< Deutéronome 14 >
1 Vous êtes fils de l'Éternel, votre Dieu: ne vous faites pas des incisions et ne vous rasez pas l'intervalle des yeux, pour un mort.
Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
2 Car tu es un peuple consacré à l'Éternel, ton Dieu, et l'Éternel t'a choisi pour être son peuple particulier entre tous les peuples qui sont sur la face de la terre.
pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
3 Abstiens-toi de tout aliment abominable.
Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
4 Voici les animaux dont vous vous nourrirez: le bœuf, la brebis et la chèvre,
Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
5 le cerf, et la gazelle et le daim, et le bouquetin, et le dischon et le theo, et le zamer,
mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
6 et tout animal ayant la corne fendue, fendue de part en part, en fourche; tout ce qui rumine parmi les animaux, vous servira de nourriture.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
7 Voici seulement ceux que vous ne mangerez pas, des ruminants et de ceux qui ont la corne fendue de part en part: le chameau, et le lièvre, et la gerboise, car ils ruminent, mais n'ont pas la corne fendue: tenez-les pour immondes;
Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
8 et le porc, car il a la corne fendue, mais ne rumine pas; tenez-le pour immonde: vous ne mangerez pas leur chair et ne toucherez pas leurs cadavres.
Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
9 Voici ceux que vous mangerez entre tous les aquatiques: tout ce qui a nageoires et écailles, vous pouvez le manger;
Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 mais vous vous abstiendrez de tout ce qui n'a pas nageoires et écailles: tenez-le pour immonde.
Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
11 Vous pouvez manger de tous les oiseaux purs, mais voici ceux dont vous vous abstiendrez:
Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
12 l'aigle, l'orfraie et l'aigle de mer
Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
13 et le faucon et le vautour et le milan selon leur espèce,
nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
14 et tous les corbeaux selon leurs espèces, et l'autruche femelle
mtundu uliwonse wa khwangwala,
15 et l'autruche mâle et la mouette et l'épervier selon leur espèce,
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
16 et le hibou et l'ibis et le cygne
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
17 et le pélican et le percnoptère et le pélican sauteur
tsekwe, vuwo, dembo,
18 et la cigogne et le perroquet selon leur espèce, et la huppe et la chauve-souris.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
19 Et tenez pour immonde tout ver ailé: il ne se mangera pas.
Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
20 Mangez de tous les oiseaux purs.
Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
21 Vous ne mangerez point de bête morte, tu pourras la donner à l'étranger qui est dans tes Portes pour la manger ou la vendre à un homme du dehors; car tu es un peuple consacré à l'Éternel, ton Dieu. Tu ne feras point cuire le chevreau au lait de sa mère.
Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
22 Tu dîmeras tout le produit de tes semailles, que rend annuellement ton champ.
Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
23 Et tu mangeras devant l'Éternel, ton Dieu, au lieu qu'il aura choisi pour y fixer son nom, la dîme de ton blé, de ton moût et de ton huile et la primogéniture de ton gros et menu bétail, afin que tu apprennes à craindre en tout temps l'Éternel, ton Dieu.
Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
24 Et si le chemin est trop long pour que tu puisses l'y transporter vu la distance du lieu choisi par l'Éternel, ton Dieu, pour y fixer son nom, et l'abondance dont t'aura béni l'Éternel, ton Dieu,
Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
25 échange-la contre de l'argent, et serre l'argent dans ta main, et va au lieu choisi par l'Éternel, ton Dieu.
ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
26 Et donne cet argent en échange de tout ce que tu désires en fait de bœufs, de brebis, de vin, de cervoise, de tout ce que ton désir réclame, et mange, là, devant l'Éternel, ton Dieu, te réjouissant toi et ta famille.
Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
27 Et ne néglige pas le Lévite qui est dans tes Portes, car il n'a ni portion ni lot parmi vous.
Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
28 A la fin de chaque troisième année tu extrairas toute la dîme de ta récolte de cette année-là, et tu la déposeras dans tes Portes;
Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
29 et le Lévite (car il n'a ni portion ni lot parmi vous) et l'étranger et l'orphelin et la veuve qui sont dans tes Portes, viendront et mangeront et se rassasieront, afin que l'Éternel, ton Dieu, te bénisse dans tout le travail de tes mains que tu entreprendras.
kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.