< Psaumes 61 >
1 O Dieu, écoute mon cri, sois attentif à ma prière!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
2 Du bout de la terre, je crie à toi, quand le cœur me manque; conduis-moi sur ce rocher, qui est trop élevé pour moi.
Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
3 Car tu as été mon refuge, ma forte tour devant l'ennemi.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
4 Je séjournerai dans ta tente à jamais; je me retirerai sous l'abri de tes ailes. (Sélah)
Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
5 Car tu as, ô Dieu, exaucé mes vœux; tu m'as donné l'héritage de ceux qui craignent ton nom.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
6 Ajoute des jours aux jours du roi, et que ses années soient d'âge en âge!
Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
7 Qu'il siège à toujours devant Dieu! Donne-lui pour garde ta bonté, ta fidélité.
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
8 Alors je chanterai ton nom à jamais, et j'accomplirai mes vœux chaque jour.
Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.