< Job 41 >

1 Tu tireras le Léviathan avec un hameçon? et tu serreras sa langue avec une corde?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Mettras-tu un jonc dans ses narines, perceras-tu sa joue avec un crochet?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 T'adressera-t-il beaucoup de prières, et te dira-t-il de douces paroles?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Fera-t-il un accord avec toi, et le prendras-tu pour esclave à toujours?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 En joueras-tu comme d'un oiseau, et l'attacheras-tu pour amuser tes filles?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Les associés en feront-ils commerce, le partageront-ils entre des marchands?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Perceras-tu sa peau d'un dard, et sa tête d'un harpon?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Mets ta main sur lui: tu te souviendras de la bataille, et tu n'y reviendras pas.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Voici, tout espoir de le prendre est trompé; à son seul aspect on est jeté à terre!
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Il n'y a point d'homme si hardi qui l'ose réveiller; et qui se tiendra debout devant moi?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Qui m'a fait des avances, et je lui rendrai? Tout ce qui est sous les cieux est à moi.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Je ne me tairai pas sur ses membres, sur ses forces, et sur la beauté de sa stature.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Qui a soulevé le dessus de son vêtement? Qui est entré dans sa double mâchoire?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Qui a ouvert les portes de sa gueule? La terreur est autour de ses dents.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Ses puissants boucliers sont superbes; ils sont fermés, étroitement scellés.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Ils se touchent l'un l'autre, le vent ne passe point entre eux.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Ils sont adhérents l'un à l'autre; ils se tiennent, ils ne se séparent point.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Ses éternuements jettent un éclat de lumière, et ses yeux sont comme les paupières de l'aurore.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 De sa bouche sortent des lueurs, et s'échappent des étincelles de feu.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 De ses narines sort une fumée, comme d'un vase qui bout ou d'une chaudière.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Son souffle enflammerait des charbons, et une flamme sort de sa gueule.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 Dans son cou réside la force, et la terreur marche devant lui.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Les fanons de sa chair sont adhérents; ils sont massifs, inébranlables.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Son cœur est massif comme une pierre, massif comme la meule de dessous.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Quand il se lève, les plus forts tremblent, ils défaillent d'effroi.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Quand on l'approche, l'épée ne sert à rien, ni la lance, ni le dard, ni la cuirasse.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Il regarde le fer comme de la paille, et l'airain comme du bois pourri.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 La flèche ne le fait pas fuir, les pierres de la fronde sont pour lui comme du chaume;
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Comme du chaume, la massue; il se rit du frémissement des javelots.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Son ventre a des tessons pointus: il étend une herse sur le limon.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Il fait bouillonner le gouffre comme une chaudière, il rend la mer semblable à un vase de parfumeur.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Il laisse après lui une trace brillante, on dirait sur l'abîme une blanche chevelure.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Il n'a pas son pareil sur la terre; il a été fait pour ne rien craindre.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Il regarde tout ce qui est élevé; il est roi des plus fiers animaux.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Job 41 >