< Nombres 31 >

1 L'Éternel parla encore à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Venge les enfants d'Israël des Madianites; puis tu seras recueilli vers tes peuples.
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 Moïse parla donc au peuple, en disant: Équipez d'entre vous des hommes pour la guerre; et qu'ils attaquent Madian, pour exécuter la vengeance de l'Éternel sur Madian.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 Vous enverrez à la guerre mille hommes par tribu, de toutes les tribus d'Israël.
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 On leva donc, d'entre les milliers d'Israël, mille hommes par tribu, douze mille hommes équipés pour la guerre.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 Et Moïse les envoya à la guerre, mille par tribu, avec Phinées, fils d'Éléazar, le sacrificateur, qui avait les instruments sacrés, les trompettes éclatantes en sa main.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 Ils firent donc la guerre contre Madian, comme l'Éternel l'avait commandé à Moïse, et ils tuèrent tous les mâles.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 Ils tuèrent aussi les rois de Madian, outre les autres qui furent tués: Évi, Rékem, Tsur, Hur et Réba, cinq rois de Madian; ils tuèrent aussi par l'épée Balaam, fils de Béor.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 Et les enfants d'Israël emmenèrent prisonnières les femmes de Madian et leurs petits enfants; et ils pillèrent tout leur bétail, tous leurs troupeaux, et tous leurs biens.
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 Et ils brûlèrent toutes leurs villes, avec leurs habitations, et tous leurs bourgs;
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 Et ils prirent toutes les dépouilles, et tout le butin, en hommes et en bétail;
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 Et ils amenèrent les prisonniers, les dépouilles et le butin, à Moïse, à Éléazar, le sacrificateur, et à l'assemblée des enfants d'Israël, au camp, dans les plaines de Moab, qui sont près du Jourdain de Jérico.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 Alors Moïse, Éléazar, le sacrificateur, et tous les principaux de l'assemblée, sortirent à leur rencontre hors du camp.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 Et Moïse s'irrita contre les capitaines de l'armée, les chefs de milliers, et les chefs de centaines qui revenaient de cette expédition guerrière.
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 Et Moïse leur dit: Vous avez laissé la vie à toutes les femmes?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Voici, ce sont elles qui, d'après la parole de Balaam, ont donné occasion aux enfants d'Israël de commettre un crime contre l'Éternel dans l'affaire de Peor, ce qui attira la plaie sur l'assemblée de l'Éternel.
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Maintenant donc tuez tout mâle parmi les petits enfants, et tuez toute femme qui aura eu compagnie d'homme;
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 Mais laissez vivre, pour vous, toutes les jeunes filles qui n'ont point eu compagnie d'homme.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 Quant à vous, campez sept jours hors du camp. Quiconque a tué quelqu'un, et quiconque a touché quelqu'un de tué, qu'il se purifie le troisième jour et le septième jour, lui et ses prisonniers.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 Vous purifierez aussi tout vêtement, tout objet de peau, tout ouvrage en poil de chèvre, et tout ustensile de bois.
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 Et Éléazar, le sacrificateur, dit aux hommes de l'armée qui étaient allés à la guerre: Voici l'ordonnance de la loi que l'Éternel a commandée à Moïse.
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 L'or, l'argent, l'airain, le fer, l'étain, et le plomb, tout ce qui peut aller au feu,
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 Vous le ferez passer par le feu, et il sera pur; toutefois on le purifiera avec l'eau de purification. Mais tout ce qui ne va pas au feu, vous le ferez passer dans l'eau.
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 Vous laverez aussi vos vêtements le septième jour, et vous serez purs; ensuite, vous entrerez au camp.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 L'Éternel parla encore à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 Fais le compte du butin qu'on a emmené, en personnes et en bétail, toi, Éléazar le sacrificateur, et les chefs des maisons des pères de l'assemblée;
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 Et partage le butin entre les combattants qui sont allés à la guerre et toute l'assemblée.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 Et tu prélèveras sur les gens de guerre qui sont allés à la bataille, un tribut pour l'Éternel, un sur cinq cents, tant des personnes, que des bœufs, des ânes et des brebis.
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 Vous le prendrez sur leur moitié, et tu le donneras à Éléazar, le sacrificateur, en offrande à l'Éternel.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 Et de la moitié échue aux enfants d'Israël, tu mettras à part un sur cinquante, tant des personnes, que des bœufs, des ânes et des brebis, et de tout le bétail, et tu le donneras aux Lévites, qui ont la garde de la Demeure de l'Éternel.
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 Et Moïse et Éléazar, le sacrificateur, firent comme l'Éternel avait commandé à Moïse.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 Or le butin, reste du pillage que le peuple qui était allé à la guerre avait fait, était de six cent soixante et quinze mille brebis,
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 De soixante et douze mille bœufs,
Ngʼombe 72,000,
34 De soixante et un mille ânes.
abulu 61,000,
35 Quant aux femmes qui n'avaient point eu compagnie d'homme, elles étaient en tout trente-deux mille âmes.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 La moitié, la part de ceux qui étaient allés à la guerre, fut de trois cent trente-sept mille cinq cents brebis,
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 Dont le tribut pour l'Éternel fut de six cent soixante-quinze;
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 Et trente-six mille bœufs, dont le tribut pour l'Éternel fut de soixante et douze;
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 Et trente mille cinq cents ânes, dont le tribut pour l'Éternel fut de soixante et un;
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 Et seize mille personnes, dont le tribut pour l'Éternel fut de trente-deux personnes.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 Or Moïse donna à Éléazar, le sacrificateur, le tribut de l'offrande à l'Éternel, comme l'Éternel le lui avait commandé.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 Puis, de la moitié appartenant aux enfants d'Israël, que Moïse avait séparée de celle des hommes qui étaient allés à la guerre,
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 (Or, cette moitié échue à l'assemblée était de trois cent trente-sept mille cinq cents brebis,
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 Trente-six mille bœufs,
ngʼombe 36,000,
45 Trente mille cinq cents ânes,
abulu 30,500,
46 Et seize mille personnes),
anthu 16,000.
47 De cette moitié, appartenant aux enfants d'Israël, Moïse en mit à part un sur cinquante, tant des personnes que du bétail, et il les donna aux Lévites qui avaient charge de garder la Demeure de l'Éternel, comme l'Éternel le lui avait commandé.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 Et les capitaines des milliers de l'armée, les chefs de milliers et les chefs de centaines, s'approchèrent de Moïse,
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 Et lui dirent: Tes serviteurs ont fait le compte des gens de guerre qui étaient sous nos ordres, et il n'en manque pas un seul.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 Et nous avons apporté comme offrande à l'Éternel, chacun ce qu'il a trouvé d'objets d'or, chaînettes, bracelets, anneaux, pendants d'oreilles et colliers, afin de faire l'expiation pour nos personnes devant l'Éternel.
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 Alors Moïse et Éléazar, le sacrificateur, reçurent d'eux l'or et tous les joyaux travaillés.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 Et tout l'or de l'offrande qu'on préleva pour l'Éternel, de la part des chefs de milliers et des chefs de centaines, fut de seize mille sept cent cinquante sicles.
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 Or les gens de l'armée avaient pillé chacun pour soi.
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 Moïse et Éléazar, le sacrificateur, prirent donc l'or des chefs de milliers et de centaines, et le portèrent au tabernacle d'assignation, comme mémorial pour les enfants d'Israël, devant l'Éternel.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

< Nombres 31 >