< Proverbes 4 >

1 Enfants, écoutez l'instruction de votre père, et soyez attentifs pour connaître la prudence.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Car je vous donne de bons conseils; n'abandonnez point mon enseignement.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Quand j'étais encore enfant près de mon père, tendre et chéri auprès de ma mère,
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Il m'enseignait et me disait: Que ton cœur retienne mes paroles; garde mes commandements, et tu vivras.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Acquiers la sagesse, acquiers la prudence; ne l'oublie pas, et ne te détourne point des paroles de ma bouche.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Ne l'abandonne pas, elle te gardera; aime-la, et elle te protégera.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Le commencement de la sagesse, c'est d'acquérir la sagesse; acquiers la prudence au prix de tout ton avoir.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Estime-la, et elle t'élèvera; elle fera ta gloire quand tu l'auras embrassée.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Elle posera sur ta tête une couronne de grâces, et te donnera un diadème de gloire.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Écoute, mon fils, et reçois mes paroles; et les années de ta vie te seront multipliées.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Je t'ai enseigné le chemin de la sagesse, et je t'ai fait marcher dans les sentiers de la droiture.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Quand tu marcheras, tes pas ne seront pas gênés, et quand tu courras, tu ne broncheras point.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Embrasse l'instruction, ne la lâche point; garde-la, car c'est ta vie.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 N'entre point dans le sentier des méchants, et ne pose pas ton pied dans le chemin des pervers.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Détourne-t'en, ne passe point par là; écarte-toi, et passe outre.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Car ils ne dormiraient pas, s'ils n'avaient fait quelque mal, et le sommeil leur serait ôté, s'ils n'avaient fait tomber personne.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Car ils mangent le pain de la méchanceté, et ils boivent le vin de la violence.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Mais le sentier des justes est comme la lumière resplendissante, dont l'éclat augmente jusques à ce que le jour soit dans sa perfection.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 La voie des méchants est comme l'obscurité; ils ne voient point ce qui les fera tomber.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Mon fils, sois attentif à mes paroles, incline ton oreille à mes discours.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Qu'ils ne s'éloignent pas de tes yeux, garde-les dans ton cœur.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Car ils sont la vie de ceux qui les trouvent, et la santé de tout leur corps.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Garde ton cœur plus que toute autre chose qu'on garde; car c'est de lui que procèdent les sources de la vie.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Éloigne de toi la perversité de la bouche, et la fausseté des lèvres.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Que tes yeux regardent droit, et que tes paupières se dirigent devant toi.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Balance le chemin de tes pieds, afin que toutes tes voies soient affermies.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Ne te détourne ni à droite ni à gauche; retire ton pied du mal.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbes 4 >