< Isaïe 41 >
1 Iles, faites silence pour m'écouter, et que les peuples reprennent de nouvelles forces; qu'ils s'avancent, et qu'ils parlent! Approchons pour plaider ensemble!
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Qui a fait lever de l'Orient, celui dont la justice accompagne les pas? Il lui livre les nations, et le fait dominer sur les rois; il réduit leur épée en poussière, et leur arc est comme de la paille qui vole.
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Il les poursuit, il s'avance en paix par un chemin où il n'avait jamais mis les pieds.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Qui a fait et accompli ces choses? Celui qui appelle dès l'origine les générations; moi l'Éternel, le premier, qui suis aussi avec les derniers.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Les îles le voient, et sont dans la crainte; les extrémités de la terre tremblent; ils s'approchent, ils viennent;
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Ils s'aident l'un l'autre, et chacun dit à son frère: Courage!
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 L'ouvrier encourage le fondeur; celui qui polit au marteau encourage celui qui frappe l'enclume; il dit de la soudure: elle est bonne; et il fixe l'idole avec des clous, pour qu'elle ne branle pas.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Mais toi, Israël, mon serviteur; toi Jacob, que j'ai élu; race d'Abraham, qui m'a aimé;
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 Toi que j'ai pris des bouts de la terre, et que j'ai appelé de ses extrémités, à qui j'ai dit: Tu es mon serviteur; je t'ai élu, et je ne t'ai point rejeté.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Ne crains point, car je suis avec toi; ne sois point éperdu, car je suis ton Dieu! Je te fortifie, je t'aide, et je te maintiens par la droite de ma justice.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Voici, tous ceux qui s'irritent contre toi, seront honteux et confus. Ils seront réduits à rien et périront, ceux qui s'élèvent contre toi.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Tu les chercheras, et tu ne les trouveras plus, ceux qui disputaient contre toi; ceux qui te faisaient la guerre, périront et seront anéantis.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Car c'est moi, l'Éternel ton Dieu, qui te prends par la main et qui te dis: Ne crains point, je suis ton aide!
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Ne crains point, vermisseau de Jacob, faible reste d'Israël: Je suis ton aide, dit l'Éternel; le Saint d'Israël est ton Rédempteur.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Voici, je fais de toi une herse aiguë, neuve et armée de tranchants; tu fouleras les montagnes, tu les écraseras, et tu rendras les collines semblables à de la balle.
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Tu les vanneras, le vent les emportera, la tempête les dispersera; mais toi, tu te réjouiras en l'Éternel, tu te glorifieras dans le Saint d'Israël.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Les affligés et les misérables qui cherchent des eaux et qui n'en ont point, dont la langue est desséchée par la soif, moi, l'Éternel, je les exaucerai; moi, le Dieu d'Israël, je ne les abandonnerai point.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Je ferai jaillir des fleuves sur les hauteurs, et des sources au milieu des vallées; je changerai le désert en étang, et la terre aride en sources d'eaux;
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Je mettrai dans le désert le cèdre, l'acacia, le myrte et l'olivier; je planterai dans les solitudes le cyprès, l'orme et le buis ensemble;
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 Afin qu'ils voient et qu'ils sachent, qu'ils observent et comprennent tous, que la main de l'Éternel a fait ces choses, que le Saint d'Israël en est l'auteur.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Présentez votre cause, dit l'Éternel; exposez vos preuves, dit le roi de Jacob.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Qu'ils les exposent! Qu'ils nous déclarent ce qui doit arriver! Vos premières prédictions, quelles furent-elles? Déclarez-nous-le et nous y ferons attention, et nous en saurons l'issue. Ou faites-nous entendre les choses à venir;
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 Annoncez les choses qui arriveront plus tard, et nous saurons que vous êtes des dieux. Faites aussi du bien, ou du mal, et nous l'admirerons, et nous l'observerons ensemble.
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Voici, vous êtes moins que rien, et ce que vous faites est le néant même; c'est une abomination, que de se complaire en vous.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Je l'ai suscité de l'Aquilon, et il est venu; de l'Orient il invoquera mon nom; il marche sur les princes comme sur la boue, comme le potier foule l'argile.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Qui l'a déclaré dès le commencement, pour que nous le sachions? Qui l'a dit à l'avance, que nous disions: Il est juste? Mais personne ne l'a déclaré, personne ne l'a fait entendre, personne n'a entendu vos paroles.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 C'est moi, qui le premier ai dit à Sion: Les voici, les voici; j'enverrai à Jérusalem un messager de bonnes nouvelles.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 J'ai regardé, il n'y avait personne, point de conseiller à consulter parmi eux, pour qu'on répondit.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Voilà, ils ne sont tous que vanité; leurs ouvrages ne sont que néant, et leurs idoles de fonte qu'un vain souffle!
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.