< Ézéchiel 23 >

1 Et la parole de l'Éternel me fut adressée en ces mots:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils de l'homme, il y avait deux femmes, filles d'une même mère.
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 Et elles furent impudiques en Egypte, dans leur jeunesse elles furent impudiques; là leurs mamelles furent pressées, et là on porta la main à leur sein virginal.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 Or voici leurs noms: Ohola c'est l'aînée, et Oholiba sa sœur. Et elles furent unies à moi, et elles enfantèrent des fils et des filles. Or voici leurs noms: Samarie est Ohola, et Jérusalem Oholiba.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Et Ohola me désertant fut impudique, et s'éprit de ses amants, des Assyriens, ses voisins,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 revêtus de pourpre violette, gouverneurs et satrapes, tous beaux jeunes hommes, cavaliers, montés sur des coursiers.
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 Et elle leur prostitua son amour adultère, à toute l'élite des enfants de l'Assyrie, et elle se souilla avec tous ceux dont elle s'éprit, avec toutes leurs idoles.
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 Cependant elle ne renonça point à ses impudicités avec l'Egypte; car ils avaient habité avec elle dans sa jeunesse, et porté la main à son sein virginal, et s'étaient livrés à des débordements d'impudicité avec elle.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 Aussi l'ai-je livrée aux mains de ses amants, aux mains des enfants de l'Assyrie dont elle était éprise.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 Ils découvrirent sa nudité, enlevèrent ses fils et ses filles et la firent périr elle-même par l'épée; et elle devint la fable des femmes, quand ils eurent exécuté sur elle les jugements.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 C'est ce dont fut témoin Oholiba sa sœur; mais elle fut pire qu'elle dans ses débordements, et son impudicité fut pire que l'impudicité de sa sœur.
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 Elle s'éprit des enfants de l'Assyrie, gouverneurs et. satrapes, ses voisins, vêtus magnifiquement, cavaliers, montés sur des coursiers, tous beaux jeunes hommes.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 Et je vis qu'elle se souillait; elles suivaient l'une et l'autre la même voie.
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 Mais elle ajouta encore à son impudicité, et à la vue d'hommes dessinés sur la muraille, images des Chaldéens, dessinés au vermillon,
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 portant une ceinture autour de leurs reins, sur leurs têtes des tiares tombantes, tous ayant l'air des guerriers montés sur les chars, pareils aux enfants de Babel, de la Chaldée, leur pays natal,
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 elle s'éprit d'eux au premier coup d'œil, et leur envoya des messagers en Chaldée.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 Et les enfants de Babel vinrent partager avec elle le lit des amours, et la souillèrent par leur impudicité, et elle se souilla avec eux, puis son cœur se détacha d'eux.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 Et quand elle montra son impudicité, et montra sa nudité, alors mon cœur se détacha d'elle, comme mon cœur s'était détaché de sa sœur.
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 Cependant elle ajouta encore à son impudicité, en se reportant aux jours de sa jeunesse, quand elle avait été impudique au pays d'Égypte,
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 et elle s'éprit de ses concubinaires qui avaient des membres comme des ânes, et étaient lascifs comme des étalons.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 Tu regrettas ta jeunesse criminelle, quand des Égyptiens pressaient tes mamelles, à cause de ton sein virginal.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 Aussi, Oholiba, ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Voici, je vais exciter contre toi tes amants, dont tu t'es détachée, et je les amènerai contre toi de toutes parts:
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 les enfants de Babel et tous les Chaldéens, chefs, riches et Grands, tous les enfants de l'Assyrie avec eux, beaux jeunes hommes, tous gouverneurs et satrapes, combattant sur des chars, hommes d'élite, montés sur des coursiers.
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 Et ils s'avancent contre toi avec des armes, des chars et des roues, et des troupes nombreuses; et avec le pavois, le bouclier et le casque ils se portent sur toi de toutes parts; et je leur remets le jugement, afin qu'ils te jugent selon leurs lois;
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 et je donne cours à mon indignation contre toi, afin qu'ils te traitent avec fureur; ils te couperont le nez et les oreilles, et ta postérité périra par l'épée: ils enlèveront tes fils et tes filles, et ta postérité sera dévorée par le feu;
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 et ils te dépouilleront de tes habits et prendront tes superbes atours.
