< Proverbes 10 >
1 Proverbes de Salomon. L'enfant sage réjouit son père; mais l'enfant insensé est le chagrin de sa mère.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Les trésors de méchanceté ne profitent point; mais la justice délivre de la mort.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 L'Éternel ne permet pas que le juste souffre de la faim; mais il repousse l'avidité des méchants.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 La main paresseuse appauvrit; mais la main des diligents enrichit.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Celui qui amasse en été est un fils prudent; celui qui dort pendant la moisson est un fils qui fait honte.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Il y a des bénédictions sur la tête du juste; mais la violence fermera la bouche aux méchants.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 La mémoire du juste sera en bénédiction; mais le nom des méchants tombera en pourriture.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Celui qui a le cœur sage, reçoit les avertissements; mais celui qui a les lèvres insensées, tombera.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Celui qui marche dans l'intégrité, marche en assurance; mais celui qui pervertit ses voies, sera découvert.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Celui qui cligne de l'œil cause du trouble; et celui qui a les lèvres insensées, court à sa perte.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 La bouche du juste est une source de vie; mais la violence fermera la bouche aux méchants.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 La haine excite les querelles; mais la charité couvre toutes les fautes.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 La sagesse se trouve sur les lèvres de l'homme sage; mais la verge est pour le dos de celui qui est dépourvu de sens.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Les sages tiennent la science en réserve; mais la bouche de l'insensé est une ruine prochaine.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Les biens du riche sont sa ville forte; mais la pauvreté des misérables est leur ruine.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 L'œuvre du juste conduit à la vie; mais le fruit du méchant est le péché.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Celui qui garde l'instruction, est dans le chemin de la vie; mais celui qui oublie la correction, s'égare.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Celui qui dissimule la haine a des lèvres trompeuses; et celui qui répand la calomnie, est un insensé.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 Où il y a beaucoup de paroles, il ne manque pas d'y avoir du péché; mais celui qui retient ses lèvres est prudent.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 La langue du juste est un argent de choix; mais le cœur des méchants vaut peu de chose.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Les lèvres du juste nourrissent beaucoup d'hommes; mais les insensés mourront, faute de sens.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 C'est la bénédiction de l'Éternel qui enrichit, et il n'y joint aucune peine.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Faire le mal est la joie de l'insensé; la sagesse est celle de l'homme prudent.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Ce que le méchant craint, lui arrivera; mais Dieu accordera aux justes ce qu'ils désirent.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Comme le tourbillon passe, ainsi le méchant disparaît; mais le juste s'appuie sur un fondement éternel.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Ce que le vinaigre est aux dents, et la fumée aux yeux, tel est le paresseux à ceux qui l'envoient.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 La crainte de l'Éternel multiplie les jours; mais les années des méchants seront retranchées.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 L'espérance des justes est la joie; mais l'attente des méchants périra.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 La voie de l'Éternel est la force de l'homme intègre; mais elle est la ruine des ouvriers d'iniquité.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Le juste ne sera jamais ébranlé; mais les méchants n'habiteront point sur la terre.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 La bouche du juste produira la sagesse; mais la langue perverse sera retranchée.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Les lèvres du juste connaissent ce qui est agréable; mais la bouche des méchants n'est que perversité.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.