< Juges 20 >
1 Alors tous les enfants d'Israël sortirent, depuis Dan jusqu'à Béer-Shéba, et jusqu'au pays de Galaad; et l'assemblée se réunit comme si ce n'eût été qu'un seul homme, devant l'Éternel, à Mitspa.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
2 Et les chefs de tout le peuple, et toutes les tribus d'Israël se présentèrent dans l'assemblée du peuple de Dieu, au nombre de quatre cent mille hommes de pied, portant l'épée.
Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
3 Or les enfants de Benjamin apprirent que les enfants d'Israël étaient montés à Mitspa. Et les enfants d'Israël dirent: Parlez; comment ce crime a-t-il été commis?
Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
4 Et le Lévite, le mari de la femme qu'on avait tuée, répondit et dit: J'étais entré à Guibea de Benjamin, moi et ma concubine, pour y passer la nuit.
Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
5 Les maîtres de Guibea se sont élevés contre moi, et ils ont environné de nuit la maison où j'étais, prétendant me tuer; et ils ont fait violence à ma concubine, et elle en est morte.
Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
6 Alors, ayant pris ma concubine, je l'ai mise en pièces, et j'en ai envoyé par tout le territoire de l'héritage d'Israël; car ils ont commis un crime énorme, et une infamie en Israël.
Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
7 Vous voici tous, enfants d'Israël; consultez-vous, donnez ici votre avis.
Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
8 Et tout le peuple se leva, comme un seul homme, en disant: Aucun de nous n'ira dans sa tente, et personne ne se retirera dans sa maison.
Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
9 Mais, voici ce que nous ferons maintenant à Guibea; nous marcherons contre elle d'après le sort.
Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
10 Nous prendrons dix hommes sur cent, d'entre toutes les tribus d'Israël, et cent sur mille, et mille sur dix mille, afin qu'ils prennent des vivres pour le peuple, et que, se rendant à Guibea de Benjamin, on la traite selon l'infamie du crime qu'elle a commis en Israël.
Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
11 Ainsi tous les hommes d'Israël s'assemblèrent contre cette ville-là, unis comme un seul homme.
Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
12 Les tribus d'Israël envoyèrent des hommes dans toute la tribu de Benjamin, pour dire: Quelle méchante action a-t-on commise parmi vous?
Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
13 Livrez-nous maintenant ces hommes pervers qui sont à Guibea, afin que nous les fassions mourir, et que nous ôtions le mal du milieu d'Israël. Mais les Benjamites ne voulurent point écouter la voix de leurs frères, les enfants d'Israël.
Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
14 Et les enfants de Benjamin sortirent de leurs villes, et s'assemblèrent à Guibea, pour aller combattre les enfants d'Israël.
Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
15 En ce jour-là, on fit le dénombrement des enfants de Benjamin, venus des villes; et il se trouva vingt-six mille hommes tirant l'épée, sans les habitants de Guibea, dont on fit aussi le dénombrement, formant sept cents hommes d'élite.
Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
16 Parmi tout ce peuple, il y avait sept cents hommes d'élite qui ne se servaient pas de la main droite. Tous ceux-là lançaient des pierres avec une fronde contre un cheveu, et ne le manquaient pas.
Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
17 On fit aussi le dénombrement des hommes d'Israël, sans compter ceux de Benjamin, et il s'en trouva quatre cent mille hommes tirant l'épée, tous gens de guerre.
Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
18 Ils partirent donc, montèrent à Béthel, et consultèrent Dieu. Et les enfants d'Israël dirent: Qui de nous montera le premier pour faire la guerre aux enfants de Benjamin? Et l'Éternel répondit: Juda montera le premier.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
19 Dès le matin, les enfants d'Israël se mirent donc en marche, et campèrent près de Guibea.
Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
20 Et les hommes d'Israël sortirent pour combattre ceux de Benjamin, et se rangèrent en bataille contre eux devant Guibea.
Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
21 Alors les enfants de Benjamin sortirent de Guibea, et ce jour-là ils étendirent par terre vingt-deux mille hommes d'Israël.
A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
22 Toutefois le peuple, les hommes d'Israël reprirent courage, et ils se rangèrent de nouveau en bataille, dans le lieu où ils s'étaient placés le premier jour.
Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
23 Et les enfants d'Israël montèrent, et pleurèrent devant l'Éternel jusqu'au soir. Ils consultèrent l'Éternel en disant: M'approcherai-je encore pour combattre contre les enfants de Benjamin, mon frère? Et l'Éternel répondit: Montez contre lui.
Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
24 Le lendemain donc, les enfants d'Israël s'approchèrent des enfants de Benjamin.
Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
25 Les Benjamites sortirent aussi contre eux de Guibea ce second jour, et ils étendirent encore par terre dix-huit mille hommes des enfants d'Israël, qui tiraient tous l'épée.
Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
26 Alors tous les enfants d'Israël et tout le peuple montèrent, et vinrent à Béthel. Ils y pleurèrent, et se tinrent là, devant l'Éternel, et jeûnèrent ce jour-là jusqu'au soir; et ils offrirent des holocaustes et des sacrifices de prospérité devant l'Éternel.
Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
27 Ensuite les enfants d'Israël consultèrent l'Éternel (l'arche de l'alliance de Dieu était alors en ce lieu-là;
Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
28 Et Phinées, fils d'Éléazar, fils d'Aaron, se tenait devant l'Éternel); ils dirent donc: Dois-je marcher encore pour combattre les enfants de Benjamin, mon frère, ou dois-je m'en abstenir? Et l'Éternel répondit: Montez; car demain je les livrerai entre vos mains.
Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
29 Alors Israël mit des embuscades autour de Guibea.
Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
30 Et les enfants d'Israël montèrent, le troisième jour, contre les Benjamites, et se rangèrent contre Guibea comme les autres fois.
Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
31 Or les Benjamites, étant sortis à la rencontre du peuple, furent attirés loin de la ville. Et ils commencèrent à en frapper quelques-uns du peuple, comme les autres fois, et il y eut environ trente hommes d'Israël qui furent blessés à mort dans les chemins, dont l'un monte à Béthel et l'autre à Guibea, par la campagne.
Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
32 Et les enfants de Benjamin disaient: Ils tombent devant nous comme la première fois. Mais les enfants d'Israël disaient: Fuyons, et attirons-les loin de la ville, dans les chemins.
Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
33 Alors tous ceux d'Israël, se levant du lieu où ils étaient, se rangèrent à Baal-Thamar, et l'embuscade d'Israël déboucha de son poste, de la prairie de Guibea;
Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
34 Et dix mille hommes d'élite, de tout Israël, vinrent contre Guibea; et la mêlée fut rude, et ceux de Benjamin n'aperçurent point le mal qui allait tomber sur eux.
Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
35 Et l'Éternel battit Benjamin devant les Israélites; et les enfants d'Israël, en ce jour-là, tuèrent vingt-cinq mille et cent hommes de Benjamin, tous tirant l'épée.
Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
36 Les Benjamites avaient cru que les hommes d'Israël étaient battus. Or, ils avaient reculé devant ceux de Benjamin; car ils se reposaient sur les embuscades qu'ils avaient mises près de Guibea.
Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
37 Et ceux qui étaient en embuscade, se jetèrent vivement sur Guibea; ainsi ceux qui étaient en embuscade marchèrent, et firent passer toute la ville au fil de l'épée.
Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
38 Or, les hommes d'Israël avaient donné pour signal à ceux qui étaient en embuscade, qu'ils fissent monter de la ville une épaisse fumée.
Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
39 Les hommes d'Israël avaient donc tourné le dos dans la bataille, et les Benjamites avaient commencé de frapper et de blesser à mort environ trente hommes de ceux d'Israël; et ils disaient: Certainement ils tombent devant nous comme à la première bataille!
ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
40 Mais quand une colonne de fumée s'éleva et commença à monter de la ville, ceux de Benjamin regardèrent derrière eux, et voici, la ville entière montait en feu vers le ciel;
Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
41 Alors les gens d'Israël se retournèrent, et ceux de Benjamin furent épouvantés en voyant le désastre qui allait les atteindre.
Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
42 Et ils tournèrent le dos devant ceux d'Israël, par le chemin du désert; mais l'armée d'Israël les serra de près; et ceux des villes, ils les tuèrent dans leurs propres endroits.
Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
43 Ils environnèrent Benjamin, le poursuivirent, et le foulèrent aux pieds, sans relâche, jusqu'à l'opposite de Guibea, vers le soleil levant.
Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
44 Il tomba ainsi dix-huit mille hommes de Benjamin, tous vaillants hommes.
Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
45 Parmi ceux qui tournèrent le dos pour s'enfuir vers le désert, au rocher de Rimmon, ceux d'Israël en grappillèrent, par les chemins, cinq mille hommes; et, les poursuivant de près jusqu'à Guidéom, ils en frappèrent deux mille.
Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
46 Tous ceux de Benjamin qui tombèrent ce jour-là furent donc vingt-cinq mille hommes, tirant l'épée, et tous vaillants hommes.
Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
47 Et il y eut six cents hommes, de ceux qui avaient tourné le dos, qui échappèrent vers le désert, au rocher de Rimmon, et demeurèrent au rocher de Rimmon pendant quatre mois.
Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
48 Mais les gens d'Israël revinrent vers les enfants de Benjamin, et les firent passer au fil de l'épée, tant les hommes de chaque ville, que le bétail et tout ce qui s'y trouva. Ils brûlèrent aussi toutes les villes qu'ils rencontrèrent.
Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.