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 Et ainsi je mettrai fin à ton crime et à ton impudicité d'Egypte, pour que tu ne lèves plus les yeux vers eux, et que tu ne portes plus tes pensées vers l'Egypte.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 Car ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Voici, je vais te livrer aux mains de ceux que tu hais, aux mains de ceux de qui ton cœur s'est détaché;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 et ils te traiteront avec haine, et prendront tous tes gains, et te laisseront nue et découverte, afin de mettre à découvert ta nudité que tu as prostituée, et ton crime, et ton impudicité.
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 Je te ferai ces choses parce que tu es allée te prostituant après les nations, et parce que tu t'es souillée de leurs idoles.
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Tu as suivi le même chemin que ta sœur, aussi mettrai-je sa coupe en ta main.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 Ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Tu boiras la coupe de ta sœur, coupe profonde et large; elle excitera contre toi la risée et la moquerie; grande est sa capacité.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Tu seras chargée d'ivresse et de chagrin; c'est une coupe de stupeur et d'effroi que la coupe de ta sœur Samarie.
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 Et tu la boiras, la videras, tu en lécheras les têts, dont tu te déchireras les mamelles; car je l'ai prononcé, dit le Seigneur, l'Éternel.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 Aussi, ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Parce que tu m'as oublié, et que tu m'as jeté derrière toi, toi aussi subis les suites de ton crime et de ton impudicité.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 Et l'Éternel me dit: Fils de l'homme, jugeras-tu Ohola et Oholiba? et montre-leur leurs abominations:
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 qu'elles furent adultères, qu'il y a du sang à leurs mains, et qu'elles ont commis adultère avec leurs idoles, et que même leurs enfants qu'elles avaient enfantés pour moi, elles les leur ont consacrés comme nourriture.
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 Voici ce qu'elles m'ont encore fait: elles ont souillé mon sanctuaire en ce jour-là, et profané mes sabbats.
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 Car après avoir immolé leurs enfants à leurs idoles, elles sont venues dans mon sanctuaire ce jour-là pour le profaner, et voici, cela, elles l'ont fait au sein de ma maison.
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 Bien plus, elles envoyèrent chercher des hommes qui devaient venir de loin, et auxquels des messagers furent expédiés, et voici, ils vinrent: pour eux tu te baignas, peignis tes yeux, et te paras-de tes parures;
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 et tu te plaças sur un lit magnifique: au devant était dressée une table sur laquelle tu mis mon encens et mon huile;
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 et de ce lieu on entendait sortir les cris joyeux d'une multitude en sécurité; et outre les hommes de la multitude on avait fait venir des buveurs du désert, qui leur mirent des bracelets aux mains et de superbes diadèmes sur la tête.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 Alors je dis de celle qu'ont usée les adultères: Maintenant aura-t-on commerce avec elle? avec elle!
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 Et l'on vint à elle, comme on vient à une prostituée; c'est ainsi qu'on vint à Ohola et à Oholiba, femmes criminelles.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 Mais des hommes justes les jugeront selon la loi des adultères, et selon la loi des meurtriers; car elles sont adultères, et ont du sang à leurs mains.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 Car ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Je vais faire avancer contre elles un rassemblement, et les livrer aux tourments et au pillage;
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 et elles seront lapidées par eux, et taillées en pièces par leurs épées, leurs fils et leurs filles seront égorgés, et leurs maisons brûlées au feu.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 Ainsi mettrai-je fin au crime dans le pays, afin que toutes les femmes en reçoivent instruction, et ne deviennent pas criminelles comme elles.
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 Et ils feront retomber leur crime sur vous, et vous subirez le, péché de votre idolâtrie, afin que vous sachiez que je suis le Seigneur, l'Éternel.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

< Ézéchiel 23 >