< Jérémie 11 >

1 La parole qui fut adressée à Jérémie, de la part de l'Éternel, en ces mots:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Écoutez les paroles de cette alliance, et parlez aux hommes de Juda et aux habitants de Jérusalem.
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 Tu leur diras: Ainsi a dit l'Éternel, le Dieu d'Israël: Maudit est l'homme qui n'écoute pas les paroles de cette alliance,
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 Que j'ai prescrite à vos pères le jour où je les ai retirés du pays d'Égypte, de la fournaise de fer, en disant: Écoutez ma voix, et faites toutes les choses que je vous commande, et vous serez mon peuple et je serai votre Dieu;
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 J'accomplirai le serment que j'ai fait à vos pères, de leur donner un pays où coulent le lait et le miel, comme vous le voyez aujourd'hui. Et je répondis et dis: Amen! ô Éternel!
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 Et l'Éternel me dit: Crie toutes ces paroles par les villes de Juda et par les rues de Jérusalem, en disant: Écoutez les paroles de cette alliance, et observez-les.
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 Car j'ai sommé vos pères, depuis le jour où je les fis monter du pays d'Égypte jusqu'à ce jour, je les ai sommés dès le matin, disant: Écoutez ma voix!
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 Mais ils n'ont pas écouté; ils n'ont pas prêté l'oreille; ils ont marché chacun selon la dureté de son cœur. Et j'ai fait venir sur eux toutes les paroles de cette alliance, que je leur avais commandé de garder et qu'ils n'ont point gardée.
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 Et l'Éternel me dit: Il y a une conjuration entre les hommes de Juda et entre les habitants de Jérusalem.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 Ils sont retournés aux iniquités de leurs ancêtres qui ont refusé d'écouter mes paroles, et ils sont allés après d'autres dieux pour les servir. La maison d'Israël et la maison de Juda ont violé mon alliance, que j'ai traitée avec leurs pères.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 C'est pourquoi, ainsi a dit l'Éternel: Voici, je vais faire venir sur eux un mal duquel ils ne pourront sortir; ils crieront vers moi, mais je ne les écouterai point.
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 Et les villes de Juda et les habitants de Jérusalem s'en iront crier vers les dieux auxquels ils offrent leurs parfums; mais ils ne les sauveront point au temps de leur malheur.
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 Car, ô Juda! tu as autant de dieux que de villes, et, autant il y a de rues à Jérusalem, autant vous avez dressé d'autels à l'infamie, des autels pour offrir des parfums à Baal.
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 Et toi, n'intercède pas pour ce peuple, n'élève pour eux ni cri ni prière; car je ne les écouterai pas, lorsqu'ils crieront vers moi à cause de leur malheur.
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 Que viendrait faire mon bien-aimé dans ma maison? Cette foule n'y est que pour commettre la fraude! Mais on ôtera de devant toi la chair sacrée. Quand tu fais le mal, c'est alors que tu t'élèves!
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 Olivier verdoyant, excellent par la beauté de son fruit, ainsi l'appelait l'Éternel. Au bruit d'un grand fracas il y allume le feu, et ses rameaux sont brisés!
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 Et l'Éternel des armées, qui t'a planté, a prononcé le mal contre toi, à cause du mal que se sont fait à elles-mêmes la maison d'Israël et la maison de Juda, en m'irritant par leurs encensements à Baal.
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 L'Éternel me l'a fait connaître, et je l'ai connu; alors tu m'as fait voir leurs œuvres.
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 Et moi, comme un agneau familier, qu'on mène pour être égorgé, je ne savais pas les mauvais desseins qu'ils méditaient contre moi: “Détruisons l'arbre avec son fruit, et l'exterminons de la terre des vivants, et qu'il ne soit plus fait mention de son nom! “
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 Mais l'Éternel des armées est un juste juge, qui sonde les reins et les cœurs. Tu me feras voir la vengeance que tu tireras d'eux; car je t'ai découvert ma cause.
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 C'est pourquoi, ainsi a dit l'Éternel contre les gens d'Anathoth, qui cherchent ta vie et qui disent: Ne prophétise pas au nom de l'Éternel, et tu ne mourras pas de notre main;
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 C'est pourquoi, ainsi dit l'Éternel des armées: Voici, je vais les punir; les jeunes hommes mourront par l'épée; leurs fils et leurs filles mourront par la famine.
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 Et il ne restera rien d'eux; car je ferai venir le mal sur les gens d'Anathoth, l'année de leur visitation.
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”

< Jérémie 11 >