partie rentrante de l'autel, et aux jambages de la porte du parvis intérieur.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
20 Et tu en feras autant le septième jour du mois, à cause de ceux qui auront péché par méprise ou par ignorance: et c'est ainsi que vous ferez l'expiation pour la maison.
Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
21 Le premier mois, le quatorzième jour du mois, vous célébrerez la Pâque, la fête des sept jours; vous mangerez des pains sans levain.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
22 Et ce jour-là, le prince offrira pour lui et pour tout le peuple du pays un taureau en sacrifice pour le péché.
Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
23 Et durant les sept jours de la fête il offrira à l'Éternel un holocauste, sept taureaux et sept béliers sans défaut, chacun des sept jours, et une victime pour le péché, un bouc, chaque jour.
Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
24 Et pour offrande il présentera un épha pour chaque taureau et un épha pour chaque bélier, et un hin d'huile par épha.
Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
25 Au septième mois, le quinzième jour du mois, à la fête, il offrira les mêmes sacrifices durant sept jours, tant pour le sacrifice pour le péché que pour l'holocauste et l'offrande et l'huile.
“‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”