< Nombres 34 >
1 L'Éternel parla encore à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Ordonne ceci aux enfants d'Israël, et dis-leur: Lorsque vous serez entrés au pays de Canaan, ce pays qui vous échoit en héritage, le pays de Canaan selon ses limites,
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 La région du Midi sera à vous depuis le désert de Tsin, le long d'Édom. Ainsi votre frontière du Midi partira du bout de la mer Salée, vers l'Orient.
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 Et cette frontière tournera au midi de la montée d'Akrabbim, passera vers Tsin, et aboutira au midi de Kadès-Barnéa; puis elle sortira vers Hatsar-Addar, et passera vers Atsmon.
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 D'Atsmon la frontière tournera vers le torrent d'Égypte, et aboutira à la mer.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 Et quant à la frontière d'Occident, vous aurez la grande mer pour limite; ce sera votre frontière occidentale.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 Et voici quelle sera votre frontière du Nord: depuis la grande mer vous marquerez pour vos limites la montagne de Hor;
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 Puis de la montagne de Hor, vous marquerez pour vos limites l'entrée de Hamath, et la frontière aboutira à Tsedad.
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 Et cette frontière sortira vers Ziphron, et aboutira à Hatsar-Enan; telle sera votre frontière du Nord.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 Puis vous prendrez pour vos frontières, vers l'Orient, de Hatsar-Enan à Shepham.
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 Et la frontière descendra de Shepham à Ribla, à l'Orient d'Aïn; puis cette frontière descendra et atteindra la côte de la mer de Kinnéreth, vers l'Orient;
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 Enfin la frontière descendra vers le Jourdain, et aboutira à la mer Salée. Tel sera le pays que vous aurez, selon ses frontières tout autour.
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 Et Moïse commanda aux enfants d'Israël, et leur dit: C'est là le pays que vous partagerez par le sort, et que l'Éternel a commandé de donner aux neuf tribus et à la moitié d'une tribu.
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 Car la tribu des descendants de Ruben, selon les maisons de leurs pères, et la tribu des descendants de Gad, selon les maisons de leurs pères, et la demi-tribu de Manassé ont reçu leur héritage.
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 Ces deux tribus et la demi-tribu ont reçu leur héritage de ce côté-ci du Jourdain de Jérico, à l'Orient, vers le Levant.
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 L'Éternel parla encore à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Voici les noms des hommes qui vous partageront le pays: Éléazar, le sacrificateur, et Josué, fils de Nun.
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 Vous prendrez aussi un chef de chaque tribu, pour partager le pays.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 Voici les noms de ces hommes: Pour la tribu de Juda, Caleb, fils de Jéphunné;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 Pour la tribu des enfants de Siméon, Samuël, fils d'Ammihud;
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 Pour la tribu des enfants de Benjamin, Élidad, fils de Kislon;
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 Pour la tribu des enfants de Dan, un chef, Buki, fils de Jogli;
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 Pour les enfants de Joseph: pour la tribu des enfants de Manassé, un chef, Hanniel, fils d'Éphod;
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 Et pour la tribu des enfants d'Éphraïm, un chef, Kemuël, fils de Shiphtan;
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 Pour la tribu des enfants de Zabulon, un chef, Élitsaphan, fils de Parnac;
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 Pour la tribu des enfants d'Issacar, un chef, Paltiel, fils d'Azzan;
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 Pour la tribu des enfants d'Asser, un chef, Ahihud, fils de Shelomi;
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 Et pour la tribu des enfants de Nephthali, un chef, Pedahel, fils d'Ammihud.
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 Tels sont ceux auxquels l'Éternel commanda de partager l'héritage aux enfants d'Israël, dans le pays de Canaan.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.